< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
respondens autem Iob dixit
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
ergo vos estis soli homines et vobiscum morietur sapientia
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
et mihi est cor sicut et vobis nec inferior vestri sum quis enim haec quae nostis ignorat
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
qui deridetur ab amico suo sicut ego invocabit Deum et exaudiet eum deridetur enim iusti simplicitas
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
lampas contempta apud cogitationes divitum parata ad tempus statutum
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
abundant tabernacula praedonum et audacter provocant Deum cum ipse dederit omnia in manibus eorum
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
nimirum interroga iumenta et docebunt te et volatilia caeli et indicabunt tibi
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
loquere terrae et respondebit tibi et narrabunt pisces maris
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
quis ignorat quod omnia haec manus Domini fecerit
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
in cuius manu anima omnis viventis et spiritus universae carnis hominis
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
nonne auris verba diiudicat et fauces comedentis saporem
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
in antiquis est sapientia et in multo tempore prudentia
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
apud ipsum est sapientia et fortitudo ipse habet consilium et intellegentiam
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
si destruxerit nemo est qui aedificet et si incluserit hominem nullus est qui aperiat
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
si continuerit aquas omnia siccabuntur et si emiserit eas subvertent terram
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
apud ipsum est fortitudo et sapientia ipse novit et decipientem et eum qui decipitur
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
adducit consiliarios in stultum finem et iudices in stuporem
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
balteum regum dissolvit et praecingit fune renes eorum
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
ducit sacerdotes inglorios et optimates subplantat
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
commutans labium veracium et doctrinam senum auferens
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
effundit despectionem super principes et eos qui oppressi fuerant relevans
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
qui revelat profunda de tenebris et producit in lucem umbram mortis
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
qui multiplicat gentes et perdet eas et subversas in integrum restituet
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
qui inmutat cor principum populi terrae et decipit eos ut frustra incedant per invium
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
palpabunt quasi in tenebris et non in luce et errare eos faciet quasi ebrios

< Yobu 12 >