< Yobu 12 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Felélt Jób és mondta:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
Valóban, ti vagytok ám a nép, s veletek kihal a bölcsesség!
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
Nekem is van szívem mint nektek, nem esem messze tőletek, hisz kinél nem volnának effélék?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Nevetségéül vagyok barátnak, ki Istent szólította s ő meghallgatta; nevetségül az igaz, a gáncstalan!
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
A balvégzetnek megvetés, a gondtalannak vélekedése szerint, készen áll, a tántorgó lábúaknak.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
Boldogságban vannak a rablók sátrai és biztosság azoké, kik Istent haragítják, azé, ki istenét kezében hordja.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
Azonban kérdezd csak meg a barmot, majd tanít téged, s az ég madarát, majd megjelenti neked;
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
vagy szólj a földnek, majd tanít téged, és elbeszélik neked a tenger halai.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Ki ne tudná mindezekből, hogy az Örökkévaló keze cselekedte ezt;
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
kinek kezében van minden élőnek a lelke, s minden ember testének a szelleme.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Nemde a fül vizsgálja a szavakat s az íny az ételt ízleli meg?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
Aggastyánokban van bölcsesség, s hosszú élet: értelmesség.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
Ő nála van bölcsesség és erő, övé tanács és értelmesség!
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Lám, lerombol s nem építtetik föl, rázár valakire s nem nyittatik ki neki.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Im elrekeszt vizeket s kiszáradnak – megereszti őket s feldúlják a földet.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
Ő nála van hatalom és üdvösség, övé a tévelygő és a megtévesztő.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Járatja a tanácsosokat megfosztottan s a bírákat megtébolyítja;
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
a királyok kötelékét föloldotta és reákötött övet az ő derekukra;
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
járatja a papokat megfosztottan s a szilárdakat elferdíti;
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
megvonja a biztosszavúak beszédjét s a véneknek eszét elveszi;
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
csúfot önt a nemesekre s a hatalmasoknak kötését meglazítja.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Feltár mély dolgokat a sötétségből s kihozza világosságra a vakhomályt.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Nagyra növeszti a nemzeteket s elveszíti, kiterjeszti a nemzeteket és elviszi.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Szívét veszi az ország népe fejeinek s eltévelyíti úttalan pusztaságban;
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
tapogatóznak sötétségben világosság nélkül, s eltévelyíti őket mint a részeget.