< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Et Job, répondant, dit:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
Ainsi vous, vous êtes les seuls hommes, et avec vous mourra la sagesse?
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
J’ai cependant un cœur comme vous, et je ne vous suis pas inférieur; qui, en effet, ignore ce que vous savez?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Celui qui est raillé par son ami comme moi invoquera Dieu, et Dieu l’exaucera; car la simplicité du juste est tournée en dérision.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
C’est une lampe méprisée dans les pensées des riches, mais préparée pour un temps marqué.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
Les tentes des voleurs sont dans l’abondance, et ils provoquent audacieusement Dieu, quoique ce soit lui qui ait mis toutes choses en leurs mains.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
Certes, interroge les bêtes, et elles te l’enseigneront; et les volatiles du ciel, et ils te l’indiqueront.
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Parle à la terre, et elle te répondra; et les poissons de la mer te le raconteront.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Qui ignore que la main du Seigneur a fait toutes ces choses?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
C’est dans sa main qu’est l’âme de tout vivant, et l’esprit de toute chair d’homme.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Est-ce que l’oreille ne discerne pas les paroles, et le palais de celui qui mange la saveur des aliments?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
Dans les vieillards est la sagesse, et dans une longue vie la prudence.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
En Dieu sont la sagesse et la force; c’est lui qui possède le conseil et la prudence.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
S’il détruit, il n’y a personne pour édifier; s’il enferme un homme, nul ne pourra lui ouvrir.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
S’il retient les eaux, tout se desséchera; et, s’il les lâche, elles ravageront la terre.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
En lui sont la force et la sagesse: il connaît et celui qui trompe et celui qui est trompé.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Il amène les conseillers à une fin insensée, et les juges à l’étourdissement.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
Il délie le baudrier des rois, et ceint leurs reins d’une corde.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Il fait que les prêtres vont sans gloire, et il renverse les grands;
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
Changeant le langage des hommes véridiques, et enlevant la science des vieillards.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
Il verse le mépris sur les princes, en relevant ceux qui avaient été opprimés.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
C’est lui qui découvre les profondeurs des ténèbres, et produit à la lumière l’ombre de la mort.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
C’est lui qui multiplie les nations et les perd, et qui, après les avoir renversées, les rétablit entièrement.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
C’est lui qui change le cœur des princes du peuple de la terre; qui les trompe, afin qu’ils marchent par où il n’y a point de voie.
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Ils tâtonneront comme dans les ténèbres, et ils ne marcheront pas à la lumière, et il les fera chanceler comme des hommes ivres.

< Yobu 12 >