< Yobu 12 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Mais Job répondit, et dit:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
Vraiment, êtes-vous tout un peuple; et la sagesse mourra-t-elle avec vous?
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
J'ai du bon sens aussi bien que vous, et je ne vous suis point inférieur; et qui [est-ce qui ne sait] de telles choses?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Je suis un homme qui est en risée à son ami, [mais] qui invoquera Dieu, et Dieu lui répondra. On se moque d'un homme qui est juste et droit.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
Celui dont les pieds sont tout prêts à glisser, est selon la pensée de celui qui est à son aise, un flambeau dont on ne tient plus de compte.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
Ce sont les tentes des voleurs [qui] prospèrent, et ceux-là sont assurés qui irritent le [Dieu] Fort, et ils sont ceux à qui Dieu remet tout entre les mains.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
Et, en effet, je te prie, interroge les bêtes, et [chacune d'elles] t'enseignera; ou les oiseaux des cieux, et ils te le déclareront;
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Ou parle à la terre, et elle t'enseignera; même les poissons de la mer te le raconteront;
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Qui est-ce qui ne sait toutes ces choses, [et] que c'est la main de l'Eternel qui a fait cela?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
[Car c'est lui] en la main duquel est l'âme de tout ce qui vit, et l'esprit de toute chair humaine.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
L'oreille ne discerne-t-elle pas les discours, ainsi que le palais savoure les viandes?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
La sagesse est dans les vieillards, et l'intelligence [est le fruit] d'une longue vie.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
Mais en lui est la sagesse et la force; à lui appartient le conseil et l'intelligence.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Voilà, il démolira, et on ne rebâtira point; s'il ferme sur quelqu'un, on n'ouvrira point.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Voilà, il retiendra les eaux, et tout deviendra sec; il les lâchera, et elles renverseront la terre.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
En lui est la force et l'intelligence; à lui est celui qui s'égare, et celui qui le fait égarer.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Il emmène dépouillés les conseillers, et il met hors du sens les juges.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
Il détache la ceinture des Rois, et il serre leurs reins de sangles.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Il emmène nus ceux qui sont en autorité, et il renverse les forts.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
Il ôte la parole à ceux qui sont les plus assurés en leurs discours, et il prive de sens les anciens.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
Il répand le mépris sur les principaux; il rend lâche la ceinture des forts.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Il met en évidence les choses qui étaient cachées dans les ténèbres, et il produit en lumière l'ombre de la mort.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Il multiplie les nations, et les fait périr; il répand çà et là les nations, et puis il les ramène.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Il ôte le cœur aux Chefs des peuples de la terre, et les fait errer dans les déserts où il n'y a point de chemin.
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Ils vont à tâtons dans les ténèbres, sans aucune clarté, et il les fait chanceler comme des gens ivres.