< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
And Job answers and says:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
“Truly—you [are] the people, and wisdom dies with you.
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
I also have a heart like you, I am not fallen more than you, And with whom is there not like these?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
I am a laughter to his friend: He calls to God, and He answers him, A laughter [is] the perfect righteous one.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
A torch—despised in the thoughts of the secure Is prepared for those sliding with the feet.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
The tents of spoilers are at peace, And those provoking God have confidence, Into whose hand God has brought.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
And yet, now ask [one of] the beasts, And it shows you, And a bird of the heavens, And it declares to you.
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Or talk to the earth, and it shows you, And fishes of the sea recount to you:
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Who has not known in all these, That the hand of YHWH has done this?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
In whose hand [is] the breath of every living thing, And the spirit of all flesh of man.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Does the ear not try words? And the palate taste food for itself?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
With the very aged [is] wisdom, And [with] length of days [is] understanding.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
With Him [are] wisdom and might, To Him [are] counsel and understanding.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Behold, He breaks down, and it is not built up, He shuts against a man, And it is not opened.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Behold, He keeps in the waters, and they are dried up, And He sends them forth, And they overturn the land.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
With Him [are] strength and wisdom, His the deceived and deceiver.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Causing counselors to go away [as] a spoil, Indeed, He makes fools of judges.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
He has opened the bands of kings, And He binds a girdle on their loins.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Causing ministers to go away [as] a spoil And strong ones He overthrows.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
Turning aside the lip of the steadfast, And the reason of the aged He takes away.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
Pouring contempt on princes, And the girdle of the mighty He made feeble.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Removing deep things out of darkness, And He brings out to light death-shade.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Magnifying the nations, and He destroys them, Spreading out the nations, and He quiets them.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Turning aside the heart Of the heads of the people of the land, And He causes them to wander In vacancy—no way!
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
They feel darkness, and not light, He causes them to wander as a drunkard.”

< Yobu 12 >