< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
約伯回答說:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
你們真是子民哪, 你們死亡,智慧也就滅沒了。
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
但我也有聰明,與你們一樣, 並非不及你們。 你們所說的,誰不知道呢?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
我這求告上帝、蒙他應允的人 竟成了朋友所譏笑的; 公義完全人竟受了人的譏笑。
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
安逸的人心裏藐視災禍; 這災禍常常等待滑腳的人。
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
強盜的帳棚興旺, 惹上帝的人穩固, 上帝多將財物送到他們手中。
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
你且問走獸,走獸必指教你; 又問空中的飛鳥,飛鳥必告訴你;
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
或與地說話,地必指教你; 海中的魚也必向你說明。
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
看這一切, 誰不知道是耶和華的手做成的呢?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
凡活物的生命和人類的氣息都在他手中。
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
耳朵豈不試驗言語, 正如上膛嘗食物嗎?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
年老的有智慧; 壽高的有知識。
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
在上帝有智慧和能力; 他有謀略和知識。
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
他拆毀的,就不能再建造; 他捆住人,便不得開釋。
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
他把水留住,水便枯乾; 他再發出水來,水就翻地。
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
在他有能力和智慧, 被誘惑的與誘惑人的都是屬他。
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
他把謀士剝衣擄去, 又使審判官變成愚人。
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
他放鬆君王的綁, 又用帶子捆他們的腰。
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
他把祭司剝衣擄去, 又使有能的人傾敗。
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
他廢去忠信人的講論, 又奪去老人的聰明。
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
他使君王蒙羞被辱, 放鬆有力之人的腰帶。
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
他將深奧的事從黑暗中彰顯, 使死蔭顯為光明。
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
他使邦國興旺而又毀滅; 他使邦國開廣而又擄去。
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
他將地上民中首領的聰明奪去, 使他們在荒廢無路之地漂流;
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
他們無光,在黑暗中摸索, 又使他們東倒西歪,像醉酒的人一樣。

< Yobu 12 >