< Yobu 12 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
約伯回答說:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
的確,只有你們是有知識的子民;那麼,你們一死,智慧也與你們一同喪亡!
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
其實,我和你們有同樣的心理,我並不亞於你們! 誰不知道這些事﹖
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
我這呼籲天主而蒙應允的人,卻被他的友人所嘲笑,無辜的義人卻成了笑柄。
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
幸運的人心想:遭難的人應受蔑視,失足的人應再予以打擊。
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
但是,強盜的帳幕竟能安全,觸怒天主的人,以勢力為神的人卻享平安。
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
請你詢問走獸,牠們也會開導你;詢問天上的飛鳥,牠們也會告訴你;
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
地上的爬蟲也會教訓你,海中的魚族也會給你說明。
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
牠們中有誰不知道:是天主的手創造了這一切﹖
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
因為一切活物的生魂,一切血肉之人的靈魂,都握在他手中。
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
耳朵不是為明辨言語,口腔不是為辨嘗食物嗎﹖
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
白髮老人是有智慧的,年紀大者是有見識的;
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
但智慧和能力同在天主內,智慧與見識是天主所有。
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
他若拆毀,人不能再建;他若拘禁,人不得開釋。
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
他若制水,水便乾涸;他若放水,水便沖毀大地。
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
力量與才能,為他所有;受騙者與騙人者,都屬於他。
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
他使謀士糊塗,使判官愚蠢;
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
他解除君王所繫的玉帶,將繩索捆在他們的腰間;
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
他使司祭赤足而行,推倒掌握大權者;
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
奪去忠貞者的辯才,剝去年老者的理智:
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
使貴人備受侮辱,使勇士的腰帶鬆弛;
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
使隱秘的事由暗處彰顯,使黑暗進入光明;
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
使邦國興起而又滅亡,使民族強大而又消散;
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
剝去國君的理智,使他們漂泊於無路的荒野中,
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
在無光的黑暗中摸索,踉蹌猶如醉漢。