< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Тогава Иов в отговор рече:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
Наистина само вие сте люде, И с вас ще умре мъдростта!
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
Но и аз имам разум както и вие; Не съм по-долен от вас; И такива работи, кой ги не знае?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Станах за поругание на ближния си, Човек, който призовавах Бога, и Той му отговаряше, - Праведният, непорочният човек стана за поругание!
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
Тоя, чиито нозе са близо до подхлъзване, Е като презрян светилник в мисълта на благополучния.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
Шатрите на разбойниците са в благоденствие, И тия, които разгневяват Бога, са в безопасност; Бог докарва изобилие в ръцете им.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
Но попитай сега животните, и те ще те научат, И въздушните птици, и те ще ти кажат;
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Или говори на земята, и тя ще те научи, И морските риби ще ти изявят.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
От всички тия кой не разбира, Че ръката на Господа е сторила това?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
В Чиято ръка е душата на всичко живо, И дишането на цялото човечество.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Ухото не изпитва ли думите Както небцето вкусва ястието си?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
Мъдростта е у белокосите, казвате вие, И разумът в дългия живот.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
А у Бога е мъдростта и силата; Той има разсъждение и разум.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Ето, Той събаря, и не съгражда вече; Затваря човека, и не му се отваря.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Ето, задържа водите, и пресъхват; Пуща ги пак, и изравят земята.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
У Него е силата и мъдростта; Негов е измаменият и измамникът.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Закарва съветниците ограбени, И прави съдиите глупави.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
Разпасва пояса на царете, И опасва кръста им с въже.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Закарва първенците ограбени, И поваля силните.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
Отнема думата от ползуващите се с доверие, И взема ума на старейшините.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
Излива презрение върху князете, И ослабва силата на яките.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Открива дълбоки работи из тъмнината, И изважда на видело мрачната сянка.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Умножава народите, и погубва ги, Разширява народите, и стеснява ги.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Отнема бодростта на началниците на земните жители, И прави ги да се скитат по непроходна пустиня;
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Пипат в тъмнината без виделина, И прави ги да залитат като пиян.

< Yobu 12 >