< Yobu 11 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Y respondió Sofar Naamatita, y dijo:
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
¿Las muchas palabras, no han de tener respuesta? ¿Y el hombre parlero será justificado?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
¿Tus mentiras harán callar los hombres? ¿y harás escarnio, y no habrá quien te avergüence?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
Tú dices: Mi manera de vivir es pura, y yo soy limpio delante de tus ojos.
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
Mas, ¡oh quién diera que Dios hablara, y abriera sus labios contigo!
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
Y que te declarara los secretos de la sabiduría: porque dos tantos mereces según la ley; y sabe que Dios te ha olvidado por tu iniquidad.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
¿Alcanzarás tú el rastro de Dios? ¿llegarás tú a la perfección del Todopoderoso?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
Es más alto que los cielos, ¿qué harás? es más profundo que el infierno, ¿cómo le conocerás? (Sheol h7585)
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Su medida es más larga que la tierra, y más ancha que la mar.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
Si cortare, o encerrare, o juntare, ¿quién le responderá?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
Porque el conoce a los hombres vanos: y ve la iniquidad, ¿y no entenderá?
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
El hombre vano se hará entendido, aunque nazca como el pollino del asno montés.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
Si tú preparares tu corazón, y extendieres a él tus manos:
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
Si alguna iniquidad está en tu mano, y la echares de ti, y no consintieres que en tus habitaciones more maldad:
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Entonces levantarás tu rostro de mancha, y serás fuerte, y no temerás;
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
Y olvidarás tu trabajo, y te acordarás de él, como de aguas que pasaron.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
Y en mitad de la siesta se levantará bonanza: resplandecerás, y serás como la mañana.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
Y confiarás, que habrá esperanza; y cabarás, y dormirás seguro.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
Y acostarte has, y no habrá quien te espante; y muchos te rogarán.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
Mas los ojos de los malos se consumirán, y no tendrán refugio; y su esperanza será dolor de alma.

< Yobu 11 >