< Yobu 11 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Potem je odgovoril Cofár Naámčan in rekel:
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
»Mar ne bo množica besed odgovorjena? Mar naj bo mož, poln govora, opravičen?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Mar naj tvoje laži naredijo možem, da molčijo? In ko zasmehuješ, ali te noben človek ne bo osramotil?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
Kajti rekel si: ›Moj nauk je čist in jaz sem čist v tvojih očeh.‹
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
Toda oh, da bi Bog spregovoril in zoper tebe odprl svoje ustnice
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
in da bi ti pokazal skrivnosti modrosti, da so dvojne temu kar je! Vedi torej, da Bog od tebe terja manj, kakor zasluži tvoja krivičnost.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Mar lahko z iskanjem najdeš Boga? Mar lahko do popolnosti spoznaš Vsemogočnega?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
To je tako visoko kakor nebo. Kaj lahko storiš? Globlje kakor pekel. Kaj lahko spoznaš? (Sheol )
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Njegova mera je daljša kakor zemlja in širša kakor morje.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
Če odseka in zapre, ali zbere skupaj, kdo ga potem lahko ovira?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
Kajti pozna praznoglave ljudi. Tudi zlobnost vidi. Mar ne bo potem tega preudaril?
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
Kajti praznoglav človek bi bil moder, čeprav bi bil človek rojen kakor žrebe divjega osla.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
Če pripraviš svoje srce in svoje roke iztegneš k njemu,
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
če je krivičnost v tvoji roki, jo odloži daleč proč in naj zlobnost ne prebiva v tvojih šotorih.
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Kajti potem boš povzdignil svoj obraz brez madeža. Da, neomajen boš in se ne boš bal,
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
ker boš pozabil svojo bedo in se je boš spominjal kakor vode, ki tečejo mimo,
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
in tvoja starost bo jasnejša kakor opoldan; svetil boš naprej, ti boš kakor jutro.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
Ti boš varen, ker je upanje. Da, kopal boš okoli sebe in svoj počitek si boš vzel v varnosti.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
Tudi ulegel se boš in nihče te ne bo strašil. Da, mnogi te bodo obžalovali.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
Toda oči zlobnih bodo odpovedale in ne bodo pobegnili in njihovo upanje bo kakor izročitev duha.«