< Yobu 11 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Respondens autem Sophar Naamathites, dixit:
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
Numquid qui multa loquitur, non et audiet? aut vir verbosus iustificabitur?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Tibi soli tacebunt homines? et cum ceteros irriseris, a nullo confutaberis?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
Dixisti enim: Purus est sermo meus, et mundus sum in conspectu tuo.
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
Atque utinam Deus loqueretur tecum, et aperiret labia sua tibi,
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
Ut ostenderet tibi secreta sapientiae, et quod multiplex esset lex eius, et intelligeres quod multo minora exigaris ab eo, quam meretur iniquitas tua.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Forsitan vestigia Dei comprehendes, et usque ad perfectum Omnipotentem reperies?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
Excelsior caelo est, et quid facies? profundior inferno, et unde cognosces? (Sheol h7585)
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Longior terra mensura eius, et latior mari.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
Si subverterit omnia, vel in unum coarctaverit, quis contradicet ei?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
Ipse enim novit hominum vanitatem, et videns iniquitatem, nonne considerat?
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
Vir vanus in superbiam erigitur, et tamquam pullum onagri se liberum natum putat.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
Tu autem firmasti cor tuum, et expandisti ad eum manus tuas.
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
Si iniquitatem, quae est in manu tua, abstuleris a te, et non manserit in tabernaculo tuo iniustitia:
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Tunc levare poteris faciem tuam absque macula, et eris stabilis, et non timebis.
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
Miseriae quoque oblivisceris, et quasi aquarum quae praeterierunt recordaberis.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
Et quasi meridianus fulgor consurget tibi ad vesperam: et cum te consumptum putaveris, orieris ut lucifer.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
Et habebis fiduciam, proposita tibi spe, et defossus securus dormies.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
Requiesces, et non erit qui te exterreat: et deprecabuntur faciem tuam plurimi.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
Oculi autem impiorum deficient, et effugium peribit ab eis, et spes illorum abominatio animae.

< Yobu 11 >