< Yobu 11 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Et Zophar de Naama prit la parole et dit:
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
A tant de paroles ne répondra-t-on point? Et l'homme aux discours aura-t-il gain de cause?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
A tes vains propos des hommes se tairont-ils, pour que tu te moques, sans que nul te réponde,
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
que tu dises: Ma doctrine est pure; et je suis net à Tes yeux?
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
Mais que Dieu veuille parler, et ouvrir ses lèvres contre toi,
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
pour te révéler les mystères d'une sagesse double de notre prudence! et tu verras que pour toi Dieu oublie une partie de ton crime.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Atteindras-tu à la portée de Dieu? A la science parfaite du Tout-puissant atteindras-tu?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
C'est la hauteur des Cieux! que ferais-tu? plus que la profondeur des Enfers! que saurais-tu? (Sheol h7585)
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Elle mesure en longueur plus que la terre, en largeur plus que la mer.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
S'Il se porte agresseur, s'Il saisit, s'il convoque, qui l'arrêtera?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
Car Il connaît les hommes méchants, et voit le mal, sans effort d'attention.
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
Mais l'homme est stupide dans sa sagacité, et le poulain de l'onagre naît l'égal d'un humain.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
Mais si tu diriges bien ton cœur, et que tu tendes vers Lui tes mains,
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
(secoue le mal qui est en ta main, et ne laisse pas l'iniquité loger dans ta tente!)
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
alors tu lèveras la tête sans reproche, tu seras ferme et sans crainte;
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
alors tu oublieras ta peine; il t'en souviendra comme d'eaux écoulées;
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
la vie surgira plus claire que le midi; assombri, tu seras comme le matin;
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
tu auras de l'assurance, car il y aura espérance; outragé, tu te coucheras tranquille;
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
dans ton repos, nul ne te troublera, et plusieurs flatteront ton visage.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
Mais les yeux des impies se consumeront, la retraite leur sera coupée, et leur espoir sera un dernier soupir.

< Yobu 11 >