< Yobu 11 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Alors Zophar, le Naamathite, prit la parole,
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
« Ne faut-il pas répondre à la multitude de mots? Un homme plein de paroles doit-il être justifié?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Vos fanfaronnades devraient-elles inciter les hommes à se taire? Quand tu te moques, personne ne te fait honte?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
Car vous dites: « Ma doctrine est pure ». Je suis propre à vos yeux.
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
Mais oh, que Dieu parle, et ouvrir ses lèvres contre toi,
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
qu'il te montre les secrets de la sagesse! Car la vraie sagesse a deux côtés. Sachez donc que Dieu exige de vous moins que ce que votre iniquité mérite.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
« Pouvez-vous sonder le mystère de Dieu? Ou pouvez-vous sonder les limites du Tout-Puissant?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
Ils sont hauts comme le ciel. Que pouvez-vous faire? Ils sont plus profonds que le Sheol. Que pouvez-vous savoir? (Sheol h7585)
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Sa mesure est plus longue que la terre, et plus large que la mer.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
S'il passe, ou s'il enferme, ou convoque un tribunal, alors qui peut s'opposer à lui?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
Car il connaît les faux hommes. Il voit aussi l'iniquité, même s'il ne la considère pas.
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
Un homme à la tête vide devient sage quand un homme naît comme le petit d'une ânesse sauvage.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
« Si tu mets ton cœur à l'endroit, tendez vos mains vers lui.
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
Si l'iniquité est dans ta main, éloigne-la. Ne laissez pas l'iniquité habiter dans vos tentes.
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Alors tu lèveras ton visage sans tache. Oui, vous serez inébranlables, et vous ne craindrez pas,
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
car tu oublieras ta misère. Vous vous en souviendrez comme des eaux qui sont passées.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
La vie sera plus claire que l'aurore. Même s'il y a des ténèbres, ce sera comme le matin.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
Vous serez en sécurité, car il y a de l'espoir. Oui, vous chercherez, et vous vous reposerez en sécurité.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
Tu te coucheras aussi, et personne ne te fera peur. Oui, beaucoup vont vous courtiser.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
Mais les yeux des méchants se perdront. Ils n'auront aucun moyen de fuir. Leur espoir sera l'abandon de l'esprit. »

< Yobu 11 >