< Yobu 11 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Then responded Zophar the Naamathite, and said: —
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
Should, the multitude of words, not be answered? Or should, a man full of talk, be justified?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Shall, thy pratings, cause men to hold their peace? When thou hast mocked, shall there be none to put thee to shame?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
Since thou hast said, Right is my doctrine, and pure am I in his eyes.
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
But, in very deed, oh that GOD would speak, that he would open his lips with thee:
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
That he would declare to thee the secrets of wisdom, for they are double to that which actually is, —Know then that GOD could bring into forgetfulness for thee, a portion of thine iniquity.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
The hidden depth of GOD canst thou discover? Or, unto the furthest limit of the Almighty, canst thou attain?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
The heights of the heavens, what canst thou do? Depths deeper than hades, what canst thou know? (Sheol )
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Longer than the earth, is the measure thereof, and broader than the sea.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
If he sweep on, or shut up, or call together, Who then shall hinder him?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
For, he, knoweth men of falsity, and seeth iniquity, and him that doth not diligently consider.
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
But, an empty person, will get sense, when, a wild ass’s colt, is born a man!
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
If, thou, hast prepared thy heart, and wilt spread forth, unto him, thy hands—
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
If, iniquity, be in thy hand, Put it far away, and let there not dwell in thy tents perversity,
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Surely, then, shalt thou lift up thy face free from blemish, and shalt be established, and not fear.
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
For, now, shalt thou forget, sorrow, Like waters passed away, shalt thou remember it.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
Above high noon, shall rise life’s continuance, Darkness, like a morning, shall appear,
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
And thou shalt he confident, that there is hope, and, when thou hast searched, securely shalt thou lie down;
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
And shalt rest, with none to put thee in terror, —and many shall entreat thy favour.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
But, the eyes of the lawless, shall fail, —and, place of refuge, shall have vanished from them, and, their hope, be a breathing out of life.