< Yobu 11 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Then Sophar the Naamathite answered, and said:
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
Shall not he that speaketh much, hear also? or shall a man full of talk be justified?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Shall men hold their peace to thee only? and when thou hast mocked others, shall no man confute thee?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
For thou hast said: My word is pure, and I am clean in thy sight.
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
And I wish that God would speak with thee, and would open his lips to thee,
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
That he might shew thee the secrets of wisdom, and that his law is manifold, and thou mightest understand that he exacteth much less of thee, than thy iniquity deserveth.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Peradventure thou wilt comprehend the steps of God, and wilt find out the Almighty perfectly?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
He is higher than heaven, and what wilt thou do? he is deeper than hell, and how wilt thou know? (Sheol )
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
The measure of him is longer than the earth, and broader than the sea.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
If he shall overturn all things, or shall press them together, who shall contradict him?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
For he knoweth the vanity of men, and when he seeth iniquity, doth he not consider it?
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
A vain man is lifted up into pride, and thinketh himself born free like a wild ass’s colt.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
Rut thou hast hardened thy heart, and hast spread thy hands to him.
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
If thou wilt put away from thee the iniquity that is in thy hand, and lot not injustice remain in thy tabernacle:
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Then mayst thou lift up thy face without spot, and thou shalt be steadfast, and shalt not fear.
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
Thou shalt also forget misery, and remember it only as waters that are passed away.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
And brightness like that of the noonday, shall arise to thee at evening: and when thou shalt think thyself consumed, thou shalt rise as the day star.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
And thou shalt have confidence, hope being set before thee, and being buried thou shalt sleep secure.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
Thou shalt rest, and there shall be none to make thee afraid: and many shall entreat thy face.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
But the eyes of the wicked shall decay, and the way to escape shall fail them, and their hope the abomination of the soul.