< Yobu 11 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Then Sophar the Minaean answered and said,
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
He that speaks much, should also hear on the other side: or does the fluent speaker think himself to be righteous? blessed [is] the short lived offspring of woman.
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Be not a speaker of many words; for is there none to answer you?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
For say not, I am pure in my works, and blameless before him.
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
But oh that the Lord would speak to you, and open his lips to you!
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
Then shall he declare to you the power of wisdom; for it shall be double of that which is with you: and then shall you know, that a just recompence of your sins has come to you from the Lord.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Will you find out the traces of the Lord? or have you come to the end [of that] which the Almighty has made?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
Heaven [is] high; and what will you do? and there are deeper things than those in hell; what do you know? (Sheol )
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Or longer than the measure of the earth, or the breadth of the sea.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
And if he should overthrow all things, who will say to him, What have you done?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
For he knows the works of transgressors; and when he sees wickedness, he will not overlook [it].
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
But man vainly buoys himself up with words; and a mortal born of woman [is] like an ass in the desert.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
For if you have made your heart pure, and lift up [your] hands towards him;
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
if there is any iniquity in your hands, put if far from you, and let not unrighteousness lodge in your habitation.
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
For thus shall your countenance shine again, as pure water; and you shall dive yourself of uncleanness, and shall not fear.
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
And you shall forget trouble, as a wave that has passed by; and you shall not be scared.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
And your prayer [shall be] as the morning star, and life shall arise to you [as] from the noonday.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
And you shall be confident, because you have hope; and peace shall dawn to you from out of anxiety and care.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
For you shall be at ease, and there shall be no one to fight against you; and many shall charge, and make supplication to you.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
But safety shall fail them; for their hope is destruction, and the eyes of the ungodly shall waste away.