< Yobu 1 >

1 Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
Il y avait dans le pays d’Uts un homme dont le nom était Job; et cet homme était parfait et droit, craignant Dieu et se retirant du mal.
2 Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
Et il lui naquit sept fils et trois filles;
3 ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
et il possédait 7 000 brebis, et 3 000 chameaux, et 500 paires de bœufs, et 500 ânesses; et [il avait] un très grand nombre de serviteurs; et cet homme était plus grand que tous les fils de l’orient.
4 Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
Et ses fils allaient et faisaient un festin, chacun dans [sa] maison, à son jour; et ils envoyaient appeler leurs trois sœurs pour manger et pour boire avec eux.
5 Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
Et il arrivait que, quand les jours de festin étaient terminés, Job envoyait [vers eux] et les sanctifiait: il se levait de bonne heure le matin et offrait des holocaustes selon leur nombre à tous, car Job disait: Peut-être mes fils ont-ils péché et ont-ils maudit Dieu dans leurs cœurs. Job faisait toujours ainsi.
6 Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
Or, un jour, il arriva que les fils de Dieu vinrent se présenter devant l’Éternel, et Satan aussi vint au milieu d’eux.
7 Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Et l’Éternel dit à Satan: D’où viens-tu? Et Satan répondit à l’Éternel et dit: De courir çà et là sur la terre et de m’y promener.
8 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
Et l’Éternel dit à Satan: As-tu considéré mon serviteur Job, qu’il n’y a sur la terre aucun homme comme lui, parfait et droit, craignant Dieu, et se retirant du mal?
9 Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
Et Satan répondit à l’Éternel et dit: Est-ce pour rien que Job craint Dieu?
10 “Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
Ne l’as-tu pas, toi, entouré de toutes parts d’une haie de protection, lui, et sa maison, et tout ce qui lui appartient? Tu as béni le travail de ses mains, et tu as fait abonder son avoir sur la terre.
11 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Mais étends ta main et touche à tout ce qu’il a: [tu verras] s’il ne te maudit pas en face.
12 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
Et l’Éternel dit à Satan: Voici, tout ce qu’il a est en ta main, seulement tu n’étendras pas ta main sur lui. Et Satan sortit de la présence de l’Éternel.
13 Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
Et, un jour, il arriva que ses fils et ses filles mangeaient et buvaient du vin dans la maison de leur frère premier-né;
14 wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
et un messager vint à Job et dit: Les bœufs labouraient et les ânesses paissaient auprès d’eux,
15 tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
et ceux de Sheba sont tombés [sur eux] et les ont pris, et ils ont frappé les jeunes hommes par le tranchant de l’épée; et j’ai échappé, moi seul, pour te l’annoncer.
16 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Celui-ci parlait encore, qu’un autre vint et dit: Le feu de Dieu est tombé du ciel et a brûlé les brebis et les jeunes hommes, et les a consumés; et j’ai échappé, moi seul, pour te l’annoncer.
17 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Celui-ci parlait encore, qu’un autre vint et dit: Les Chaldéens ont formé trois bandes, et se sont jetés sur les chameaux et les ont pris, et ils ont frappé les jeunes hommes par le tranchant de l’épée; et j’ai échappé, moi seul, pour te l’annoncer.
18 Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
Celui-ci parlait encore, qu’un autre vint et dit: Tes fils et tes filles mangeaient et buvaient du vin dans la maison de leur frère premier-né,
19 mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
et voici, un grand vent est venu d’au-delà du désert et a donné contre les quatre coins de la maison, et elle est tombée sur les jeunes gens et ils sont morts; et j’ai échappé, moi seul, pour te l’annoncer.
20 Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
Et Job se leva, et déchira sa robe, et rasa sa tête, et se jeta à terre et se prosterna.
21 nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
Et il dit: Nu je suis sorti du sein de ma mère, et nu j’y retournerai; l’Éternel a donné, et l’Éternel a pris; que le nom de l’Éternel soit béni!
22 Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”
En tout cela Job ne pécha pas, et n’attribua rien à Dieu qui soit inconvenable.

< Yobu 1 >