< Yobu 1 >

1 Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
Il y avait au pays d'Uz un homme dont le nom était Job. Cet homme était irréprochable et droit, il craignait Dieu et se détournait du mal.
2 Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
Il lui naquit sept fils et trois filles.
3 ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
Il possédait aussi sept mille moutons, trois mille chameaux, cinq cents paires de bœufs, cinq cents ânes femelles, et une très grande maison, de sorte que cet homme était le plus grand de tous les enfants de l'Orient.
4 Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
Ses fils allèrent faire un festin dans la maison de chacun d'eux le jour de son anniversaire; et ils envoyèrent chercher leurs trois sœurs pour manger et boire avec eux.
5 Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
Lorsque leurs jours de fête furent écoulés, Job les envoya et les sanctifia; il se leva de bon matin et offrit des holocaustes selon leur nombre. Car Job disait: « Il se peut que mes fils aient péché et renoncé à Dieu dans leur cœur. » Et Job ne cessait de le faire.
6 Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
Or, le jour où les fils de Dieu vinrent se présenter devant Yahvé, Satan aussi vint au milieu d'eux.
7 Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Yahvé dit à Satan: « D'où viens-tu? » Alors Satan répondit à Yahvé: « D'aller et de venir sur la terre, et d'y monter et d'y descendre. »
8 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
Yahvé dit à Satan: « As-tu considéré mon serviteur Job? Car il n'y a personne comme lui sur la terre, un homme irréprochable et droit, qui craint Dieu et se détourne du mal. »
9 Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
Alors Satan prit la parole devant Yahvé, et dit: Job craint-il Dieu pour rien?
10 “Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
N'as-tu pas fait une haie autour de lui, autour de sa maison, et autour de tout ce qu'il possède, de tous côtés? Tu as béni l'ouvrage de ses mains, et ses biens se sont accrus dans le pays.
11 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Mais étends maintenant ta main et touche à tout ce qu'il possède, et il te reniera en face. »
12 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
Yahvé dit à Satan: « Voici, tout ce qu'il possède est en ton pouvoir. Seulement sur lui-même, n'étends pas ta main. » Et Satan sortit de la présence de Yahvé.
13 Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
Un jour que ses fils et ses filles mangeaient et buvaient du vin dans la maison de leur frère aîné,
14 wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
un messager vint trouver Job et lui dit: « Les bœufs labouraient, et les ânes paissaient à côté d'eux,
15 tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
mais les Sabéens ont attaqué et les ont emmenés. Oui, ils ont tué les serviteurs au fil de l'épée, et moi seul ai échappé pour te le dire. »
16 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Comme il parlait encore, un autre vint aussi et dit: « Le feu de Dieu est tombé du ciel, il a brûlé les brebis et les serviteurs et les a consumés, et moi seul j'ai échappé pour vous le dire. »
17 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Comme il parlait encore, un autre vint aussi et dit: « Les Chaldéens ont formé trois bandes et se sont jetés sur les chameaux, ils les ont emmenés, oui, et ils ont tué les serviteurs au fil de l'épée; moi seul, j'ai échappé pour vous le dire. »
18 Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
Comme il parlait encore, un autre arriva, et dit: « Tes fils et tes filles mangeaient et buvaient du vin dans la maison de leur frère aîné,
19 mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
et voici qu'un grand vent est venu du désert, il a frappé les quatre coins de la maison, il est tombé sur les jeunes gens, et ils sont morts. Moi seul, je me suis échappé pour vous le dire. »
20 Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
Alors Job se leva, déchira sa robe, se rasa la tête, se jeta à terre et se prosterna.
21 nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
Il dit: « Nu, je suis sorti du ventre de ma mère, et nu, j'y retournerai. Yahvé a donné, et Yahvé a repris. Que le nom de Yahvé soit béni. »
22 Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”
Dans tout cela, Job n'a pas péché, ni accusé Dieu de mal faire.

< Yobu 1 >