< Yeremiya 1 >

1 Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
Słowa Jeremijasza, syna Helkijaszowego, z kapłanów, którzy byli w Anatot, w ziemi Benjamin
2 Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
Do którego stało się słowo Pańskie za dni Jozyjasza, syna Amonowego, króla Judzkiego trzynastego roku królowania jego.
3 Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
A stało się za dni Joakima, syna Jozyjaszowego, króla Judzkiego, aż do skończenia jedenastego roku Sedekijasza, syna Jozyjasza, króla Judzkiego, aż do przeprowadzenia Jeruzalemczyków, miesiąca piątego,
4 Yehova anayankhula nane kuti,
Stało się mówię, słowo Pańskie do mnie, mówiąc
5 “Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
Pierwej niżelim cię utworzył w żywocie, znałem cię, a pierwej niżeliś wyszedł z żywota, poświęciłem cię, za proroka narodom dałem cię.
6 Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
I rzekłem: Ach, ach panujący Panie! Oto nie umiem mówić, bom jest dziecięciem.
7 Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
Ale Pan rzekł do mnie: Nie mów: Jestem dziecięciem, owszem, na wszystko, na co cię poślę, idź, a wszystko, coć rozkażę, mów
8 Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Nie bój się oblicza ich, bom Ja jest z tobą, abym cię wybawił, mówi Pan.
9 Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
A wyciągnąwszy Pan rękę swoję, dotknął się ust moich, i rzekł mi Pan: Otom dał słowa moje do ust twoich.
10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
Oto cię dziś postanawiam nad narodami i nad królestwami, abyś wykorzeniał, i psuł, i wytracał, i obalał, i abyś budował i szczepił.
11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
Potem stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc: Co widzisz Jeremijaszu? I rzekłem: Widzę rózgę migdałową.
12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
I rzekł Pan do mnie: Dobrze widzisz: albowiem się Ja pospieszam z słowem swem, abym je wykonał.
13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
I stało się słowo Pańskie do mnie powtóre, mówiąc: Co widzisz? I rzekłem: Widzę garniec wrzący, a przednia strona jego ku stronie północnej.
14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
I rzekł Pan do mnie: Od północy przypadnie złe na wszystkich mieszkających na tej ziemi.
15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
Bo oto Ja zawołam wszystkich rodzajów z królestw północnych, mówi Pan, aby przyciągnąwszy każdy z nich, postanowił stolicę swoję w wejściu bram Jeruzalemskich i przy wszystkich murach jego, i przy wszystkich miastach Judzkich.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
A tak opowiem sądy moje przeciwko nim dla wszelakiej złości tych, którzy mię opuścili, a kadzili bogom obcym, i kłaniali się robocie rąk swoich.
17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
Przetoż ty przepasz biodra swoje, a wstawszy mów do nich wszystko, co Ja tobie rozkazuję, nie bój się ich bym cię snać nie starł przed obliczem ich,
18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
Bo oto Ja postanawiam cię dziś miastem obronnem, i słupem żelaznym, i murem miedzianym przeciwko tej wszystkiej ziemi, przeciwko królom Judzkim, przeciwko książętom ich, przeciwko kapłanom ich, i przeciwko ludowi tej ziemi;
19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Którzy walczyć będą przeciwko tobie, ale cię nie przemogą: bom Ja z tobą mówi Pan, abym cię wybawił.

< Yeremiya 1 >