< Yeremiya 1 >

1 Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
Paroles de Jérémie, fils de Hilkija, l'un des prêtres qui étaient à Anathoth, dans le pays de Benjamin.
2 Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
La parole de Yahvé lui fut adressée au temps de Josias, fils d'Amon, roi de Juda, la treizième année de son règne.
3 Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
Elle arriva aussi aux jours de Jojakim, fils de Josias, roi de Juda, à la fin de la onzième année de Sédécias, fils de Josias, roi de Juda, jusqu'à la déportation de Jérusalem au cinquième mois.
4 Yehova anayankhula nane kuti,
Or la parole de Yahvé me fut adressée, en ces termes,
5 “Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
« Avant de te former dans le ventre de ta mère, je te connaissais. Avant ta naissance, je t'ai sanctifié. Je t'ai établi prophète des nations. »
6 Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
Et je dis: « Ah! Seigneur Yahvé! Voici, je ne sais pas comment parler, car je suis un enfant. »
7 Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
Mais Yahvé me dit: « Ne dis pas: « Je suis un enfant », car tu iras vers celui que je t'enverrai, et tu diras tout ce que je te commanderai.
8 Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
N'aie pas peur à cause d'eux, car je suis avec toi pour te sauver, dit l'Éternel.
9 Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
Alors Yahvé étendit sa main et toucha ma bouche. Et Yahvé me dit: « Voici, j'ai mis mes paroles dans ta bouche.
10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
Voici, je t'ai établi aujourd'hui sur les nations et sur les royaumes, pour arracher et démolir, pour détruire et renverser, pour bâtir et planter. »
11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
La parole de Yahvé me fut adressée en ces termes: « Jérémie, que vois-tu? » J'ai dit: « Je vois une branche d'amandier. »
12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
Et Yahvé me dit: « Tu as bien vu, car je veille sur ma parole pour l'accomplir. »
13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
La parole de Yahvé me fut adressée pour la seconde fois, en disant: « Que vois-tu? » J'ai dit: « Je vois un chaudron en ébullition, et il bascule vers le nord. »
14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
Alors Yahvé me dit: « Du nord, le mal se répandra sur tous les habitants du pays.
15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
Car voici, j'appellerai toutes les familles des royaumes du nord, dit l'Éternel. « Ils viendront, et ils placeront chacun leur trône à l'entrée des portes de Jérusalem, et contre toutes ses murailles tout autour, et contre toutes les villes de Juda.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
Je prononcerai contre eux mes jugements sur toute leur méchanceté, en ce qu'ils m'ont abandonné, et ont brûlé de l'encens à d'autres dieux, et adoraient les œuvres de leurs propres mains.
17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
« Mets donc ta ceinture à ta taille, lève-toi, et dis-leur tout ce que je t'ordonne. Ne t'effraie pas devant eux, de peur que je ne t'effraie devant eux.
18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
Car voici, je fais de toi aujourd'hui une ville fortifiée, une colonne de fer et des murs de bronze contre tout le pays, contre les rois de Juda, contre ses princes, contre ses prêtres et contre le peuple du pays.
19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Ils te combattront, mais ils ne te vaincront pas, car je suis avec toi, dit l'Éternel, pour te secourir. »

< Yeremiya 1 >