< Yeremiya 9 >
1 Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
“Who will provide water for my head, and a fount of tears for my eyes? And then I will weep day and night for the slain of the daughter of my people.
2 Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
Who will provide me, in the wilderness, with a lodging place along the road? And then I will forsake my people, and withdraw from them. For they are all adulterers, a union of transgressors.
3 “Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
And they have bent their tongue, like a bow, to send forth lies and not the truth. They have been strengthened upon the earth. And they have gone from one evil to another. But they have not known me, says the Lord.
4 “Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
Let each one guard himself against his neighbor, and let him have no trust in any brother of his. For every brother will utterly overthrow, and every friend will advance deceitfully.
5 Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
And a man will deride his brother, and they will not speak the truth. For they have taught their tongue to speak lies; they have labored to commit iniquity.
6 Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
Your habitation is in the midst of deceit. In their deceitfulness, they have refused to know me, says the Lord.”
7 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
Because of this, thus says the Lord of hosts: “Behold, I will refine them, and I will test them. For what else can I do before the face of the daughter of my people?
8 Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
Their tongue is a wounding arrow; it has spoken deceit. With his mouth, he speaks peace with his friend, and then he secretly lies in ambush for him.
9 Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
Shall I not visit upon them concerning these things, says the Lord? Or shall my soul not take vengeance on a nation of this kind?
10 Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
I will take up weeping and lamentation over the mountains, and mourning over the beautiful places in the desert. For they have been scorched because no man is passing through them. And they have not heard the voice of any occupant. From the birds of the air, even to the cattle, they have migrated and withdrawn.
11 Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
And I will make Jerusalem into piles of sand and into a lair for serpents. And I will make the cities of Judah desolate, so much so that there will be no inhabitant.
12 Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
Who is the wise man who understands this, and to whom a word from the mouth of the Lord may be given, so that he may announce this: why the land has perished, and has been scorched like a desert, so much so that no one passes through it?”
13 Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
And the Lord said: “It is because they have abandoned my law, which I gave to them, and they have not listened to my voice, and they have not walked by it.
14 Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
And they have gone after the depravity of their own heart, and after Baal, which they learned from their fathers.”
15 Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
For this reason, thus says the Lord of hosts, the God of Israel: “Behold, I will feed this people with absinthe, and I will give them the water of gall to drink.
16 Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
And I will disperse them among nations, which they and their fathers have not known. And I will send the sword after them, until they are consumed.”
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
Thus says the Lord of hosts, the God of Israel: “Consider and call upon the women mourners, and let them approach. And send to those women who are wise, and let them hurry.
18 Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
‘Let them hasten to take up a lamentation over us. Let our eyes shed tears, and our eyelids run with water.’
19 Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
For a voice of lamentation has been heard from Zion: ‘How is it that we have been devastated and greatly confounded? Our tabernacles have been thrown down because we have forsaken the land.’”
20 Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
“Therefore, listen, O women, to the word of the Lord! And let your ears take up the word of his mouth. And teach your daughters to lament. And let each one teach her neighbor to mourn:
21 Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
‘For death has climbed through our windows. It has entered our houses to perish the little children from the outdoors, the youths from the streets.’”
22 Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
“Speak: Thus says the Lord: And the corpses of men will fall like manure over the face of the countryside, and like hay behind the back of the reaper, and there will be no one to gather it.”
23 Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
Thus says the Lord: “The wise man should not glory in his wisdom, and the strong man should not glory in his strength, and the rich man should not glory in his riches.
24 koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
But he who glories should glory in this: to know me and to know me well. For I am the Lord, who accomplishes mercy and judgment and justice upon the earth. For these things are pleasing to me, says the Lord.
25 “Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
Behold, the days are approaching, says the Lord, when I will visit upon all who are uncircumcised:
26 Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”
upon Egypt, and upon Judah, and upon Edom, and upon the sons of Ammon, and upon Moab, and upon all who have shaved off their hair, living in the desert. For all the nations are uncircumcised in body, but all the house of Israel is uncircumcised in heart.”