< Yeremiya 9 >

1 Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
Gid mit Hoved var Vand og mit Øje en Taarekilde! da vilde jeg begræde Dag og Nat mit Folks Datters ihjelslagne.
2 Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
Gid jeg havde i Ørken et Herberg for vejfarende! da vilde jeg forlade mit Folk og gaa fra dem; thi de ere alle sammen Horkarle, en Forsamling af troløse Folk.
3 “Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
Og de spænde deres Tunge som deres Bue til Løgn, og ikke ved Troskab ere de blevne vældige i Landet; men de gaa fra det ene Onde til det andet; og mig kende de ikke, siger Herren.
4 “Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
Forvarer eder hver for sin Ven, forlader eder ikke paa nogen Broder; thi hver Broder er fuld af List, og hver Ven vandrer om som en Bagvadsker.
5 Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
Og de handle bedragelig hver imod sin Ven og tale ikke Sandhed, de have lært deres Tunge at tale Løgn, de have trættet sig med at handle forvendt.
6 Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
Du bor midt i Bedrageri; i Bedrageri vægre de sig ved at kende mig, siger Herren,
7 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
Derfor, saa siger den Herre Zebaoth: Se, jeg vil smelte dem og prøve dem; thi hvorledes skal jeg handle over for mit Folks Datter.
8 Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
Deres Tunge er en dræbende Pil, der taler Bedrageri; med sin Mund taler enhver Fred med sin Ven, men i sit Hjerte lægger han Snarer for ham.
9 Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
Skulde jeg ikke hjemsøge dem for disse Ting? siger Herren; eller skulde min Sjæl ikke hævne sig paa saadant Folk som dette?
10 Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
Jeg vil opløfte Graad og Klage paa Bjergene og Klagemaal over Græsgangene i Ørken; thi de ere forbrændte, saa ingen gaar over dem, og man ikke hører Lyd af Kvæg, baade Himmelens Fugle og Dyrene de ere bortfløjne, de ere bortgangne.
11 Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
Og jeg vil gøre Jerusalem til en Stenhob, til Dragers Bolig; og jeg vil gøre Judas Stæder til en Ørk, saa at ingen bor der.
12 Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
Hvo er den Mand, som er viis? han forstaa dette! og til hvem har Herrens Mund talt? han kundgøre det, hvorfor Landet er ødelagt, er forbrændt som en Ørk, saa at ingen gaar igennem det!
13 Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
Og Herren sagde: Fordi de forlode min Lov, som jeg lagde for deres Ansigt, og ikke hørte paa min Røst og ikke vandrede derefter,
14 Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
men vandrede efter deres Hjertes Stivhed og efter Baalerne, som deres Fædre lærte dem:
15 Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
Derfor siger den Herre Zebaoth, Israels Gud, saaledes: Se, jeg vil bespise dem, dette Folk med Malurt og give dem besk Vand at drikke.
16 Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
Og jeg vil adsprede dem iblandt de Hedninger, som hverken de eller deres Fædre kendte, og jeg vil sende Sværdet efter dem, indtil jeg faar gjort Ende paa dem.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
Saa siger den Herre Zebaoth: Lægger Mærke dertil og kalder ad Klagekvinder, at de komme, og skikker Bud efter kyndige Kvinder, at de komme;
18 Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
og de skulle skynde sig og opløfte Klagesang over os, og vore Øjne skulle rinde med Graad og vore Øjenlaage strømme med Vand.
19 Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
Thi der er hørt en Klagerøst fra Zion: Hvor ere vi dog ødelagte! vi ere saare beskæmmede; thi vi have maattet forlade Landet, og de havde omstyrtet vore Boliger.
20 Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
Thi hører, I Kvinder! Herrens Ord, og eders Øre modtage hans Munds Ord; og lærer eders Døtre Klagesang, og hver Kvinde lære sin Veninde Klagemaal.
21 Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
Thi Døden er steget ind igennem vore Vinduer, er kommen ind i vore Paladser til at udrydde de spæde Børn, at de ej findes udenfor, de unge Karle, at de ej findes paa Gaderne.
22 Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
Tal: Saa siger Herren: Menneskers døde Kroppe skulle ligge som Møg paa Marken og som et Neg efter Høstmanden, hvilket ingen sanker op.
23 Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
Saa siger Herren: Den vise rose sig ikke af sin Visdom, og den stærke rose sig ikke af sin Styrke, den rige rose sig ikke af sin Rigdom;
24 koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
men hvo som vil rose sig, rose sig af dette, at han forstaar og kender mig, at jeg er Herren, som gør Miskundhed, Ret og Retfærdighed paa Jorden; thi disse Ting behage mig, siger Herren.
25 “Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
Se, de Dage komme, siger Herren, da jeg vil hjemsøge hver omskaaren, som har Forhud:
26 Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”
Ægypten og Juda og Edom og Ammohs Børn og Moab og alle dem med rundklippet Haar, som bo i Ørken; thi alle Hedningerne have Forhud, men Israels hele Hus, de have Forhud paa Hjertet.

< Yeremiya 9 >