< Yeremiya 8 >

1 Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
Czasu onego, mówi Pan, wybiorą kości królów Judzkich, i kości książąt ich, i kości kapłanów, i kości proroków, i kości obywateli Jeruzalemskich z grobów ich;
2 Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
I rozrzucą je przed słońce, i przed miesiąc, i przed wszystko wojsko niebieskie, które miłują, i którym służą, i za którymi chodzą, i których szukają, i którym się kłaniają; nie pozbierają ich, ani pogrzebią, ale będą miasto gnoju na wierzchu ziem i.
3 Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
I obiorą raczej śmierć niżeli żywot wszystkie ostatki, które zostaną z tego rodzaju złośliwego po wszystkich miejscach, gdziebykolwiek zostali, tam, kędy ich zapędzę, mówi Pan zastępów.
4 “Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
Przetoż rzeczesz do nich: Tak mówi Pan: Także upadli, aby nie mogli powstać? także się odwrócił, aby się zaś nie mógł nawrócić?
5 Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
Przeczże się odwrócił ten lud Jeruzalemski odwróceniem wiecznem? chwytają się kłamstwa a nie chcą się nawracać.
6 Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
Pilnowałem i słuchałem: nic nie mówiąc, co jest prawego; niemasz ktoby żałował złości swej, mówiąc: Cóżem uczynił? Każdy się obrócił za biegiem swoim, jako koń, który pędem bieży ku potkaniu.
7 Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
I bocian na powietrzu zna ustawione czasy swoje, i synogarlica, i żuraw, i jaskółka przestrzegają czasu przylecenia swego; ale lud mój nie zna sądu Pańskiego.
8 “‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
Jakoż mówicie: Myśmy mądrzy, a zakon Pański jest przy nas? zaprawdę, oto daremnie pióro pisarz czyni; daremnie są w zakonie biegłymi.
9 Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
Kogoż zawstydzili ci mędrcy? Którzyż są przestraszeni i pojmani? Oto słowo Pańskie odrzucają; cóż to tedy za mądrość ich?
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Dlatego dam żony ich innym, pola ich tym, którzy ich opanują; bo od najmniejszego aż do największego, wszyscy zgoła udali się za łakomstwem; od proroka aż do kapłana wszyscy przewodzą kłamstwo.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
Bo leczą skruszenie córki ludu mego tylko po wierzchu, mówiąc: Pokój, pokój! choć niemasz pokoju.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
Izali się zawstydzili, przeto, że obrzydliwość czynili? Zaiste, ani się zapałać ani wstydzić umieli; przetoż upadną między padającymi, czasu nawiedzenia swego upadną, mówi Pan.
13 “‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
Do szczętu ich wykorzenię, mówi Pan; nie będzie żadnego grona na winnej macicy, ani żadnych fig na drzewie figowem; nawet i liść opadnie, a com im dał, odjęte będzie.
14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
Przecz my tu siedzimy? Zejdźcie się, a wynijdżmy do miast obronnych, a tam odpoczniemy; ale Pan, Bóg nasz każe nam odpocznąć, gdy nas napoi wodą żółci, iżeśmy zgrzeszyli przeciwko Panu.
15 Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
Czekaj pokoju, alić nic dobrego; czasu uzdrowienia, alić oto strach.
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
Od Dan słyszeć chrapanie koni jego, od głosu wykrzykania mocarzy jego wszystka ziemia zadrżała, którzy ciągną, aby pożarli ziemię, i wszystko, co jest na niej, miasto i tych, którzy mieszkają w niem.
17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
Bo oto Ja poślę na was węże najjadowitsze, przeciwko którym niemasz zaklinania; i pokąsają was, mówi Pan.
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
Serce moje we mnie, któreby mię miało posilać w smutku, mdłe jest.
19 Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
Oto głos krzyku córki ludu mego z ziemi bardzo dalekiej mówiącej: Izali Pana niemasz na Syonie? Izali króla jego niemasz na nim? Przeczże mię wzruszyli do gniewu bałwanami swemi, próżnościami cudzoziemców? mówi Pan.
20 “Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
Pominęło żniwo, skończyło się lato, a myśmy nie wybawieni.
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
Dla skruszenia córki ludu mojego skruszonym jest, żałobę ponoszę, zdumienie zdjęło mię.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?
Izali niemasz balsamu w Galaad? Izali tam niemasz lekarza? Czemuż tedy nie jest uleczona córka ludu mojego?

< Yeremiya 8 >