< Yeremiya 8 >

1 Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
Ngalesosikhathi, itsho iNkosi, bazakhupha amathambo amakhosi akoJuda, lamathambo eziphathamandla zayo, lamathambo abapristi, lamathambo abaprofethi, lamathambo abahlali beJerusalema, emangcwabeni abo;
2 Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
baweneke elangeni lenyangeni, lakulo lonke ibutho lamazulu, abakuthandayo, labakusebenzelayo, labakulandelayo, labakudingayo, labakukhonzayo; kawayikubuthwa, kawayikungcwatshwa; azakuba ngawomquba phezu kobuso bomhlaba.
3 Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
Njalo ukufa kuzakhethwa kulempilo yiyo yonke insali yabaseleyo balolusapho olubi, kuzo zonke indawo zabaseleyo lapho engibaxotshele khona, itsho iNkosi yamabandla.
4 “Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
Uzakuthi kibo futhi: Itsho njalo INkosi: Bazakuwa bangavuki yini? Uzaphambuka angaphenduki yini?
5 Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
Pho, baphambukelani lababantu eJerusalema ngokuphambuka okulaphakade? Babambelela enkohlisweni, bayala ukuphenduka.
6 Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
Ngilalele ngezwa, kabakhulumanga kuhle; kakulamuntu ozisolayo ngobubi bakhe esithi: Ngenzeni? Wonke uphendukela emjahweni wakhe njengebhiza ligijimela empini.
7 Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
Yebo ingabuzane emazulwini liyazazi izikhathi zalo ezimisiweyo; lejuba lehemu lenkonjane kuyagcina isikhathi sokubuya kwakho; kodwa abantu bami kabazazi izimiso zeNkosi.
8 “‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
Litsho njani ukuthi: Sihlakaniphile, lomlayo weNkosi ulathi? Khangelani, isibili usiba lwamanga lwababhali lusebenzela ize.
9 Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
Abahlakaniphileyo bayangekile, besabe kakhulu bathethwe; khangela, balalile ilizwi leNkosi; pho balenhlakanipho bani?
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Ngakho omkabo ngizabanika abanye, amasimu abo kwabazakudla ilifa labo; ngoba kusukela komncinyane kuze kufike komkhulu bonke bayizihwaba zenzuzo embi, kusukela kumprofethi kuze kube kumpristi wonke wenza ngenkohliso.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
Ngoba balipholise kancane inxeba lendodakazi yabantu bami, besithi: Ukuthula, ukuthula; khona kungelakuthula.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
Baba lenhloni yini lapho sebenze amanyala? Hatshi, kababanga lanhloni lakanye, futhi kabakwazi ukuyangeka; ngakho bazakuwa phakathi kwabawayo; ngesikhathi sokuhanjelwa kwabo bazawiselwa phansi, itsho iNkosi.
13 “‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
Isibili ngizabaqeda, itsho iNkosi; kakuyikuba khona izithelo zevini evinini; njalo kakuyikuba khona imikhiwa emkhiweni, lehlamvu lizabuna; lengibanike khona kuzakwedlula kibo.
14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
Sihlaleleni? Buthanani, singene emizini evikelweyo, sithule khona; ngoba iNkosi uNkulunkulu wethu isithulisile, yasinathisa amanzi enyongo, ngoba sonile eNkosini.
15 Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
Salindela ukuthula, kodwa kakubanga lokuhle; isikhathi sokwelatshwa, kodwa khangela, luhlupho.
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
Ukuthimula kwamabhiza akhe kwezwakala kusukela koDani; ilizwe lonke lathuthumela emsindweni wokukhonya kwalamandla akhe; ngoba afikile, adla ilizwe lokugcwala kwalo, umuzi labahlala kiwo.
17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
Ngoba khangelani, ngithumela phakathi kwenu izinyoka, amabululu, angelakulunjwa, njalo azaliluma, itsho iNkosi.
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
Ukududuzwa kwami kusosizini, inhliziyo yami iphelelwa ngamandla kimi.
19 Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
Khangelani, ilizwi lokukhala kwendodakazi yabantu bami livela elizweni elikhatshana. INkosi kayikho eZiyoni yini? Inkosi yayo kayikho phakathi kwayo yini? Bangicunuleleni ngezithombe zabo ezibaziweyo, ngokuyize kwabezizwe?
20 “Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
Isivuno sidlulile, ihlobo liphelile, kanti thina kasisindiswanga.
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
Ngokwephuka kwendodakazi yabantu bami ngephukile; ngimnyama; ukumangala okukhulu kungibambile.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?
Kakulabhalisamu yini eGileyadi? Kakho yini umelaphi khona? Ngoba kungani kungaveli ukwelatshwa kwendodakazi yabantu bami?

< Yeremiya 8 >