< Yeremiya 8 >

1 Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
En ce temps-là, dit le Seigneur, on jettera les os des rois de Juda, et les os de ses princes, et les os des prêtres, et les os des prophètes, et les os de ceux qui ont habité Jérusalem, hors de leurs sépulcres;
2 Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
Et on les exposera au soleil et à la lune, et à toute la milice du ciel, qu’ils ont aimés, qu’ils ont servis, qu’ils ont cherchés et qu’ils ont adorés; on ne les recueillera pas, et on ne les ensevelira pas; comme un fumier, ils seront sur la face de la terre.
3 Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
Et ils choisiront la mort plutôt que la vie, tous ceux qui seront restés de cette race très méchante, dans tous les lieux qui ont été abandonnés, dans lesquels je les ai jetés, dit le Seigneur des armées.
4 “Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
Et tu leur diras: Voici ce que dit le Seigneur: Est-ce que celui qui tombe ne se relèvera pas? et celui qui s’est détourné ne reviendra-t-il pas?
5 Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
Pourquoi donc ce peuple à Jérusalem s’est-il détourné par un détournement opiniâtre? Ils ont saisi le mensonge, et ils n’ont pas voulu revenir.
6 Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
J’ai prêté attention et j’ai écouté; personne ne dit ce qui est bon; il n’en est aucun qui fasse pénitence de son péché, disant: Qu’ai-je fait? tous ont suivi leur cours, comme un cheval qui s’élance avec impétuosité au combat.
7 Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
Le milan connaît dans le ciel son temps; la tourterelle, l’hirondelle et la cigogne gardent le temps de leur arrivée; mais mon peuple n’a pas connu le jugement du Seigneur.
8 “‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
Comment dites-vous: Nous sommes sages, et la loi de Dieu est avec nous? il a vraiment gravé le mensonge, le style menteur des scribes.
9 Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
Les sages ont été confondus, ils ont été épouvantés et pris; car ils ont rejeté la parole du Seigneur, et il n’est aucune sagesse en eux.
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
À cause de cela je donnerai leurs femmes à des étrangers, et leurs champs à des héritiers, parce que, depuis le plus petit jusqu’au plus grand, tous suivent l’avarice; et que depuis le prophète jusqu’au prêtre, tous commettent le mensonge.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
Et ils guérissaient la blessure de la fille de mon peuple avec ignominie, disant: Paix, paix, lorsqu’il n’y avait point de paix.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
Ils ont été confus, parce qu’ils ont fait des abominations; et encore ne l’ont-ils pas été entièrement, et n’ont-ils pas su rougir; c’est pour cela qu’ils tomberont parmi ceux qui sont renversés; qu’au temps de leur Visitation ils seront renversés tous ensemble, dit le Seigneur.
13 “‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
Les rassemblant, je les rassemblerai, dit le Seigneur; il n’y a pas de raisin aux vignes, et il n’y a pas de figue aux figuiers, les feuilles sont tombées; et ce que je leur avais donné leur a échappé.
14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
Pourquoi sommes-nous assis? venez ensemble, entrons dans la ville fortifiée, et soyons-y en silence; car le Seigneur notre Dieu nous a réduits au silence, et il nous a donné pour breuvage de l’eau de fiel; car nous avons péché contre le Seigneur.
15 Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
Nous avons attendu la paix, et nul bien n’est venu; le temps de la guérison, et voilà l’épouvante.
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
Le roulement de ses chevaux a été entendu de Dan; à la voix des hennissements de ses combattants, toute la terre a été émue; et ils sont venus, et ils ont dévoré la terre et tout ce qu’elle contient, la ville et ses habitants.
17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
Parce que voilà que moi, je vous enverrai des serpents, des basilics, contre lesquels il n’y a point d’enchantement, et ils vous mordront, dit le Seigneur.
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
Ma douleur est au-dessus d’une douleur; au-dedans de moi, mon cœur est triste.
19 Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
Voilà la voix de la fille de mon peuple qui me crie d’une terre lointaine: Est-ce que le Seigneur n’est pas dans Sion, ou son roi n’est-il pas en elle? Pourquoi donc m’ont ils excité au courroux par leurs images taillées au ciseau, et par des vanités étrangères?
20 “Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
La moisson est passée, l’été est fini, et nous, nous n’avons pas été sauvés.
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
Je suis brisé à cause du brisement de la fille de mon peuple, et contristé; la stupeur m’a saisi.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?
Est-ce qu’il n’y a point de résine en Galaad? ou n’y a-t-il pas là de médecin? pourquoi donc n’a-t-elle pas été fermée, la blessure de la fille de mon peuple?

< Yeremiya 8 >