< Yeremiya 8 >

1 Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
En ce temps-là, dit l'Éternel, on jettera les os des rois de Juda, et les os de ses princes, les os des sacrificateurs, les os des prophètes et les os des habitants de Jérusalem, hors de leurs sépultures;
2 Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
On les étendra devant le soleil, et devant la lune, et devant toute l'armée des cieux qu'ils ont aimés, qu'ils ont servis et après lesquels ils ont marché, qu'ils ont recherchés et devant lesquels ils se sont prosternés. Ils ne seront point recueillis, ni ensevelis; ils seront comme du fumier sur la face du sol.
3 Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
Et la mort sera plus désirable que la vie pour tous ceux qui seront restés de cette race mauvaise, dans tous les lieux où j'en aurai chassé les restes, dit l'Éternel des armées.
4 “Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
Tu leur diras donc: Ainsi a dit l'Éternel: Si l'on tombe, ne se relève-t-on pas? et si l'on se détourne, ne revient-on pas?
5 Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
Pourquoi donc ce peuple de Jérusalem, s'est-il égaré d'un égarement continuel? Ils persistent dans la tromperie; ils refusent de se convertir.
6 Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
J'ai prêté l'oreille, j'ai écouté: ils ne parlent pas droitement. Nul ne se repent de sa méchanceté, et ne dit: Qu'ai-je fait? Tous ils retournent à leur course, comme le cheval qui se précipite au combat.
7 Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
La cigogne même connaît dans les cieux ses saisons; la tourterelle, l'hirondelle et la grue observent le temps où elles doivent venir; mais mon peuple ne connaît pas le jugement de l'Éternel.
8 “‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
Comment dites-vous: Nous sommes sages, et la loi de l'Éternel est avec nous? Mais voici, la plume menteuse des scribes en fait un mensonge!
9 Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
Les sages seront confus; ils seront épouvantés, et ils seront pris. Car ils ont rejeté la parole de l'Éternel, et quelle sagesse auraient-ils?
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
C'est pourquoi je donnerai leurs femmes à d'autres, et leurs champs à de nouveaux possesseurs. Car, depuis le plus petit jusqu'au plus grand, tous sont avides de gain. Depuis le prophète jusqu'au sacrificateur, tous se conduisent faussement.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
Ils pansent à la légère la plaie de la fille de mon peuple, en disant: Paix, paix! et il n'y a point de paix.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
Ont-ils été confus de ce qu'ils ont commis l'abomination? Ils n'en ont même eu aucune honte, et ils ne savent ce que c'est de rougir. C'est pourquoi ils tomberont avec ceux qui tombent; au temps de leur visitation ils seront renversés, dit l'Éternel.
13 “‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
Je les enlèverai entièrement, dit l'Éternel. Il n'y a point de grappes à la vigne; il n'y a point de figues au figuier; la feuille est flétrie; ce que je leur ai donné sera enlevé!
14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
Pourquoi demeurons-nous assis? Assemblez-vous, et entrons dans les villes fortes, et nous y périrons! Car l'Éternel notre Dieu a résolu notre perte; il nous fait boire des eaux empoisonnées; parce que nous avons péché contre l'Éternel.
15 Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
On attendait la paix, mais il n'y a rien de bon; un temps de guérison, et voici la terreur!
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
Du côté de Dan se fait entendre le ronflement de leurs chevaux; au bruit du hennissement de leurs puissants coursiers, toute la terre tremble. Ils viennent; ils dévorent le pays et ce qu'il contient, la ville et ceux qui y habitent.
17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
Car voici, j'envoie contre vous des serpents, des basilics, contre lesquels il n'y a point de charme; ils vous mordront, dit l'Éternel.
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
Ah! du répit pour ma douleur! Mon cœur souffre au-dedans de moi!
19 Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
Voici la voix de la fille de mon peuple, qui crie d'un pays éloigné: L'Éternel n'est-il plus dans Sion? Son roi n'est-il plus au milieu d'elle? Pourquoi m'ont-ils irrité par leurs images taillées, par les vanités de l'étranger?
20 “Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
La moisson est passée, l'été a pris fin, et nous ne sommes pas délivrés!
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
Je suis blessé de la blessure de la fille de mon peuple; j'en suis en deuil, la désolation m'en a saisi.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?
N'y a-t-il point de baume en Galaad? N'y a-t-il point de médecin? Pourquoi donc la plaie de la fille de mon peuple n'est-elle pas consolidée?

< Yeremiya 8 >