< Yeremiya 8 >

1 Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
“At that time—this is Yahweh's declaration—they will bring out from the graves the bones of the kings of Judah and its officials, the bones of the priests and the prophets, and the bones of the inhabitants of Jerusalem.
2 Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
Then they will spread them out in the light of the sun and moon and all the stars of the skies; these things in the sky that they have followed and served, that they have walked after and sought, and that they have worshiped. The bones will not be gathered or buried again. They will be like dung on the surface of the earth.
3 Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
In every remaining place where I have driven them, they will choose death instead of life for themselves, all who are still left over from this evil nation—this is the declaration of Yahweh of hosts.
4 “Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
So say to them, 'Yahweh says this: Does anyone fall and not get up? Does anyone get lost and not try to return?
5 Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
Why has this people, Jerusalem, turned away in permanent faithlessness? They hold on to treachery and refuse to repent.
6 Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
I paid attention and listened, but they did not speak right; no one was sorry for his wickedness, no one who says, “What have I done?” All of them go where they wish, like a stallion rushing toward battle.
7 Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
Even the stork in heaven knows the right times; and the doves, swifts, and cranes. They go on their migrations at the right time, but my people do not know Yahweh's decrees.
8 “‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
How can you say, “We are wise, for the law of Yahweh is with us”? Indeed, see! The deceitful pen of the scribes has created deceit.
9 Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
The wise men will be ashamed. They are dismayed and trapped. Behold! They reject Yahweh's word, so what use is their wisdom?
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
So I will give their wives to others, and their fields to those who will possess them, because from the least to the greatest, all of them are greedy for dishonest gain! From the prophet to the priest, all of them practice deceit.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
They healed the wounds of my people lightly, saying, “Peace, Peace,” when there was no peace.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
Were they ashamed when they practiced abominations? They were not ashamed; they did not know how to blush! So they will fall among the fallen; they will be brought down when they are punished, says Yahweh.
13 “‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
I will remove them completely—this is Yahweh's declaration—there will be no grapes on the vine, nor will there be figs on the fig trees. For the leaf will wither, and what I have given to them will pass away.
14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
Why are we sitting here? Come together; let us go to the fortified cities, and we will become silent there in death. For Yahweh our God will silence us. He will make us drink poison, since we have sinned against him.
15 Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
We are hoping for peace, but there will be nothing good. We are hoping for a time of healing, but see, there will be terror.
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
The snorting of his stallions is heard from Dan. The whole earth shakes at the sound of the neighing of his strong horses. For they will come and consume the land and its wealth, the city and the ones living in it.
17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
For see, I am sending out snakes among you, vipers that you cannot charm. They will bite you—this is Yahweh's declaration.'”
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
My sorrow has no end, and my heart is sick.
19 Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
Behold! The screaming voice of the daughter of my people from a land far away! Is Yahweh not in Zion? Is her king no longer there? Why then do they provoke me to anger with their carved figures and their worthless foreign idols?
20 “Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
The harvest has passed on, summer is over. But we have not been saved.
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
I am hurt because of the hurt of the daughter of my people. I mourn at the horrible things that have happened to her; I am dismayed.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?
Is there no medicine in Gilead? Is there no healer there? Why will the healing of the daughter of my people not happen?

< Yeremiya 8 >