< Yeremiya 8 >

1 Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
В онова време, каза Господ, ще извадят от гробовете им Костите на Юдовите царе и костите на техните първенци, Костите на свещениците и костите на пророците, И костите на ерусалимские жители;
2 Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
И ще ги пръснат пред слънцето и луната И пред всичкото небесно войнство, които те обичаха, На които служиха и които последваха, Които потърсиха и на които се поклониха; Тия кости не ще бъдат събрани нито погребани, Но ще служат за тор по лицето на земята.
3 Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
И смъртта ще бъде по-желателна от живота За всичките останали, оцелели от тоя лош род, Които би останали във всичките места, гдето бих ги изгонил, Казва Господ на Силите.
4 “Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
При това рече им: Така казва Господ: Който падне, няма ли да стане? Който се отбие, няма ли да се върне?
5 Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
Защо, прочее, се отбиха тия Ерусалимски люде С неизменимо отбиване, Като се прилепват за измамата И не искат да се върнат?
6 Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
Слушах и чух, но те не говориха право; Няма кой да се кае поради злото си И да рече: Какво сторих! Всеки се връща в своето поприще Както кон, който стремително тича в боя.
7 Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
Даже щъркелът по небето знае определените си времена, И гургулицата, и лястовицата, и жеравът Пазят времето на дохождането си; А Моите люде не знаят закона Господен.
8 “‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
Как казвате: Ние сме мъдри, И законът Господен е с нас? Ето, наистина и него Лъжливото перо на книжниците е обърнало в лъжа.
9 Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
Мъдрите се посрамиха, Уплашиха се, и хванати бидоха; Ето, отхвърлиха словото Господно; И каква мъдрост има в тях?
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Затова, ще дам жените им на други, И нивите им на ония, които ще ги завладеят; Защото всеки от малък до голям, Се е предал на сребролюбие; От пророк до свещеник Всеки постъпва лъжливо.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
И повърхностно лекуваха раната на дъщерята на людете Ми, Като казваха - Мир, мир!, а пък няма мир.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
Засрамиха ли се, когато извършиха мерзости? Не, никак не ги досрамя, Нито са знаели да почервенеят; Затова, ще падат между падащите, Ще бъдат поваляни, когато ги накажа казва Господ
13 “‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
Съвършено ще ги изтребя, казва Господ; Не ще има гроздове на лозата Нито смокини на смоковницата, И листът ще повехне, И даже това, което им съм дал, ще избяга от тях.
14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
Защо още седим? Съберете се, нека влезем в укрепените градове, И нека загинем там; Защото Господ нашият Бог не ни е предал на погибел, И напоил ни е с горчива вода, Понеже съгрешихме на Господа.
15 Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
Очаквахме мир, но никакво добро не дойде, - Време на изцеление, но, ето, смущение.
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
Пръхането на конете му се чу от Дан; Цялата страна се потресе от гласа на цвиленията на яките му коне; Защото дойдоха та изпоядоха страната и всичко, що има по нея, Града и ония, които живеят в него.
17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
Защото, ето, Аз пращам върху вас змии, ехидни, Които не се омайват, Но ще ви хапят, казва Господ.
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
Дано бих намерил утешение за скръбта си! Сърцето ми е от дън изнемощяло.
19 Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
Ето, гласът на дъщерята на людете Ми, Която вика от далечна земя, като казва: Господ не е ли в Сион? Царят му не е ли в него? Защо Ме разгневиха с изваяните си идоли, С чужди суети?
20 “Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
Премина жетвата, мина се лятото, И ние не се избавихме.
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
Съкрушен съм поради съкрушението на дъщерята на людете Ми; Помрачен съм; ужас ме обзе.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?
Няма ли балсама в Галаад? Няма ли там лекар? Защо, прочее, изцеляването на дъщерята на людете Ми не се усъвършенствува?

< Yeremiya 8 >