< Yeremiya 7 >
1 Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
Leli yilizwi elafika kuJeremiya livela kuThixo lisithi:
2 “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
“Mana esangweni lendlu kaThixo umemezele ilizwi leli ukhonapho uthi: ‘Zwanini ilizwi likaThixo, lonke lina bantu bakoJuda abangena ngala amasango ukuzakhonza uThixo.
3 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
UThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi: Lungisani izindlela zenu lezenzo zenu, ukuze ngilivumele ukuba lihlale kule indawo.
4 Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
Lingathembi amazwi akhohlisayo lithi, “Leli lithempeli likaThixo, ithempeli likaThixo, ithempeli likaThixo!”
5 Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
Lingalungisa izindlela zenu lezenzo zenu sibili liphathane ngokulunga,
6 ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
nxa lingancindezeli owezizweni, izintandane loba umfelokazi njalo lingachithi gazi elingelacala kule indawo, njalo nxa lingalandeli abanye onkulunkulu okuzalilimaza,
7 Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
ngizalivumela ukuba lihlale kule indawo, elizweni engalinika okhokho benu ukuba libe ngelabo kuze kube nini lanini.
8 Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
Kodwa khangelani, lina lithemba amazwi akhohlisayo angasizi lutho.
9 “Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
Kambe lizantshontsha njalo libulale, lifebe, lifunge amanga, litshisele uBhali impepha njalo lilandele abanye onkulunkulu elingakaze libazi,
10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
beselisizakuma phambi kwami kuyonale indlu, eleBizo lami, lithi, “Sivikelekile,” livikeleka ukuba lenze zonke lezizinto ezenyanyekayo na?
11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
Indlu le, eleBizo lami, seyaba lubhalu lwabaphangi na? Kodwa kade ngikhangele! kutsho uThixo.
12 “‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
Hambani khathesi endaweni yami eShilo lapho engenza khona kuqala indawo yokuhlala iBizo lami, libone engakwenza kuyo ngenxa yobubi babantu bami bako-Israyeli.
13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
UThixo uthi, kwathi lapho lisenza lezizinto, mina ngakhuluma lani futhifuthi, kodwa kalingilalelanga, ngalibiza, kalaze lasabela.
14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
Ngakho-ke, lokho engakwenza eShilo khathesi ngizakwenza kule indlu eleBizo lami, ithempeli elilithembileyo, indawo engalinika yona lina kanye labokhokho benu.
15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
Ngizalixotsha phambi kwami, njengalokho engakwenza abafowenu bonke, abantu bako-Efrayimi.’
16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
Ngakho abantu laba ungabakhulekeli loba ubakhulumele kumbe ubenzele isicelo; ungangincengi ngoba angiyikukulalela.
17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
Abakwenzayo emadolobheni akoJuda lasemigwaqweni yaseJerusalema kawukuboni na?
18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
Abantwana batheza inkuni, oyise babasa imililo, labesifazane baxova inhlama benzele iNdlovukazi yaseZulwini isinkwa. Bathelela abanye onkulunkulu iminikelo yokunathwayo ukuba bangithukuthelise.
19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
Kodwa yimi abangithukuthelisayo na? kutsho uThixo. Kabazilimazi bona ngokwabo na, okulihlazo kubo?
20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
‘Ngakho uThixo Wobukhosi uthi: Ukuthukuthela kwami lolaka lwami kuzakwehliselwa kule indawo, phezu kwabantu lasezinyamazaneni, phezu kwezihlahla zeganga laphezu kwezithelo zomhlabathi; njalo kuzakutsha kungacitsheki.
21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
UThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi: Qhubekani, fakani iminikelo yenu yokutshiswa kweminye imihlatshelo yenu lidle inyama lina ngokwenu!
22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
Ngoba ekukhupheni kwami okhokho benu eGibhithe ngikhuluma labo, angizange ngibanike imilayo nje kuphela ngeminikelo yokutshiswa lemihlatshelo,
23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
kodwa ngabanika umlayo lo othi: Ngilalelani, njalo ngizakuba nguNkulunkulu wenu lina libe ngabantu bami. Hambani ngezindlela zonke engililaye zona, ukuze kulilungele.
24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
Kodwa kabazange balalele kumbe banake; esikhundleni salokho, bona balandela inkani yentando yezinhliziyo zabo ezimbi. Baya emuva hatshi phambili.
25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
Kusukela ngesikhathi okhokho benu besuka eGibhithe kuze kube khathesi, usuku ngosuku, njalonjalo ngalithumela izinceku zami abaphrofethi.
26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
Kodwa kabangilalelanga kumbe banake. Babelentamo ezilukhuni njalo benza ububi obudlula obabokhokho babo.’
27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
Lapho ubatshela konke lokhu, kabayikukulalela; lalapho ubabiza, kabayikusabela.
28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
Ngakho batshele uthi, ‘Lesi yisizwe esingalalelanga uThixo uNkulunkulu waso kumbe sivume ukuqondiswa. Iqiniso selifile; kalisekho ezindebeni zabo.
29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
Gelani inwele zenu lizilahlele khatshana; lenze isililo emiqolweni elugwadule, ngoba uThixo usesalile wasidela isizukulwane lesi esingaphanasi kolaka lwakhe.’”
30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
“‘Abantu bakoJuda benze ububi phambi kwami, kutsho uThixo. Bamise izithombe zabo ezenyanyekayo endlini eleBizo lami balingcolisa.
31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
Sebakhe izindawo eziphakemeyo zaseThofethi esigodini saseBheni-Hinomu ukuba batshisele khona amadodana lamadodakazi abo ngomlilo, into engingabalayanga yona, engazange ifike engqondweni yami.
32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
Ngakho qaphelani, insuku ziyeza, kutsho uThixo, lapho abantu bengayikuyithi yiThofethi kumbe iSigodi saseBheni-Hinomu, kodwa iSigodi sokuBulala, ngoba abafileyo bazabangcwaba eThofethi kuze kusweleke indawo.
33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
Lapho-ke izidumbu zabantu laba zizakuba yikudla kwezinyoni zasemoyeni lezinyamazana zomhlaba, njalo akuyikuba lomuntu ozazethusa.
34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”
Ngizaqeda imisindo yokuthokoza leyenjabulo emadolobheni akoJuda lasemigwaqweni yaseJerusalema, lokuthaba lelizwi lomlobokazi lelomyeni, ngoba ilizwe lizachitheka.’”