< Yeremiya 7 >

1 Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
La parole qui fut adressée à Jérémie de la part de Yahvé, en ces termes:
2 “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
« Tenez-vous à la porte de la maison de Yahvé, et proclamez-y cette parole, en disant: « Écoutez la parole de Yahvé, vous tous de Juda, qui entrez par ces portes pour vous prosterner devant Yahvé! ».
3 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
L'Éternel des armées, le Dieu d'Israël, dit: « Modifiez vos voies et vos actions, et je vous ferai habiter dans ce lieu.
4 Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
Ne vous fiez pas à des paroles mensongères, disant: « Le temple de l'Éternel, le temple de l'Éternel, le temple de l'Éternel, c'est cela ».
5 Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
Car si vous corrigez vos voies et vos actions, si vous pratiquez la justice entre un homme et son prochain,
6 ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
si vous n'opprimez pas l'étranger, l'orphelin et la veuve, si vous ne répandez pas le sang innocent dans ce lieu, et si vous ne marchez pas après d'autres dieux pour votre propre malheur,
7 Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
alors je vous ferai habiter dans ce lieu, dans le pays que j'ai donné à vos pères, dès les temps anciens et à jamais.
8 Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
Voici, vous vous confiez à des paroles mensongères qui ne profitent pas.
9 “Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
Voulez-vous voler, assassiner, commettre l'adultère, jurer faussement, offrir de l'encens à Baal, marcher après d'autres dieux que vous n'avez pas connus,
10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
puis venir vous présenter devant moi dans cette maison qui porte mon nom, et dire: « Nous sommes délivrés », afin de commettre toutes ces abominations?
11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
Cette maison, qui porte mon nom, est-elle devenue à vos yeux une caverne de voleurs? Voici, je l'ai vu moi-même, dit Yahvé.
12 “‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
« Va maintenant dans le lieu qui était à Silo, où j'ai d'abord fait résider mon nom, et regarde ce que j'y ai fait à cause de la méchanceté de mon peuple d'Israël.
13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
Maintenant, puisque tu as fait toutes ces choses, dit l'Éternel, et que je t'ai parlé, que je me suis levé de bonne heure et que j'ai parlé, mais que tu n'as pas écouté, que je t'ai appelé, mais que tu n'as pas répondu,
14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
je ferai à la maison qui porte mon nom, dans laquelle tu te confies, et au lieu que j'ai donné à toi et à tes pères, ce que j'ai fait à Silo.
15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
Je te chasserai de ma vue, comme j'ai chassé tous tes frères, toute la race d'Éphraïm.
16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
« Ne priez donc pas pour ce peuple. N'élève pas pour eux un cri ou une prière, et n'intercède pas auprès de moi, car je ne t'écouterai pas.
17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
Ne voyez-vous pas ce qu'ils font dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem?
18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
Les enfants ramassent du bois, les pères allument le feu, et les femmes pétrissent la pâte, pour préparer des gâteaux à la reine du ciel, et pour verser des libations à d'autres dieux, afin de m'irriter.
19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
Me provoquent-ils à la colère? dit l'Éternel. « Ne s'irritent-ils pas eux-mêmes, jusqu'à la confusion de leur propre visage? »
20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
C'est pourquoi le Seigneur Yahvé dit: « Voici que ma colère et ma fureur vont se répandre sur ce lieu, sur l'homme, sur l'animal, sur les arbres des champs et sur les fruits du sol; elles brûleront et ne s'éteindront pas. »
21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
Yahvé des Armées, le Dieu d'Israël, dit: « Ajoutez vos holocaustes à vos sacrifices et mangez de la viande.
22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
Car, le jour où je les ai fait sortir du pays d'Égypte, je n'ai pas parlé à vos pères ni ne leur ai donné d'ordre concernant les holocaustes ou les sacrifices.
23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
Mais je leur ai donné cet ordre: « Écoutez ma voix, et je serai votre Dieu, et vous serez mon peuple.
24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
Mais ils n'ont pas écouté, ils n'ont pas prêté l'oreille, ils ont suivi leurs propres conseils et l'obstination de leur mauvais cœur, et ils ont marché en arrière et non en avant.
25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
Depuis le jour où vos pères sont sortis du pays d'Égypte jusqu'à ce jour, je vous ai envoyé tous mes serviteurs les prophètes, me levant chaque jour de bonne heure et les envoyant.
26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
Mais ils ne m'ont pas écouté, ils n'ont pas prêté l'oreille, ils ont raidi leur cou. Ils ont fait pire que leurs pères.
27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
« Tu leur diras toutes ces paroles, mais ils ne t'écouteront pas. Tu les appelleras aussi, mais ils ne te répondront pas.
28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
Tu leur diras: « C'est une nation qui n'a pas écouté la voix de Yahvé, son Dieu, et qui n'a pas reçu d'instruction. La vérité a disparu, elle a été retranchée de leur bouche ».
29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
Coupe tes cheveux, jette-les au loin, et fais des lamentations sur les hauteurs, car l'Éternel a rejeté et abandonné la génération de sa colère.
30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
« Car les enfants de Juda ont fait ce qui est mal à mes yeux, dit Yahvé. « Ils ont placé leurs abominations dans la maison qui porte mon nom, pour la souiller.
31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
Ils ont bâti les hauts lieux de Topheth, qui est dans la vallée du fils de Hinnom, pour brûler au feu leurs fils et leurs filles, ce que je n'ai pas ordonné et ce qui ne m'est pas venu à l'esprit.
32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
C'est pourquoi voici, les jours viennent, dit Yahvé, où l'on ne l'appellera plus Topheth ou vallée du fils de Hinnom, mais vallée du carnage, car on enterrera à Topheth jusqu'à ce qu'il n'y ait plus de place pour enterrer.
33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
Les cadavres de ce peuple serviront de nourriture aux oiseaux du ciel et aux animaux de la terre. Personne ne les fera fuir.
34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”
Alors je ferai cesser, dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem, la voix de la joie et la voix de l'allégresse, la voix du fiancé et la voix de la fiancée, car le pays sera dévasté. »

< Yeremiya 7 >