< Yeremiya 7 >

1 Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
The word which it came to Jeremiah from with Yahweh saying.
2 “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
Stand in [the] gate of [the] house of Yahweh and you will proclaim there the word this and you will say hear [the] word of Yahweh O all Judah who come in the gates these to bow down to Yahweh.
3 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
Thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel make good ways your and deeds your so let me cause to dwell you in the place this.
4 Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
May not you trust for yourselves to words of deception saying [the] temple of Yahweh [the] temple of Yahweh [are] [the] temple of Yahweh they.
5 Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
That except certainly you will make good ways your and deeds your certainly [if] you will do justice between everyone and between neighbor his.
6 ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
[the] sojourner [the] fatherless And [the] widow not you must oppress and blood innocent may not you shed in the place this and after gods other not you must walk for harm of you.
7 Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
And I will cause to dwell you in the place this in the land which I gave to ancestors your from antiquity and until perpetuity.
8 Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
Here! you [are] relying for yourselves on words of deception to not to profit.
9 “Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
¿ Will you steal - will you murder? and will you commit adultery? and will you swear? to falsehood and will you make smoke? to Baal and will you walk? after gods other which not you have known.
10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
And you will come and you will stand before me in the house this which it is called name my on it and you will say we are delivered so as to do all the abominations these.
11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
¿ A den of robbers has it become the house this which it is called name my on it in view your also I here! I have seen [the] utterance of Yahweh.
12 “‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
That go please to place my which [was] in Shiloh where I caused to dwell name my there at the former [time] and see [that] which I did to it because of [the] wickedness of people my Israel.
13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
And therefore because did you all the deeds these [the] utterance of Yahweh and I spoke to you rising early and speaking and not you listened and I called you and not you answered.
14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
And I will do to the house - which it is called name my on it which you [are] trusting in it and to the place which I gave to you and to ancestors your just as I did to Shiloh.
15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
And I will cast out you from on face my just as I cast out all relatives your all [the] offspring of Ephraim.
16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
And you may not you pray - for the people this and may not you lift up for them a cry of entreaty and a prayer and may not you entreat me for not I [will be] hearing you.
17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
¿ [are] not You seeing what? [are] they doing in [the] cities of Judah and in [the] streets of Jerusalem.
18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
The children [are] gathering wood and the fathers [are] kindling the fire and the women [are] kneading dough to make cakes for [the] queen of the heavens and they are pouring out drink offerings to gods other so as to provoke to anger me.
19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
¿ Me [are] they provoking [the] utterance of Yahweh ¿ not themselves for [the] sake of [the] shame of faces their.
20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
Therefore thus he says - [the] Lord Yahweh here! anger my and rage my [are] about to be poured out against the place this on humankind and on the animal[s] and on [the] tree[s] of the field and on [the] fruit of the ground and it will burn and not it will be quenched.
21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
Thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel burnt offerings your add to sacrifices your and eat meat.
22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
For not I spoke with ancestors your and not I commanded them on [the] day (brought out I *Q(K)*) them from [the] land of Egypt on matters of burnt offering and sacrifice.
23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
That except the matter this I commanded them saying listen to voice my and I will become for you God and you you will become for me a people and you will walk in every way which I will command you so that it may go well for you.
24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
And not they listened and not they inclined ear their and they walked in counsels in [the] stubbornness of heart their evil and they were backwards and not forwards.
25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
From the day when they came out ancestors your from [the] land of Egypt until the day this and I sent to you all servants my the prophets day rising early and sending.
26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
And not they listened to me and not they inclined ear their and they stiffened neck their they did evil more than ancestors their.
27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
And you will say to them all the words these and not they will listen to you and you will call to them and not they will answer you.
28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
And you will say to them this [is] the nation which not they listened to [the] voice of Yahweh God its and not they accepted correction it has perished faithfulness and it has been cut off from mouth their.
29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
Cut off hair your and throw [it] away and take up on bare heights a lamentation for he has rejected Yahweh and he has abandoned [the] generation of fury his.
30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
For they have done [the] people of Judah the evil in view my [the] utterance of Yahweh they have put detestable things their in the house which it is called name my on it to make unclean it.
31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
And they have built [the] high places of Topheth which [is] in [the] valley of Ben Hinnom to burn sons their and daughters their in the fire which not I commanded and not it came up on heart my.
32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
Therefore here! days [are] coming [the] utterance of Yahweh and not it will be said again Topheth and [the] valley of Ben Hinnom that except [the] valley of slaughter and people will bury in Topheth from not room.
33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
And it will become [the] corpse[s] of the people this food for [the] bird[s] of the heavens and for [the] animal[s] of the earth and there not [will be one who] terrifies.
34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”
And I will cause to cease - from [the] cities of Judah and from [the] streets of Jerusalem [the] sound of joy and [the] sound of gladness [the] sound of a bridegroom and [the] sound of a bride for a desolation it will become the land.

< Yeremiya 7 >