< Yeremiya 7 >
1 Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
The word that came to Jeremias from the Lord, saying:
2 “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
Stand in the gate of the house of the Lord, and proclaim there this word, and say: Hear ye the word of the Lord, all ye men of Juda, that enter in at these gates, to adore the Lord.
3 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
Thus saith the Lord of hosts the God of Israel: Make your ways and your doings good: and I will dwell with you in this place.
4 Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
Trust not in lying words, saying: The temple of the Lord, the temple of the Lord, it is the temple of the Lord.
5 Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
For if you will order well your ways, and your doings: if you will execute judgement between a man and his neighbor,
6 ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
If you opress not the stranger, the fatherless, and the widow, and shed not innocent blood in this place, and walk not after strange gods to your own hurt,
7 Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
I will dwell with you in this place: in the land, which I gave to your fathers from the beginning and for evermore.
8 Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
Behold you put your trust in lying words, which shall not profit you:
9 “Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
To steal, to murder, to commit adultery, to swear falsely, to offer to Baalim, and to go after strange gods, which you know not.
10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
And you have come, and stood before me in this house, in which my name is called upon, and have said: We are delivered, because we have done all these abominations.
11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
Is this house then, in which my name hath been called upon, in your eyes become a den of robbers? I, I am he: I have seen it, saith the Lord.
12 “‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
Go ye to my place in Silo, where my name dwelt from the beginning: and see what I did to it for the wickedness of my people Israel:
13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
And now, because you have done all these works, saith the Lord: and I have spoken to you rising up early, and speaking, and you have not heard: and I have called you, and you have not answered:
14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
I will do to this house, in which my name is called upon, and in which you trust, and to the places which I have given you and your fathers, as I did to Silo.
15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
And I will cast you away from before my face, as I have cast away all your brethren, the whole seed of Ephraim.
16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
Therefore, do not thou pray for this people, nor take to thee praise and supplication for them: and do not withstand me: for I will not hear thee.
17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
Seest thou not what they do in the cities of Juda, and in the streets of Jerusalem?
18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
The children gather wood, and the fathers kindle the fire and the women knead the dough, to make cakes to the queen of heaven, and to offer libations to strange gods, and to provoke me to anger.
19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
Do they provoke me to anger, saith the Lord? Is it not themselves, to the confusion of their contenance?
20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
Therefore thus saith the Lord God: Behold my wrath and my indignation was enkindled against this place, upon men and upon beasts, and upon the trees of the field, and upon the fruits of the land, and it shall burn, and shall not be quenched.
21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
Thus saith the Lord of hosts the God of Israel: Add your burnt offerings to your sacrifices, and eat ye the flesh.
22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
For I spoke not to your fathers, and I commanded them not, in the day that I brought them out of the land of Egypt, concerning the matter of burnt offerings and sacrifices.
23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
But this thing I commanded them, saying: Hearken to my voice, and I will be your God, and you shall be my people: and walk ye in all the way that I have commanded you, that it may be well with you.
24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
But they hearkened not, nor inclined their ear: but walked in their own will, and in the perversity of their wicked heart: and went backward and not forward,
25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
From the day that their fathers came out of the land of Egypt, even to this day. And I have sent to you all my servants the prophets from day to day, rising up early and sending.
26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
And they have not hearkened to me: nor inclined their ear: but have hardened their neck, and have done worse than their fathers.
27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
And thou shalt speak to them all these words, but they will not hearken to thee: and thou shalt call them, but they will not answer thee.
28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
And thou shalt say to them: This is a nation which hath not hearkened to the voice of the Lord their God, nor received instruction: Faith is lost, and is carried away out of their mouth.
29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
Cut off thy hair, and cast it away: and take up a lamentation on high: for the Lord hath rejected and forsaken the generation of his wrath,
30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
Because the children of Juda have done evil in my eyes, saith the Lord. They have set their abominations in the house in which my name is called upon, to pollute it;
31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
And they have built the high places of Topeth, which is in the valley of the son of Ennom, to burn their sons, and their daughters in the fire: which I commanded not, nor thought on in my heart.
32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
Therefore behold the days shall come, saith the Lord, and it shall no more be called Topeth, nor the valley of the son of Ennom: but the valley of slaughter, and they shall bury in Topeth, because there is no place.
33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
And the carcasses of this people shall be meat for the fowls of the air, and for the beasts of the earth, and there shall be non to drive them away.
34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”
And I will cause to cease out of the cities of Juda, and out of the streets of Jerusalem, the voice of joy, and the voice of gladness, the voice of the bridegroom and the voice of the bride: for the land shall be desolate.