< Yeremiya 7 >

1 Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
Det Ord, som kom fra Herren til Jeremias, der han sagde:
2 “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
Stil dig i Herrens Hus's Port, og du skal udraabe der dette Ord og sige: Hører Herrens Ord, alle I af Juda! I, som gaa ind ad disse Porte, for at tilbede Herren!
3 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
Saa siger den Herre Zebaoth, Israels Gud: Bedrer eders Veje og eders Idrætter, saa vil jeg lade eder bo paa dette Sted.
4 Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
Forlader eder ikke paa løgnagtige Ord, naar de sige: Herrens Tempel, Herrens Tempel, Herrens Tempel er her!
5 Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
Men dersom I alvorligt bedre eders Veje og eders Idrætter, og dersom I gøre Ret imellem Mand og hans Næste,
6 ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
og I ej gøre den fremmede, den faderløse og Enken Vold og ej udøse uskyldigt Blod paa dette Sted og ej vandre efter andre Guder, eder til Ulykke:
7 Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
Da vil jeg lade eder bo paa dette Sted, i Landet, som jeg gav eders Fædre, altid og evindelig.
8 Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
Se, I forlade eder paa løgnagtige Ord, som intet gavne.
9 “Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
Skulde I stjæle, slaa ihjel og bedrive Hor og sværge falskelig og gøre Røgelse for Baal og vandre efter fremmede Guder, som I ikke kende,
10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
og saa komme og staa for mit Ansigt i dette Hus, som er kaldet efter mit Navn, og sige: Vi ere frelste for at kunne gøre alle disse Vederstyggeligheder?
11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
Mon dette Hus, som er kaldet efter mit Navn, i eders Øjne er blevet en Røverhule? ja, jeg, se, jeg har set det, siger Herren.
12 “‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
Thi gaar dog til mit Sted, som var i Silo, hvor jeg lod mit Navn bo i Begyndelsen, og ser, hvad jeg har gjort ved det for mit Folk Israels Ondskabs Skyld.
13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
Og nu, fordi I gøre alle disse Gerninger, siger Herren, og jeg talte til eder tidligt og ideligt, og I hørte ikke, og jeg kaldte ad eder, og I svarede ikke:
14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
Saa vil jeg gøre ved dette Hus, som er kaldet efter mit Navn, og paa hvilket I forlade eder, og ved det Sted, som jeg gav eder og eders Fædre, ligesom jeg har gjort ved Silo.
15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
Og jeg vil bortkaste eder fra mit Ansigt, ligesom jeg bortkastede alle eders Brødre, Efraims hele Sæd.
16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
Og du, du maa ikke bede for dette Folk og ikke opløfte Skrig eller Bøn for dem og ikke trænge ind paa mig med Forbøn; thi jeg hører dig ikke.
17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
Ser du ikke, hvad de gøre i Judas Stæder og paa Jerusalems Gader?
18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
Børnene sanke Træ og Fædrene tænde Ilden, og Kvinderne ælte Dejg for at lave Kager til Himmelens Dronning, og de udøse Drikoffer for andre Guder for at gøre mig Fortræd.
19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
Monne de gøre mig Fortræd dermed? siger Herren; monne de ikke gøre sig selv Fortræd, til deres Ansigters Bluelse?
20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
Derfor siger den Herre, Herre saaledes: Se, min Vrede og min Harme er udøst over dette Sted, over Mennesker og over Dyr og over Træer paa Marken og over Landets Frugt; og den skal brænde og ikke udslukkes.
21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
Saa siger den Herre Zebaoth, Israels Gud: Lægger eders Brændofre til eders Slagtofre, og æder Kødet!
22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
Thi jeg har ikke talt med eders Fædre, ej heller befalet dem paa den Dag, jeg udførte dem af Ægyptens Land, angaaende Brændoffer og Slagtoffer.
23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
Men denne Ting har jeg befalet dem og sagt: Hører paa min Røst, saa vil jeg være eders Gud, og I skulle være mit Folk; og I skulle vandre paa hver en Vej, som jeg befaler eder, at det maa gaa eder vel.
24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
Men de hørte ikke og bøjede ikke deres Øre, men de vandrede i deres Raad, i deres onde Hjertes Stivhed; og de gik tilbage og ikke fremad.
25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
Fra den Dag, der eders Fædre udgik af Ægyptens Land, indtil denne Dag sendte jeg til eder alle mine Tjenere, Profeterne, dagligt, tidligt og ideligt.
26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
Men de hørte mig ikke og bøjede ikke deres Øre; men de forhærdede deres Nakke; de gjorde det værre end deres Fædre.
27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
Og du skal tale til dem alle disse Ord, men de skulle ikke høre dig; og du skal kalde ad dem, men de skulle ikke svare dig.
28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
Og du skal sige til dem: Dette er det Folk, som ikke hører paa Herrens, deres Guds Røst og ej annammer Tugt; Troskaben er gaaet til Grunde og forsvunden af deres Mund.
29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
Afklip din Haarprydelse og kast den bort, og opløft et Klagemaal paa de nøgne Høje; thi Herren har forkastet og forladt den Slægt, som hans Fortørnelse er imod.
30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
Thi Judas Børn have gjort det, som er ondt for mine Øjne, siger Herren; de have sat deres Vederstyggeligheder i det Hus, som er kaldet efter mit Navn, til at besmitte det.
31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
Og de have bygget Tofeths Høje, som ere i Ben-Hinnoms Dal, for at opbrænde deres Sønner og Døtre i Ilden, hvilket jeg ikke har budet, og hvad ej heller er kommet mig i Tanke.
32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
Derfor se, de Dage komme, siger Herren, at man ikke skal kalde det mere Tofeth og Ben-Hinnoms Dal, men Morderdal; og de skulle begrave i Tofeth af Mangel paa Plads.
33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
Og dette Folks døde Kroppe skulle være til Føde for Himmelens Fugle og Dyrene paa Jorden, og der skal ingen skræmme dem bort.
34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”
Og jeg vil lade Fryds Røst og Glædes Røst, Brudgoms Røst og Bruds Røst ophøre fra Judas Stæder og fra Gaderne i Jerusalem; thi Landet skal være øde.

< Yeremiya 7 >