< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Утікайте, сини Веніями́на, з сере́дини Єрусалиму, і засурмі́те в сурму́ у Текої, і знак підіймі́ть на Бет-Гаккерем, бо з пі́вночі грізно підно́ситься зло та велике нещастя!
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
І ви́кореню Я Сіонську дочку́, вродли́ву та ви́пещену.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
Пастухи поприхо́дять до неї з своїми стада́ми, понапина́ють наме́ти навко́ло при ній, кожен місце своє випаса́тиме.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
Приготуйте війну проти неї, вставайте та вдармо опі́вдні! Горе нам, бо минає вже день, бо вже тя́гнуться тіні вечі́рні!
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
Уставайте та пі́демо вночі і пони́щмо пала́ти її!
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
Бо так промовляє Господь Саваот: Постина́йте дере́ва та ва́ла насипте при Єрусалимі! Він те місто, що має зруйно́ване бути, в ньому повно наси́льства:
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
як випри́скує воду свою джерело́, так випри́скує він своє зло. Насилля й грабіж чуті в ньому, перед обличчям Моїм безпере́стань хворо́ба та рана.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Будь на́вчений, Єрусалиме, щоб душа Моя не відверну́лась від тебе, щоб тебе не вчинив Я спусто́шенням, незасе́леним кра́єм!
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Так говорить Госпо́дь Савао́т: Позбирають доре́шти оста́нки Ізраїля, мов виноградові ре́штки, — простягни́ свою руку, немов виногра́дар по гро́на!
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
До ко́го я буду казати та сві́дчити буду, — і слуха́тимуть? Необрізане ось їхнє вухо — і слухати уважно не можуть вони, ось слово Господнє для них стало по́сміхом — вони не жада́ють його́!
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
І гніву Господнього по́вен я став, зму́чився я, його стримуючи, — на вулиці виллю його на дітей та на збір юнакі́в одноча́сно, бо схо́плені будуть чоловік із жінкою, старий із віджи́лим літа́,
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
і дістануться іншим доми́ їхні, теж поля́ та жінки́. Бо Я руку Свою простягну́ на мешка́нців цієї землі, говорить Госпо́дь.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Бо вони від мало́го свого й до великого, — усі пожадли́ві на зи́ски, і від пророка та аж до священика роблять неправду.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
І рани наро́ду Мого́ легковажно лікують, говорячи: „Мир, мир“, а миру нема!
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
Чи вони засоромилися, що гидо́ту робили? не засоро́милися ані тро́хи вони й застида́тись не вміють. Тому́ то впадуть між упа́лими в ча́сі, — коли їх навіщу́ Я, спіткну́ться, говорить Госпо́дь.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Так говорить Госпо́дь: На дорогах спині́ться та гляньте, і спитайте про давні стежки́, де то добра дорога, — то нею ідіть, і зна́йдете мир для своєї душі! Та вони відказали: „Не пі́демо!“
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
І Я сторожі́в був поставив над вами, говорячи: Прислуха́йтесь до голосу сурми́! Та вони відказали: „Не будем прислу́хуватись!
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Тому слухайте, люди, і пізнай, ти грома́до, що станеться з ними.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Послухай, ти зе́мле: Ось Я веду́ на наро́д цей лихе, плід їхніх думо́к, бо до слів Моїх не прислуха́лись вони, а Зако́ном Моїм погорди́ли!
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
Наві́що Мені те кади́ло, що з Шеви прихо́дить, запашни́й очере́т із далекого кра́ю? Цілопа́лення ваші не любі Мені, ваші ж жертви Мені не приємні!
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Тому́ то Господь каже так: Ось Я дам спотика́ння оцьо́му наро́дові, і спіткну́ться об них разом ваші батьки́ та сини́, сусід та приятель його, — і загинуть!
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Так говорить Госпо́дь: Ось прихо́дить наро́д із півні́чного кра́ю, і збу́джується люд великий із кі́нців землі.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
Лу́ка та ра́тище міцно тримають, жорстокі вони й милосердя не мають, їхній голос, як море реве́, і гарцю́ють на ко́нях вони. Ушико́ваний, мов чоловік той до бо́ю, на те́бе, о до́чко Сіону!
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
Як почули ми звістку про ньо́го, омлі́ли нам руки, обняла́ нас триво́га та біль, немов в породі́ллі.
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Не вихо́дьте на поле й не йді́те дорогою, бо в во́рога меч та страхі́ття навко́ло!
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
До́чко наро́ду Мого́, — вере́тою підпережи́сь та качайся у по́пелі! Справ жало́бу собі, немов над одноро́дженим, голосі́ння гірке́, — бо при́йде знена́цька руїнник на нас!
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
Я дав був тебе випробо́вувачем у наро́ді Моїм, за тверди́ню, щоб ти знав і випробо́вував їхню доро́гу.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
Вони всі відсту́пники над відсту́пниками, чинять на́клепи, усі вони мідь та залізо, вони згу́бники!
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
Спали́лося ду́хало, від огню́ зникло о́ливо, — нада́рмо стара́нно розто́плювано, бо злих не відді́лено.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Срі́блом відки́неним на́звано їх, бо Госпо́дь їх відкинув“.

< Yeremiya 6 >