< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
“Güvenliğiniz için kaçın, ey Benyamin halkı! Yeruşalim'den kaçın! Tekoa'da boru çalın! Beythakkerem'e bir işaret koyun. Çünkü kuzeyden bir felaket, Büyük bir yıkım gelecek gibi görünüyor.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
Siyon kızını, o güzel, narin kızı yok edeceğim.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
Çobanlar sürüleriyle ona geliyor, Çevresinde çadırlarını kuracaklar. Herkes kendi sürüsünü otlatacak.”
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
“Yeruşalim'e karşı savaş hazırlığı yapın! Kalkın, öğleyin saldırıya geçelim! Vay halimize, gün kararıyor! Akşamın gölgeleri gitgide uzuyor.
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
Haydi, gece saldırıya geçelim, Kentin kalelerini yerle bir edelim.”
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
Her Şeye Egemen RAB diyor ki, “Ağaçları kesin, Yeruşalim'e karşı kuşatma rampaları yapın. Bu kent cezalandırılmalı, İçinde zorbalıktan başka bir şey yok.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
Kuyu suyunu nasıl taze tutuyorsa, Yeruşalim de kötülüğünü öyle taze tutuyor. Şiddet ve yıkım yankılanıyor orada, Karşımda hep hastalık ve yaralar var.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Uyarılara kulak ver, ey Yeruşalim! Yoksa seni bırakacağım, Seni bir viraneye, Oturulmaz bir ülkeye çevireceğim.”
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Her Şeye Egemen RAB diyor ki, “Asmadan nasıl üzüm toplanırsa, İsrail halkından geride kalanları da öyle toplayacaklar. Üzüm toplayan biri gibi Elini yine asma dallarına uzat.”
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
İşitsinler diye kiminle konuşayım, Kimi uyarayım? Kulakları tıkalı, işitemiyorlar. RAB'bin sözünü aşağılıyor, Ondan hoşlanmıyorlar.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
Bu yüzden RAB'bin öfkesiyle doluyum, Kendimi tutmaktan yoruldum. “Sokaktaki çocukların, Toplanan gençlerin üzerine boşalt öfkeni. Nasıl olsa karı da koca da, Yaşlı da yıllarca yaşamış olan da kurtulamayacak.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
Evleri, tarlaları, karıları Başkalarına verilecek, Çünkü ülkede yaşayanlara karşı Elimi kaldıracağım” diyor RAB.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
“Küçük büyük herkes kazanç peşinde, Peygamberler, kâhinler, hepsi halkı aldatıyor.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
Esenlik yokken, ‘Esenlik, esenlik’ diyerek Halkımın yarasını sözde iyileştirdiler.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
Yaptıkları iğrençliklerden utandılar mı? Hayır, ne utanması? Kızarıp bozarmanın ne olduğunu bile bilmiyorlar. Bu yüzden onlar da düşenlerin arasında yer alacak, Onları cezalandırdığımda sendeleyip düşecekler” diyor RAB.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
RAB diyor ki, “Yol kavşaklarında durup bakın, Eski yolları sorun, İyi yol nerede, öğrenin, O yolda yürüyün, Canlarınız rahata kavuşur. Ama onlar, ‘O yolda yürümeyiz’ dediler.
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
Size bekçiler atayıp, ‘Boru sesini dinleyin’ dedim, Ama onlar, ‘Dinlemeyiz’ dediler.
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Bundan ötürü, ey uluslar, Başlarına neler geleceğini işitin! Sen de anla, ey topluluk!
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Dinle, ey yeryüzü! Bu halkın üzerine felaket, Kendi kurduğu düzenin sonucunu getirmek üzereyim. Çünkü sözlerime kulak asmadılar, Kutsal Yasam'ı reddettiler.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
Neden bana Saba'dan günnük, Uzak bir ülkeden güzel kokulu kamış getiriliyor? Yakmalık sunularınızı kabul etmiyorum, Kurbanlarınızdan hoşnut değilim.”
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Bu yüzden RAB diyor ki, “Bu halkın önüne tökezler koyacağım, Babalar da oğullar da Tökezleyip birlikte düşecek, Komşu dostuyla birlikte yok olacak.”
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
RAB diyor ki, “İşte kuzeyden bir ordu geliyor. Dünyanın uçlarından Büyük bir ulus harekete geçiyor.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
Yay, pala kuşanmışlar, Gaddar ve acımasızlar. Atlara binmiş gelirken, Kükreyen denizi andırıyor sesleri. Savaşa hazır savaşçılar Karşına dizilecekler, ey Siyon kızı!”
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
Haberlerini aldık, Ellerimizde derman kalmadı. Doğuran kadın gibi Üzüntü, sancı sardı bizi.
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Kırlara çıkmayın, Yolda yürümeyin! Düşmanın kılıcı orada, Her yer dehşet içinde.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
Ey halkım, çula sarın, Kül içinde yuvarlan. Biricik oğul için yas tutar gibi Acı acı dövün. Çünkü yok edici ansızın gelecek üzerimize.
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
“Seni halkımı deneyesin diye atadım, Öyle ki, onları tanıyıp yollarını sınayasın.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
Hepsi de çok dikbaşlı, Onu bunu çekiştirerek dolaşan insanlardır, Tunç kadar, demir kadar katıdırlar. Hepsi baştan çıkmıştır.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
Körük üfürdükçe üfürüyor, Kurşunu ateşte eritiyor, Ama boşunadır yapılan işlem, Çünkü kötüler arınmıyor.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Onlara gümüş artığı denecek, Çünkü RAB onları reddetti.”

< Yeremiya 6 >