< Yeremiya 6 >
1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Bēgat, Benjamina bērni, no Jeruzālemes, bazūnējat Tekoā, ceļat ugunszīmi BetKeremē, jo bēdas rādās no ziemeļa puses un liels posts.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
Es izdeldu Ciānas meitu, to jauko un vēlīgo.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
Gani uz viņu nāks ar saviem ganāmiem pulkiem, tie uzcels teltis visapkārt ap viņu, tie noganīs ikviens savu vietu.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
Taisāties uz karu pret viņu, ceļaties, ejam pašā dienas vidū. Ak vai, (bēdas) mums! Jo vakars metās un ēnas paliek garākas.
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
Ceļaties, un ejam pašā naktī un izpostīsim viņas jaukos namus.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
Jo tā saka Tas Kungs Cebaot: nocērtiet kokus un uzmetiet valni pret Jeruzālemi; šī ir tā pilsēta, kas taps piemeklēta. Viņas vidū ir tik netaisnība vien.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
Kā avots izverd savu ūdeni, tā viņa izverd savu ļaunumu. Varasdarbu un postu tur dzird, kaušanās un plēšanās bez mitēšanās ir manā priekšā.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Pieņem mācību, Jeruzāleme, lai Mana dvēsele no tevis nenogriežas, lai Es tevi nedaru par tuksnesi, par zemi bez iedzīvotāja.
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Tā saka Tas Kungs Cebaot: kas atliek no Israēla, to tie otrā reizē nolasīs kā vīna koku. Ņem traukus atkal rokā kā vīna ogu lasītājs.
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
Uz ko lai es runāju un dodu liecību, ka tie to dzird? Redzi, viņu ausis ir neapgraizītas, ka tie nevar dzirdēt. Redzi, Tā Kunga vārds tiem ir par apsmieklu, pie tā tiem nav labs prāts.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
Tādēļ es esmu pilns Tā Kunga bardzības, ka nevaru valdīties. Izgāz to arī pār bērniem uz ielām, un pār to jaunekļu draudzi kopā, jo vīri un sievas tiks aizņemti, veci un kas mūžu piedzīvojuši.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
Un viņu nami taps citiem līdz ar tīrumiem un sievām; jo Es izstiepšu Savu roku pret tās zemes iedzīvotājiem, saka Tas Kungs.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Jo visi ir mantas kārīgi, tā mazi kā lieli; tā pravietis kā priesteris, visi dzen viltību.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
Un tie dziedina Manas tautas vainu kā par nieku, sacīdami: miers, miers! Kur tomēr miera nav.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
Tie krituši kaunā, ka darījuši negantību. Bet tie nemaz nekaunas un neprot kauna. Tāpēc tie kritīs starp tiem kritušiem; kad es tos piemeklēšu, tad tiem būs krist, saka Tas Kungs.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Tā saka Tas Kungs: stājaties uz ceļiem un raugāt un vaicājiet pēc tiem senajiem ceļiem, kurš tas labais ceļš, un staigājiet pa to, tad jūs atradīsiet dusu savai dvēselei. Bet tie saka: mēs negribam staigāt.
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
Es arī esmu iecēlis sargus pār jums, klausāties uz trumetes skaņu. Bet tie saka: mēs negribam klausīties.
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Tāpēc klausāties, tautas, un ņem vērā, draudze, kas viņu starpā notiek.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Klausies, zeme! Redzi, Es vedīšu ļaunumu pār šiem ļaudīm, viņu padomu augļus, jo tie neklausās uz Manu vārdu, un Manu bauslību tie atmet.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
Par ko tad Man tas vīraks, kas nāk no Sabas, un tās labās niedres no tālās zemes? Jūsu dedzināmie upuri Man nepatīk, un jūsu kaujamie upuri Man nemīlami.
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Tādēļ Tas Kungs tā saka: redzi, Es šiem ļaudīm likšu piedauzekļus, un tēvi un bērni kopā pie tiem piedauzīsies, kaimiņš ar kaimiņu ies bojā.
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Tā saka Tas Kungs: redzi, tauta nāk no ziemeļa zemes, un liela tauta celsies no pasaules malām;
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
Tā nes stopus un šķēpus, tā ir briesmīga un nežēlīga, viņu balss kauc kā jūra, un tie jāj uz zirgiem; tie ir apbruņoti kā karavīri pret tevi, Ciānas meita.
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
Kad mēs par viņiem baumas dzirdējām, tad mūsu rokas nogura, bailība mums uzbruka un sāpes kā dzemdētājai.
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Neizejat laukā un nestaigājat pa ceļu, jo ienaidnieka zobens ir visapkārt par iztrūcināšanu.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
Ak, mana tauta, apjoz maisu un nometies pelnos, žēlojies kā par vienīgo dēlu, bēdājies gauži, jo postītājs nāk pār mums piepeši.
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
Es tevi esmu iecēlis par pārbaudītāju starp Maniem ļaudīm kā stipru pili, ka tev viņu ceļu būs atzīt un pārbaudīt.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
Tie visi ir tie lielākie atkāpēji un staigā viltībā, tie ir varš un dzelzs, tie visi ir samaitātāji.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
Plēšas ir sadegušas, no viņu uguns nāk tikai svins, kausētājs velti kausējis, jo sārņi nav atšķirti.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Tie top nosaukti par atmestu sudrabu, jo Tas Kungs tos ir atmetis.