< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Υιοί Βενιαμίν, φύγετε μετά σπουδής εκ μέσου της Ιερουσαλήμ και ηχήσατε σάλπιγγα εν Θεκουέ και υψώσατε σημείον εκ πυρός εν Βαιθ-ακκερέμ· διότι κακόν προκύπτει από βορρά και συντριμμός μέγας.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
Παρωμοίασα την θυγατέρα της Σιών με χαρίεσσαν και τρυφεράν γυναίκα.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
Οι ποιμένες και τα ποίμνια αυτών θέλουσιν ελθεί εις αυτήν· θέλουσι στήσει σκηνάς κύκλω εναντίον αυτής· θέλουσι ποιμαίνει έκαστος εν τω τόπω αυτού.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
Ετοιμάσατε πόλεμον κατ' αυτής· σηκώθητε και ας αναβώμεν εν μεσημβρία. Ουαί εις ημάς, διότι κλίνει η ημέρα, διότι εκτείνονται αι σκιαί της εσπέρας.
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
Σηκώθητε και ας αναβώμεν διά νυκτός και ας καταστρέψωμεν τα παλάτια αυτής.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
Διότι ούτω λέγει ο Κύριος των δυνάμεων· Κατακόψατε δένδρα και υψώσατε περιχαρακώματα εναντίον της Ιερουσαλήμ. Αύτη είναι η πόλις, εφ' ην πρέπει να γείνη επίσκεψις· είναι όλη καταδυναστεία εν μέσω αυτής.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
Καθώς η πηγή αναβρύει τα ύδατα αυτής, ούτως αυτή αναβρύει την κακίαν αυτής· βία και αρπαγή ακούονται εν αυτή· ενώπιόν μου ακαταπαύστως είναι πόνος και πληγαί.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Σωφρονίσθητι, Ιερουσαλήμ, μήποτε αποσυρθή η ψυχή μου από σού· μήποτε σε καταστήσω έρημον, γην ακατοίκητον.
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Ούτω λέγει ο Κύριος των δυνάμεων· θέλουσι σταφυλολογήσει ολοτελώς ως άμπελον τα υπόλοιπα του Ισραήλ· επίστρεψον την χείρα σου ως ο τρυγητής εις τα καλάθια.
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
Προς τίνα θέλω λαλήσει και διαμαρτυρηθή, διά να ακούσωσιν; ιδού, το ωτίον αυτών είναι απερίτμητον και δεν δύνανται να ακούσωσιν· ιδού, ο λόγος του Κυρίου είναι προς αυτούς όνειδος· δεν ηδύνονται εις αυτόν.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
Διά τούτο είμαι πλήρης από θυμού του Κυρίου· απέκαμον κρατών εμαυτόν· θέλω εκχέει αυτόν επί τα νήπια έξωθεν και επί την σύναξιν των νέων ομού· διότι και ο ανήρ θέλει πιασθή μετά της γυναικός και ο ηλικιωμένος μετά του πλήρους ημερών.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
Και αι οικίαι αυτών θέλουσι περάσει εις άλλους, οι αγροί και αι γυναίκες ομού, διότι θέλω εκτείνει την χείρα μου επί τους κατοίκους της γης, λέγει Κύριος.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Διότι από μικρού αυτών έως μεγάλου αυτών πας τις εδόθη εις την πλεονεξίαν· και από προφήτου έως ιερέως πας τις πράττει ψεύδος.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
Και ιάτρευσαν το σύντριμμα της θυγατρός του λαού μου επιπολαίως, λέγοντες, Ειρήνη, ειρήνη· και δεν υπάρχει ειρήνη.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
Μήπως ησχύνθησαν, ότε έπραξαν βδέλυγμα; μάλιστα παντελώς δεν ησχύνθησαν ουδέ ηρυθρίασαν· διά τούτο θέλουσι πέσει μεταξύ των πιπτόντων· όταν επισκεφθώ αυτούς, θέλουσιν απολεσθή, είπε Κύριος.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Ούτω λέγει Κύριος· Στήτε επί τας οδούς και ιδέτε και ερωτήσατε περί των αιωνίων τρίβων, που είναι η αγαθή οδός, και περιπατείτε εν αυτή, και θέλετε ευρεί ανάπαυσιν εις τας ψυχάς σας. Αλλ' αυτοί είπον, δεν θέλομεν περιπατήσει εν αυτή.
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
Και κατέστησα σκοπούς εφ' υμάς, λέγων, Ακούσατε τον ήχον της σάλπιγγος. Αλλ' είπον, δεν θέλομεν ακούσει.
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Διά τούτο ακούσατε, έθνη, και συ, συναγωγή, γνώρισον τι είναι μεταξύ αυτών.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Άκουε, γή· ιδού, εγώ θέλω φέρει κακόν επί τον λαόν τούτον, τον καρπόν των διαλογισμών αυτών, διότι δεν επρόσεξαν εις τους λόγους μου και εις τον νόμον μου, αλλ' απέρριψαν αυτόν.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
Τι προς εμέ ο φερόμενος λίβανος από Σεβά και το από γης μακράς ευώδες κιννάμωμον; τα ολοκαυτώματά σας δεν είναι δεκτά ουδέ αι θυσίαι σας ευάρεστοι εις εμέ.
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Διά τούτο ούτω λέγει Κύριος· Ιδού, εγώ θέλω βάλει προσκόμματα έμπροσθεν του λαού τούτου και οι πατέρες και οι υιοί ομού θέλουσι προσκόψει επ' αυτά, ο γείτων και ο φίλος αυτού θέλουσιν απολεσθή.
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Ούτω λέγει ο Κύριος· Ιδού, λαός έρχεται από της γης του βορρά, και έθνος μέγα θέλει εγερθή από των άκρων της γης.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
Τόξον και λόγχην θέλουσι κρατεί· είναι σκληροί και ανίλεοι· φωνή αυτών εκεί ως θάλασσα, και επιβαίνουσιν επί ίππους, παρατεταγμένοι ως άνδρες εις πόλεμον εναντίον σου, θυγάτηρ της Σιών.
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
Ηκούσαμεν την φήμην αυτών· αι χείρες ημών παρελύθησαν· στενοχωρία κατέλαβεν ημάς, ωδίνες ως τικτούσης.
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Μη εξέλθητε εις τον αγρόν και εν οδώ μη περιπατείτε· διότι η ρομφαία του εχθρού είναι τρόμος πανταχόθεν.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
Θυγάτηρ του λαού μου, περιζώσθητι σάκκον και κυλίσθητι εις στάκτην· πένθος μονογενούς κάμε εις σεαυτήν· θρήνησον πικρώς· διότι ο εξολοθρευτής θέλει ελθεί εξαίφνης εφ' ημάς.
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
Σε έθεσα σκοπιάν, φρούριον μεταξύ του λαού μου, διά να γνωρίσης και να εξερευνήσης την οδόν αυτών.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
Πάντες είναι όλως απειθείς, περιπατούσι κακολογούντες· είναι χαλκός και σίδηρος· πάντες είναι διεφθαρμένοι.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
Το φυσητήριον εκαύθη· ο μόλυβδος κατηναλώθη υπό του πυρός· ο χωνευτής διαλύει εις μάτην· διότι οι κακοί δεν εχωρίσθησαν.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Αργύριον αποδεδοκιμασμένον θέλουσιν ονομάσει αυτούς, διότι ο Κύριος απεδοκίμασεν αυτούς.

< Yeremiya 6 >