< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Flee, O ye sons of Benjamin, from Jerusalem, And blow ye the trumpet in Tekoa, And lift up the banner in Beth-haccerem! For evil threateneth from the North; Yea, great destruction.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
O daughter of Zion, the comely and delicate, Thee have I doomed to destruction!
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
The shepherds with their flocks shall come to her; They shall pitch their tents against her round about; They shall feed each one in his place.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
“Prepare ye war against her, [[shall they say; ]] Arise, and let us go up at noonday; Alas for us! for the day goeth away, For the shadows of evening are lengthened.
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
Arise, and let us go up by night, And let us destroy her palaces!”
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
For thus saith Jehovah of hosts: Hew ye down trees, And raise a mound against Jerusalem! She is a city to be punished; She is full of oppression.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
As a fountain sendeth forth its waters, So she sendeth forth her wickedness. Violence and rapine are heard within her; Before me continually are bruises and wounds.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Receive correction, O Jerusalem, Lest my soul be alienated from thee, Lest I make thee a desolation, A land not inhabited!
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Thus saith Jehovah of hosts: They shall thoroughly glean the remnant of Israel as a vine; Turn thy hand like a grape-gatherer again to the baskets!
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
To whom shall I speak? To whom give warning, so that they shall hear? Behold, their ear is uncircumcised, so that they cannot hearken; Behold, the word of Jehovah is to them a derision; They have no delight in it.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
Therefore I am full of the fury of Jehovah; I am weary of holding it; I will pour it out alike upon the children in the street, And upon the assembly of the young men. Yea, also the husband with the wife shall be taken, The old man, and he that is full of days.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
Their houses also shall be transferred to others, Their fields and their wives together, For I will stretch out my hand over the inhabitants of the land, saith Jehovah.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
For from the least of them even to the greatest, Every one is greedy of gain; Prophet and priest alike, Every one of them practiseth deceit.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
They heal the wound of my people slightly, Saying, Peace! peace! when there is no peace.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
Are they ashamed that they have done abominable things? Nay, they are not at all ashamed; They know not how to blush; Therefore shall they fall with them that fall; At the time when I punish them, They shall be cast down, saith Jehovah.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Thus saith Jehovah: Stand ye upon the ways and look; And ask for the old paths, “Where is the good way?” Walk ye in it, and ye shall find for yourselves rest. But they say, We will not walk in it.
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
I have also set watchmen over you, [[saying, ]] Hearken to the sound of the trumpet! But they say, We will not hearken.
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Therefore hear, O ye nations, And know, ye assembled multitude, What shall come upon them!
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Hear thou, O earth! Behold, I bring evil upon this people, The fruit of their devices; Because they have not hearkened to my words, And have even rejected my law.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
To what purpose is incense brought to me from Sheba, And the sweet-smelling reed from a far country? Your burnt-offerings are not acceptable, Nor are your sacrifices sweet to me.
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Therefore thus saith Jehovah: Behold, I lay stumbling-blocks before this people, Upon which fathers and sons shall stumble together, The neighbor and his friend, and shall perish.
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Thus saith Jehovah: Behold, a people cometh from the land of the North; A great nation riseth up from the extremities of the earth.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
They bear the bow and the spear; They are cruel and show no mercy; Their voice roareth like the sea; And upon horses do they ride, Arrayed as a warrior against thee, O daughter of Zion.
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
We have heard the report thereof; Our hands lose their strength; Anguish hath taken hold of us, Pain, as of a woman in travail.
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Go not forth into the field, Nor walk ye in the highway! For the sword of the enemy And terror are on every side.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
O daughter of my people, gird thee with sackcloth, And roll thyself in ashes! Make thee mourning as for an only son, Most bitter lamentation! For suddenly shall the spoiler come upon us.
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
I have set thee, like a tower, for an assayer among my people, That thou mayst know and try their way.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
They are all stubborn revolters, Slanderers are they, brass and iron; They are all corrupt.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
The bellows burn; The lead is consumed by the fire; The refiner hath melted in vain, For the bad are not separated.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Rejected silver shall men call them, Because Jehovah hath rejected them.

< Yeremiya 6 >