< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Put yourselves under covert, ye children of Benjamin, away from the midst of Jerusalem, and blow the horn in Tekoa, and set up a signal on Beth-cherem; for evil looketh forth from the north, and a great destruction.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
The comely and delicate one, the daughter of Zion, will I cut off.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
Shepherds with their flocks come unto her; they pitch their tents against her round about; they feed bare every one what is nigh at hand.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
'Prepare ye war against her; arise, and let us go up at noon!' 'Woe unto us! for the day declineth, for the shadows of the evening are stretched out!'
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
'Arise, and let us go up by night, and let us destroy her palaces.'
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
For thus hath the LORD of hosts said: hew ye down her trees, and cast up a mound against Jerusalem; this is the city to be punished; everywhere there is oppression in the midst of her.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
As a cistern welleth with her waters, so she welleth with her wickedness; violence and spoil is heard in her; before Me continually is sickness and wounds.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Be thou corrected, O Jerusalem, lest My soul be alienated from thee, lest I make thee desolate, a land not inhabited.
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Thus saith the LORD of hosts: They shall thoroughly glean as a vine the remnant of Israel; turn again thy hand as a grape-gatherer upon the shoots.
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
To whom shall I speak and give warning, that they may hear? Behold, their ear is dull, and they cannot attend; behold, the word of the LORD is become unto them a reproach, they have no delight in it.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
Therefore I am full of the fury of the LORD, I am weary with holding in: pour it out upon the babes in the street, and upon the assembly of young men together; for even the husband with the wife shall be taken, the aged with him that is full of days.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
And their houses shall be turned unto others, their fields and their wives together; for I will stretch out My hand upon the inhabitants of the land, saith the LORD.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
For from the least of them even unto the greatest of them every one is greedy for gain; and from the prophet even unto the priest every one dealeth falsely.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
They have healed also the hurt of My people lightly, saying: 'Peace, peace', when there is no peace.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
They shall be put to shame because they have committed abomination; yea, they are not at all ashamed, neither know they how to blush; therefore they shall fall among them that fall, at the time that I punish them they shall stumble, saith the LORD.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Thus saith the LORD: Stand ye in the ways and see, and ask for the old paths, where is the good way, and walk therein, and ye shall find rest for your souls. But they said: 'We will not walk therein.'
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
And I set watchmen over you: 'Attend to the sound of the horn', but they said: 'We will not attend.'
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Therefore hear, ye nations, and know, O congregation, what is against them.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Hear, O earth: Behold, I will bring evil upon this people, even the fruit of their thoughts, because they have not attended unto My words, and as for My teaching, they have rejected it.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
To what purpose is to Me the frankincense that cometh from Sheba, and the sweet cane, from a far country? Your burnt-offerings are not acceptable, nor your sacrifices pleasing unto Me.
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Therefore thus saith the LORD: Behold, I will lay stumblingblocks before this people, and the fathers and the sons together shall stumble against them, the neighbour and his friend, and they shall perish.
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Thus saith the LORD: Behold, a people cometh from the north country, and a great nation shall be roused from the uttermost parts of the earth.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
They lay hold on bow and spear, they are cruel, and have no compassion; their voice is like the roaring sea, and they ride upon horses; set in array, as a man for war, against thee, O daughter of Zion.
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
'We have heard the fame thereof, our hands wax feeble, anguish hath taken hold of us, and pain, as of a woman in travail.'
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Go not forth into the field, nor walk by the way; for there is the sword of the enemy, and terror on every side.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
O daughter of my people, gird thee with sackcloth, and wallow thyself in ashes; make thee mourning, as for an only son, most bitter lamentation; for the spoiler shall suddenly come upon us.
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
I have made thee a tower and a fortress among My people; that thou mayest know and try their way.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
They are all grievous revolters, going about with slanders; they are brass and iron; they all of them deal corruptly.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
The bellows blow fiercely, the lead is consumed of the fire; in vain doth the founder refine, for the wicked are not separated.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Refuse silver shall men call them, because the LORD hath rejected them.

< Yeremiya 6 >