< Yeremiya 52 >

1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Сущу двадесяти и единому лету Седекии, внегда нача царствовати, и царствова во Иерусалиме единонадесять лет: и имя матери его Амиталь, дщи Иеремиина, от Ловны.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
И сотвори лукавое пред очима Господнима по всему, елико творяше Иоаким:
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
яко ярость Господня бысть на Иерусалим и на Иуду, дондеже отверже их от лица Своего: и отступи Седекиа от царя Вавилонска.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
И бысть в девятое лето царства его, в десятый месяц, в десятый день месяца, прииде Навуходоносор царь Вавилонский и вся сила его на Иерусалим, и облегоша его и сотвориша окрест его острог от четвероуголных камений.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
И бысть во облежении град даже до первагонадесяте лета царства Седекиина.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
Месяца же четвертаго в девятый день, утвердися глад во граде, и не бяше хлеба людем земли.
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
И просекоша град, и вси мужие воинстии изыдоша нощию путем врат, иже есть между двема стенама, иже бяше прямо вертограду цареву, Халдее же добываху град окрест лежаще, и отидоша путем в пустыню.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
И погна сила Халдейска вслед царя и постиже его об ону страну Иерихона, и вси отроцы его разсыпашася от него.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
И яша царя и приведоша и ко царю Вавилонскому в Девлаф, иже есть в земли Емаф, и глагола ему с судом.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
И изсече царь Вавилонский сыны Седекиины пред очима его, и вся князи Иудины изсече в Девлафе.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
Очи же Седекии изят, и связа его оковами, и приведе его царь Вавилонский в Вавилон и вдаде его в дом жерновный до дне, в оньже умре.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
В десятый же день пятаго месяца (лето сие девятоенадесять Навуходоносору царю Вавилонску) прииде Навузардан архимагир, стоящь пред лицем царя Вавилонска, во Иерусалим,
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
и сожже храм Господень и дом царев, и вся домы градския и всяк дом велик сожже огнем,
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
и всяку стену Иерусалимлю окрест разори сила Халдейска, яже бяше со архимагиром.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
И от убогих людий, и останок людий, и оставшихся во граде и избегших, иже убежаша ко царю Вавилонску, и прочий народ пресели Навузардан воевода:
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
прочиих же остави людий убогих в делатели винограда и земледелцев.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
Столпы же медяныя, иже во храме Господни, и подставы, и море медяное, еже во храме Господни, сокрушиша Халдее, и взяша медь их, и отнесоша в Вавилон:
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
и венец и чашы, и вилицы и вся сосуды медяныя, в нихже служаху,
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
и фимиамники и чашы, и умывалницы и свещники, и кадилницы и чашицы, яже бяху златая и яже бяху сребряная, взя архимагир.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
И столпа два и море едино, и телцев дванадесять медяных под морем, яже сотвори царь Соломон во храме Господни, не бе веса меди сосуд тех.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
Столп же кийждо осминадесяти лактей бе в высоту, вервь же дванадесяти лактей окрест его обдержаше, и толстота его четырех перст окрест,
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
и глава на них медяна, пять лакот высота главы единыя, и мрежа, и шипки на венце окрест, все бяше медяно: такожде бысть и вторый столп.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
И бяше шипков девятьдесят и шесть едина страна, и бяше всех шипков над мрежею окрест сто.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
И взя архимагир Сареа жерца старейшаго и жерца Софонию втораго и триех стрегущих путь.
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
И от града взя каженика единаго, иже бе приставник людий воинских, и седмь мужей нарочитых, иже пред лицем царевым обретошася во граде, и книгочия сил учащаго людий земли, и шестьдесят мужей от людий земли, иже обретошася среде града:
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
и взя их Навузардан архимагир и приведе я ко царю Вавилонску в Девлаф.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
И изби я царь Вавилонский в Девлафе в земли Емаф: и преселен бысть Иуда от земли своея.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
Сии суть людие, ихже пресели Навуходоносор в седмое лето, Иудеев три тысящы и двадесять и три:
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
во осмоенадесять лето Навуходоносор из Иерусалима душ осмь сот тридесять и две пресели.
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
В двадесять третие лето Навуходоносора пресели Навузардан архимагир Иудеев душ седмь сот и четыредесять пять, всех же душ четыре тысящы и шесть сот.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
И бысть в тридесять седмое лето преселения Иоакима царя Иудина, в двадесять пятый день месяца вторагонадесять, вознесе Евилмеродах царь Вавилонский в первое лето царства своего главу Иоакима царя Иудина, и изведе его из храма, в немже стрежашеся, и глагола ему благая:
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
и даде престол его выше царей, иже с ним, в Вавилоне,
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
и измени ризы его темничныя, и ядяше хлеб всегда пред лицем его во вся дни живота своего:
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
и урок ему даяшеся всегда от царя Вавилонска, даже до дне, в оньже умре, во вся дни живота его.

< Yeremiya 52 >