< Yeremiya 52 >
1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Sedekiasz miał dwadzieścia jeden lat, kiedy zaczął królować, i królował jedenaście lat w Jerozolimie. Jego matka [miała] na imię Chamutal [i była] córką Jeremiasza z Libny.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
Czynił on to, co złe w oczach PANA, zupełnie tak, jak czynił Joakim.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
Z powodu gniewu PANA przyszło to na Jerozolimę i Judę, aż odrzucił ich sprzed swego oblicza. Sedekiasz bowiem zbuntował się przeciw królowi Babilonu.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
W dziewiątym roku jego panowania, dziesiątego miesiąca, dziesiątego [dnia] tego miesiąca Nabuchodonozor, król Babilonu, wraz z całym swym wojskiem wyruszył przeciw Jerozolimie, rozbił obóz pod nią i zbudował przeciwko niej szańce dokoła.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
Miasto więc było oblężone aż do jedenastego roku króla Sedekiasza.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
A w czwartym miesiącu, dziewiątego [dnia] tego miesiąca, wzmógł się głód w mieście i nie było chleba dla ludu tej ziemi.
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
Kiedy zrobiono wyłom w [murze] miasta, wszyscy wojownicy uciekli i wyszli z miasta w nocy przez bramę między dwoma murami obok królewskiego ogrodu; Chaldejczycy zaś leżeli wokół miasta, a [tamci] poszli w stronę pustyni.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
Lecz wojsko Chaldejczyków ścigało króla i dogoniło Sedekiasza na równinach Jerycha, a całe jego wojsko rozpierzchło się od niego.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
Pojmali więc króla i przyprowadzili go do króla Babilonu, do Ribla w ziemi Chamat, gdzie ten wydał na niego wyrok.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
Król Babilonu zabił synów Sedekiasza na jego oczach, a także wszystkich książąt Judy pozabijał w Ribla.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
A Sedekiaszowi wyłupił oczy, potem król Babilonu zakuł go w łańcuchy, uprowadził go do Babilonu i wsadził do więzienia aż do jego śmierci.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
W piątym miesiącu, dziesiątego dnia [tego] miesiąca – był to dziewiętnasty rok Nabuchodonozora, króla Babilonu – do Jerozolimy przybył Nebuzaradan, dowódca gwardii, sługa króla Babilonu.
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
I spalił dom PANA i dom króla; wszystkie domy Jerozolimy i wszystkie wielkie budowle spalił ogniem.
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
Całe wojsko Chaldejczyków, które [było] z dowódcą gwardii, zburzyło wszystkie mury wokół Jerozolimy.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
A część ubogich z ludu i resztę ludu, która pozostała w mieście, zbiegów, którzy przeszli do króla Babilonu, oraz resztę pospólstwa Nebuzaradan, dowódca gwardii, uprowadził do niewoli;
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
Lecz pozostawił niektórych z ubogich tej ziemi, aby byli winogrodnikami i rolnikami.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
Chaldejczycy rozbili kolumny z brązu, które [były] w domu PANA, podstawy i morze z brązu, które [było] w domu PANA, a brąz z nich przenieśli do Babilonu.
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
Zabrali też kotły, szufle, nożyce, miski, czasze oraz wszystkie naczynia z brązu, których używano do służby.
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
Dowódca gwardii zabrał kropielnice, kadzielnice, misy, kotły, świeczniki, czasze i kubki; co było ze złota – jako złoto, co było ze srebra – jako srebro;
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
Dwie kolumny, jedno morze i dwanaście wołów z brązu, które [były] pod podstawami, a które wykonał król Salomon w domu PANA; a nie było można [zmierzyć wagi] brązu tych wszystkich przedmiotów.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
[Co do] kolumn, to każda miała osiemnaście łokci wysokości i dwanaście łokci obwodu, jej grubość wynosiła cztery palce, a w środku była pusta;
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
Głowica na niej była z brązu, wysokość jednej głowicy [wynosiła] pięć łokci, naokoło głowicy była siatka i jabłka granatowe, wszystko z brązu. Tak samo było z jabłkami granatu drugiej kolumny.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
A tych jabłek granatu było dziewięćdziesiąt sześć [po każdej] stronie; wszystkich jabłek granatu było po sto na siatce wokoło.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
Dowódca gwardii pojmał też najwyższego kapłana Serajasza, drugiego kapłana Sofoniasza i trzech stróżów progu.
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
Z miasta zaś zabrał dworzanina, który był przełożonym nad wojownikami, siedmiu [z tych, którzy] stawali przed królem, a których znaleziono w mieście, naczelnego pisarza wojskowego, dokonującego spisu ludu tej ziemi, oraz sześćdziesięciu mężczyzn spośród ludu tej ziemi, których znaleziono w mieście.
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
Tych więc zabrał Nebuzaradan, dowódca gwardii, i zaprowadził ich do króla Babilonu do Ribla.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
I król Babilonu pobił ich, i uśmiercił w Ribla, w ziemi Chamat. Tak został uprowadzony Juda ze swojej ziemi.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
Taka jest [liczba] ludu, który Nabuchodonozor uprowadził do niewoli: w siódmym roku trzy tysiące dwudziestu trzech Żydów.
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
W osiemnastym roku Nabuchodonozora, uprowadził z Jerozolimy osiemset trzydzieści dwie osoby.
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
W dwudziestym trzecim roku Nabuchodonozora dowódca gwardii Nebuzaradan uprowadził spośród Żydów siedemset czterdzieści pięć osób. Razem cztery tysiące sześćset osób.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
A w trzydziestym siódmym roku po uprowadzeniu do niewoli Joachina, króla Judy, w dwunastym miesiącu, dwudziestego piątego [dnia] tego miesiąca, Ewil-Merodak, król Babilonu, w roku objęcia królestwa, wywyższył głowę Joachina, króla Judy, i uwolnił go z więzienia;
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
Rozmawiał z nim łaskawie i ustawił jego tron wyżej niż tron królów, którzy [byli] z nim w Babilonie;
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
I zmienił jego szaty więzienne. I jadał on chleb zawsze przed nim po wszystkie dni swego życia.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
Na jego utrzymanie zapewniono mu dzienną porcję przez króla Babilonu aż do jego śmierci, po wszystkie dni jego życia.