< Yeremiya 52 >

1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
UZedekhiya waba yinkosi eleminyaka engamatshumi amabili lanye, njalo wabusa eJerusalema okweminyaka elitshumi lanye. Ibizo likanina lalinguHamuthali indodakazi kaJeremiya waseLibhina.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
Wenza okubi emehlweni kaThixo, njengalokho okwakwenziwe nguJehoyakhimi.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
Kwakungenxa yokuthukuthela kukaThixo ukuze kwenzakale konke lokhu eJerusalema lakoJuda, njalo ekucineni kwabangela ukuthi uThixo abachithe. Ngalokho uZedekhiya wayihlamukela inkosi yaseBhabhiloni.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
Ngakho ngenyanga yesificamunwemunye yokubusa kukaZedekhiya, ngosuku lwetshumi lwenyanga yetshumi, uNebhukhadineza inkosi yaseBhabhiloni, waya eJerusalema lebutho lakhe lonke. Bahlala ngaphandle kwedolobho, bakha izinqaba zokulivimbezela kuzozonke inhlangothi zalo.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
Idolobho lavinjezelwa kwaze kwaba ngumnyaka wetshumi lanye kaZedekhiya inkosi.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
Ngosuku lwesificamunwemunye lwenyanga yesine indlala yayisinzima edolobheni, abantu bengaselakudla.
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
Umduli wedolobho wafohlwa, ibutho lonke labaleka. Basuka edolobheni ebusuku bephuma ngesango eliphakathi kwemiduli emibili, phansi kwesivande senkosi, lanxa nje amaKhaladiya ayeligombolozele idolobho. Babaleka beqonde e-Arabha,
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
kodwa ibutho lamaKhaladiya laxotshana lenkosi uZedekhiya layamfica emagcekeni aseJerikho. Wonke amabutho akhe ehlukana laye njalo ahlakazeka,
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
yena wathunjwa. Wasiwa enkosini yaseBhabhiloni eRibhila elizweni laseHamathi, lapho eyamgwebela khona.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
Khona eRibhila inkosi yaseBhabhiloni yabulala amadodana kaZedekhiya emehlweni akhe; yabulala lezikhulu zakoJuda zonke.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
Emva kwalokho, yamkhupha amehlo uZedekhiya, yambopha ngamaketane ethusi, yamusa eBhabhiloni, lapho eyamfaka khona entolongweni kwaze kwafika usuku lokufa kwakhe.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
Ngosuku lwetshumi ngenyanga yesihlanu, ngomnyaka wetshumi lasificamunwemunye kaNebhukhadineza inkosi yaseBhabhiloni, uNebhuzaradani umlawuli wabalindi besikhosini, owayesebenzela inkosi yaseBhabhiloni, wafika eJerusalema.
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
Wathungela ithempeli likaThixo ngomlilo, lesigodlo senkosi lezindlu zonke zaseJerusalema. Zonke izindlu eziqakathekileyo wazitshisa.
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
Lonke ibutho laseBhabhiloni elalingaphansi komlawuli wabalindi besikhosini layidiliza yonke imiduli eyayigombolozele iJerusalema.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
UNebhuzaradani umlawuli wabalindi wathatha abanye babayanga bokucina wabasa ekuthunjweni lalabo ababesele edolobheni, lenengi lezingcwethi kanye lalabo abasebeye enkosini yaseBhabhiloni.
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
Kodwa uNebhuzaradani watshiya inengi labantu ababengabayanga bokucina elizweni ukuba basebenze ezivinini lasemasimini.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
AbeBhabhiloni baphahlaza izinsika zethusi lezinti zezibane loLwandle lwethusi, okwakusethempelini likaThixo. Bathwalela ithusi lelo eBhabhiloni.
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
Bathatha njalo imbiza, lamafotsholo, lezindlawu lemiganu yezichelo, lezinditshi lazozonke izitsha zethusi ezazisetshenziswa enkonzweni yasethempelini.
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
Umlawuli wabalindi besigodlo wathatha izinditshi, izitsha zokutshisela impepha, imiganu yezichelo, imbiza, izinti zezibane, izinditshi lemiganu okusetshenziswa eminikelweni yokunathwayo konke okwakwenziwe ngegolide elicengekileyo loba isiliva.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
Ithusi elalivela ensikeni ezimbili, loLwandle lelenkunzi zethusi ezilitshumi lambili ezazingaphansi kwalo kanye lelezidindi ezisusekayo konke okwakwenzelwe ithempeli likaThixo yinkosi uSolomoni, kwakulesisindo esasingelinganiswe.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
Ubude bensika ngayinye babuzingalo ezilitshumi lasificaminwembili, ubuqatha buzingalo ezilitshumi lambili, uhlonzi luyiminwe emine njalo ilomhome.
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
Isiduku sethusi phezu kwenye insika sasizingalo ezinhlanu ubude baso njalo siceciswe ngomeluko lamaphomegranathi ethusi nxazonke. Enye insika, lamaphomegranathi ayo, layo yayinjalo.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
Emaceleni kwakulamaphomegranathi angamatshumi ayisificamunwemunye munye lesithupha; esewonke amaphomegranathi ayengaphezu kobufikifiki obabuzungezile, ayelikhulu.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
Umlawuli wabalindi wathumba uSeraya induna yabaphristi, loZefaniya umsekeli wakhe kanye labalindi bomnyango abathathu.
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
Kulabo ababelokhu besedolobheni wathatha isikhulu esasiphethe amadoda okulwa, labacebisi besikhosini abayisikhombisa. Wathatha lonobhala owayeyinduna eyayiphethe ukubuthwa kwabantu elizweni kanye labanye abantu bakhe abangamatshumi ayisithupha ababeficwe edolobheni.
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
UNebhuzaradani umlawuli wabathatha bonke wabasa enkosini yaseBhabhiloni eRibhila.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
Khonale eRibhila, elizweni laseHamathi, inkosi yathi kabaqunywe. Ngakho abakoJuda baya ekuthunjweni kude lelizwe labo.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
Nanka amanani abantu uNebhukhadineza abasa ekuthunjweni: ngomnyaka wesikhombisa, amaJuda azinkulungwane ezintathu lamatshumi amabili lantathu;
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
ngomnyaka kaNebhukhadineza wetshumi lasificaminwembili mibili, abantu beJerusalema abangamakhulu ayisificamunwemunye lamatshumi amathathu lambili;
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
ngomnyaka wakhe wamatshumi amabili lantathu, amaJuda angamakhulu ayisikhombisa lamatshumi amane lanhlanu asiwa ekuthunjweni nguNebhuzaradani umlawuli wabalindi ekubusweni kwezizwe ezinengi. Bebonke kwakungabantu abazinkulungwane ezine lamakhulu ayisithupha.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
Ngomnyaka wamatshumi amathathu lesikhombisa uJehoyakhini inkosi yakoJuda esekuthunjweni, ngomnyaka u-Evili-Merodakhi aba yinkosi yaseBhabhiloni ngawo, wakhulula uJehoyakhini inkosi yakoJuda, wamkhupha entolongweni ngosuku lwamatshumi amabili lanhlanu lwenyanga yetshumi lambili.
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
Wakhuluma laye ngomusa, wamnika isihlalo esihloniphekayo esasingaphezu kwezamanye amakhosi ayelaye eBhabhiloni.
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
Ngakho uJehoyakhini wakhupha izigqoko zakhe zasentolongweni, wadla lenkosi izikhathi zonke okwempilo yakhe yonke.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
Nsuku zonke inkosi yaseBhabhiloni yayinika uJehoyakhini isabelo esimisiweyo malanga wonke empilweni yakhe, kwaze kwafika ilanga lokufa kwakhe.

< Yeremiya 52 >