< Yeremiya 52 >
1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
HE iwakaluakumamakahi na makahiki o Zedekia, ia ia i hoomaka ai e noho aupuni; a noho aupuni iho la oia ma Ierusalema, he umikumamakahi makahiki. O Hamutala ka inoa o kona makuwahine; o ke kaikamahine ia a Ieremia no Libena.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
Hana hewa iho la oia imua o na maka o Iehova, e like me na mea a pau a Iehoiakima i hana'i.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
No ka ukiuki o Iehova i hiki ai keia mau mea ma Ierusalema, a ma Iuda, a kipaku aku oia ia lakou mai kona alo aku, a kipi o Zedekia i ke alii o Babulona.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
A hiki i ka makahiki eiwa o ka makahiki o kona noho aupuni ana, i ka malama umi, i ka umi o ka la o ka malama, hele mai la o Nebukaneza, ke alii o Babulona, oia, a me kona poe kaua a pau e ku e ia Ierusalema, a hoomoana ku e oia ia wahi, a hana iho la i mau puu kaua a puni ia.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
Pela i hoopilikiaia ke kulanakauhale a hiki i ka makahiki umikumamakahi o ke alii o Zedekia.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
A i ka malama aha, i ka iwa o ka la o ka malama, nui loa ka wi iloko o ke kulanakauhale, aohe berena no na kanaka o ka aina.
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
Alaila wahiia ke kulanakauhale, a hee na kanaka kaua a pau, a puka aku la iwaho o ke kulanakauhale, ma ke ala o ka pukapa mawaena o na pa elua, aia ma ka mahinaai o ke alii: (ua puni hoi ke kulanakauhale i ko Kaledea; ) a hele ae la lakou ma ke ala o ka papu.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
Alaila, hahai ka poe kaua o ko Kaledea, mahope o ke alii, a loaa o Zedekia ia lakou ma na papu o Ieriko, a ua hoopuehuia'ku la kona poe kaua, mai ona aku la.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
Alaila, hoopio lakou i ke alii, a lawe aku la ia ia i ke alii o Babulona, ma Ribela, ma ka aina o Hamata; a malaila oia i hoohewa'i ia ia.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
A pepehi ke alii o Babulona i na keiki a Zedekia imua o kona maka; a pepehi no hoi oia i na luna a pau o ka Iuda ma Ribela.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
A poalo iho la oia i na maka o Zedekia, a hoopaa no hoi ke alii o Babulona ia ia i na kupe keleawe, a lawe aku la ia ia i Babulona, a waiho aku la ia ia iloko o ka halepaahao, a i ka la o kona make ana.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
A i ka malama elima, i ka umi o ka la o ka malama, oia hoi ka makahiki umikumamaiwa o Nebukaneza, ke alii o Babulona, alaila hele mai la i Ierusalema o Nebuzaredana, ka lunakaua, nana i hookauwa na ke alii o Babulona.
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
A puhi iho la oia i ka hale o Iehova, a me ka hale o ke alii, a me na hale a pau o Ierusalema, a me na hale o ka poe koikoi, puhi no oia ia mau mea i ke ahi.
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
A o na kanaka kaua a pau o ko Kaledea, ka poe mamuli o ka lunakaua, hoohiolo lakou i na pa a pau o Ierusalema a puni.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Alaila, lawe pio aku la o Nebuzaredana, ka lunakaua i na kanaka hune, a me na kanaka i koe ma ke kulanakauhale, a me ka poe i hele, na mea hoi i hele i ke alii o Babulona, a me ka nui o ka poe i koe.
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
Waiho no nae o Nebuzaredana, ka lunakaua i kekahi poe hune o ka aina i poe paipai kumuwaina, a i poe mahiai hoi.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
Wawahi no hoi ko Kaledea i na kia keleawe iloko o ka hale o Iehova, a me na poho a me na ipu auau keleawe, ka mea maloko o ka hale o Iehova, a lawe lakou i ke keleawe a pau o ia mau mea i Babulona,
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
A lawe aku no hoi lakou i na ipu wai nui, a me na kopelehu, a me na upa kukui, a me na paipu a me na puna a me na ipu keleawe a pau, na mea lawelawe o lakou.
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
A lawe aku no hoi ka lunakaua i na ipu, a me na paahi, a me na paipu, a me na ipu wai nui, a me na ipukukui manamana, na puna, a me na kiaha; o ka mea gula, he gula, a o ka mea kala, he kala.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
I na kia elua, hookahi ipu auau, he umikumamalua bipi kane na mea malalo iho o na poho, na mea a ke alii a Solomona i hana'i maloko o ka hale o Iehova. Pau ole ke keleawe o keia mau mea hana a pau, ke kaupaonaia.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
A o na kia, he umikumamawalu kubita ke kiekie o kekahi kia, a puni hoi ia i ke apo, he umikumamalua kubita; eha lima kona manoanoa; ua kawaha.
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
A he papale keleawe maluna ona. Elima kubita ke kiekie o kekahi papale, me ka mea ulana pukapuka, a me na pomegerane maluna o na papalekia a puni, ho keleawe a pau loa. A ua like hoi me neia ka lua o ke kia, a me na pomegerane.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
A he kanaiwakumamaono na pomegerano o kekahi aoao; o na pomegerane a pau ma ka mea ulana pukapuka, hookahi haneri a puni.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
A lawe aku la ka lunakoa ia Seraia ke kahuna nui, a ia Zepania ke kahuna lua, a me na kiaipuka ekolu.
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
Lawe aku la hoi oia mai ke kulanakauhale aku i kekahi luna i poaia, i hoonohoia maluna o na kanaka kaua, a i ehiku kanaka punahele o ke alii, na mea i loaa ma ke kulanakauhale; a i ke kakauolelo o ka lunakaua, nana i alakai i na kanaka o ka aina i ke kaua; a me na kanaka o ka aina he kanaono i loaa ma ke kulanakauhale.
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
A lawe aku la o Nebuzaradana ka lunakoa ia lakou i ke alii o Babulona ma Ribela.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
Pepehi aku la ke alii o Babulona ia lakou, a make lakou ia ia ma Ribela i ka aina o Hamata. A ua laweia aku la o ka Iuda mai ko lakou aina aku.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
Oia na kanaka a Nebukaneza i lawe pio aku ai: i ka hiku o ka makahiki, ekolu tausani na Iudaio, a me ka iwakaluakumamakolu.
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
I ka makahiki umikumamawalu o Nebukaneza, lawe pio aku la oia mai Ierusalema aku, i ewalu haneri me kanakolukumamalua kanaka.
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
I ka makahiki iwakaluakumamakolu o Nebukaneza, lawe pio aku la o Nebuzaradana ka lunakaua i ehiku haneri me kanahakumamalima kanaka o na Iudaio. A oia poe kanaka a pau, eha tausani lakou me na haneri keu eono.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
A i ka makahiki kanakolukumamahiku, o ke pio ana o Iehoiakina, ke alii o ka Iuda, i ka malama umikumamalua, i ka la iwakaluakumamalima o ka malama, o Evila Merodaka, ke alii o Babulona, i ka makahiki mua o kona noho aupuni ana, hapai ae la oia i ke poo o Iehoiakina, ke alii o ka Iuda, a lawe ae la ia ia iwaho o ka halepaahao.
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
A olelo oluolu iho la oia ia ia, a hoonoho iho la i kona nohoalii maluna o ka nohoalii o na'lii e noho pu ana me ia ma Babulona.
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
A no ka lole o ka halepaahao, haawi ae la oia i lole hou; a ai mau oia i ka ai imua ona, i na la a pau o kona ola ana.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
A o kana ai hoi, na ke alii o Babulona i haawi i ai mau nana, he puu no i kela la i keia la a hiki i ka la o kona make ana, i na la a pau o kona ola aua.