< Yeremiya 52 >

1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Sédécias avait vingt-et-un ans lors de son avènement, et il règna onze ans à Jérusalem; le nom de sa mère était Hamoutal, fille de Jérémie de Libna.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
Il fit ce qui est mal aux yeux de l’Eternel, tout comme avait agi Joïakim.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
C’Est ainsi que la colère de Dieu se manifesta contre Jérusalem et Juda, jusqu’à ce qu’il les eût rejetés de devant sa face. Or. Sédécias entra en révolte contre le roi de Babylone.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
Alors, dans la neuvième année de son règne, le dixième mois et le dixième jour du mois, Nabuchodonosor, roi de Babylone, marcha avec toute son armée contre Jérusalem; ils campèrent sous ses murs et élevèrent des retranchements sur toute son enceinte.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
La ville subit le siège jusqu’à la onzième année du règne de Sédécias.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
Le quatrième mois, le neuvième jour du mois, la famine sévit dans la ville et les gens du peuple manquèrent de pain.
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
Alors la ville fut ouverte par une brèche. Aussitôt tous les gens de guerre s’enfuirent en quittant la ville nuitamment par la porte du double rempart, attenante au parc du roi, tandis que les Chaldéens cernaient la ville, et ils prirent la direction de la Plaine.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
L’Armée chaldéenne se mit à la poursuite du roi, et elle atteignit Sédécias dans la plaine de Jéricho, alors que sa propre armée s’était débandée en l’abandonnant.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
On fit le roi prisonnier et on l’amena au roi de Babylone à Ribla dans le district de Hamat, et celui-ci prononça sa sentence.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
Le roi de Babylone fit égorger les fils de Sédécias sous ses yeux; il fit aussi égorger tous les notables de Juda à Ribla.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
Puis il fit crever les yeux à Sédécias et le chargea de chaînes. Enfin le roi de Babylone le déporta à Babylone, où il l’enferma dans la maison de détention jusqu’au jour de sa mort.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
Le dixième jour du cinquième mois, qui correspond à la dix-neuvième année du règne de Nabuchodonosor, roi de Babylone, Nebouzaradan, chef des gardes, serviteur du roi de Babylone, entra dans Jérusalem.
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
Il mit le feu au temple du Seigneur et au palais du roi; de même il livra aux flammes toutes les maisons de Jérusalem, à savoir toute maison d’un personnage important.
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
Et tous les remparts qui entouraient Jérusalem furent démolis par l’armée chaldéenne, placée sous les ordres du chef des gardes.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Une partie de la basse classe et le reste de la population qui était demeurée dans la ville, les transfuges qui s’étaient rendus au roi de Babylone et le surplus de la multitude furent envoyés en exil par Nebouzaradan, chef des gardes.
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
Le chef des gardes, Nebouzaradan, ne laissa dans le pays que des gens de la classe inférieure comme vignerons et laboureurs.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
Les colonnes d’airain qui se trouvaient dans la maison de Dieu, les supports et la Mer d’airain du temple, les Chaldéens les mirent en pièces et en emportèrent l’airain à Babylone.
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
Ils prirent aussi les cendriers, les pelles, les couteaux, les bassins, les cuillers et tous les ustensiles d’airain qui servaient au culte.
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
Le chef des gardes s’empara encore des marmites, des brasiers; des bassins, des poêles, des chandeliers, des écuelles et des tasses tant en or qu’en argent.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
Quant aux deux colonnes, à la Mer unique, aux douze boeufs en airain placés sous les supports que le roi Salomon avait faits pour le temple du Seigneur, le poids de l’airain de tous ces objets ne peut être évalué.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
Chacune des colonnes avait dix-huit coudées de haut, un fil de douze coudées en mesurait le tour, et ses parois avaient une épaisseur de quatre doigts; l’intérieur était creux.
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
Elle était surmontée d’un chapiteau d’airain; chaque chapiteau était haut de cinq coudées. Un treillage et des grenades entouraient le chapiteau, le tout fait d’airain. Il en était de même de la seconde colonne, également garnie de grenades.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
Les grenades qui apparaissaient sur le côté étaient au nombre de quatre-vingt seize; en réalité, le total des grenades qui entouraient le treillage s’élevait à cent.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
Le chef des gardes s’assura de la personne de Seraïa, le grand-prêtre, de Cefania, le grand-prêtre suppléant, et des trois gardiens du seuil.
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
Parmi les habitants de la ville, il arrêta un officier, préposé aux gens de guerre, sept des conseillers intimes du roi qui furent surpris dans la ville, le secrétaire, chef du recrutement, chargé d’enrôler la population du pays, ainsi que soixante hommes de cette population, qui se trouvaient dans la ville.
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
Nebouzaradan, chef des gardes, emmena tous ces prisonniers et les conduisit au roi de Babylone à Ribla.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
Le roi de Babylone les fit frapper et mettre à mort à Ribla. dans le district de Hamat, C’Est ainsi que Juda fut exilé de son territoire.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
Voici le chiffre de la population que Nabuchodonosor emmena en exil dans la septième année de son règne trois mille vingt-trois Judéens;
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
dans la dix-huitième année du règne de Nabuchodonosor, il emmena de Jérusalem huit cent trente-deux personnes;
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
dans la vingt-troisième année du règne de Nabuchodonosor, Nebouzaradan, chef des gardes, envoya en captivité sept cent quarante cinq Judéens: ce qui donne un total de quatre mille six cents hommes.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
La trente-septième année de l’exil de Joïachin, roi de Juda, le douzième mois et le vingt-cinquième jour du mois, Evil-Merodac, roi de Babylone, gracia Joïachin, roi de Juda, et le fit sortir de la maison de détention.
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
Il lui parla avec bonté, et lui donna un siège placé au-dessus du siège des rois qui étaient avec lui à Babylone.
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
Il lui fit changer ses vêtements de détention et l’admit constamment à sa table, toute sa vie durant.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
Son entretien, entretien permanent, lui fut assuré tant qu’il vécut de la part du roi de Babylone, suivant les besoins de chaque jour, jusqu’au moment de sa mort.

< Yeremiya 52 >