< Yeremiya 52 >
1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Zedekiah was one and twenty years old when he began to reign, and he reigned eleven years in Jerusalem. The name of his mother was Hamutal, the daughter of Jeremiah of Libnah.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
And he did that which was evil in the eyes of Jehovah, according to all that Jehoiakim had done.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
For, through the anger of Jehovah, it was so with Judah and Jerusalem that at length he cast them forth from his presence. And Zedekiah rebelled against the king of Babylon.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
And it came to pass in the ninth year of his reign, in the tenth month, in the tenth day of the month, that Nebuchadnezzar, the king of Babylon, came, he and all his army, against Jerusalem, and encamped against it, and built forts against it round about.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
And the city was besieged until the eleventh year of King Zedekiah.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
And in the fourth month, in the ninth day of the month, the famine was sore in the city, so that there was no bread for the people of the land.
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
And the city was broken into; and all the men of war fled, and went out of the city by night, by the way of the gate between the two walls, which is by the king's garden, (whilst the Chaldaeans were by the city round about, ) and they went toward the plain.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
But the army of the Chaldaeans pursued the king, and overtook Zedekiah in the plains of Jericho; and all his army was scattered from him.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
And they took the king, and carried him up to the king of Babylon, to Riblah, in the land of Hamath; where he gave judgment upon him.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
And the king of Babylon slew the sons of Zedekiah before his eyes. He slew also all the princes or Judah, in Riblah.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
And he put out the eyes of Zedekiah, and bound him in chains; and the king of Babylon carried him to Babylon, and put him in prison till the day of his death.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
And in the fifth month, on the tenth day of the month, (it was the nineteenth year of the reign of Nebuchadnezzar, the king of Babylon, ) came Nebuzaradan, captain of the guard, one that stood in the presence of the king of Babylon, to Jerusalem.
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
And he burned the house of Jehovah, and the king's house; and all the houses at Jerusalem, all the great houses, burned he with fire.
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
And all the army of the Chaldaeans that was with the captain of the guard brake down all the walls of Jerusalem round about.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
And some of the poor of the people, and the rest of the people that were left in the city, and the deserters that had gone over to the king of Babylon, even the remainder of the multitude, did Nebuzaradan, the captain of the guard, carry away captive.
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
But some of the poor of the land did Nebuzaradan, the captain of the guard, leave for vine-dressers and for husbandmen.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
And the pillars of brass that were in the house of Jehovah, and the bases, and the brazen sea that was in the house of Jehovah, the Chaldaeans brake, and carried all the brass of them to Babylon.
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
The caldrons also, and the shovels, and the snuffers, and the bowls, and the pans, and all the vessels of brass which were used in ministering, did they take away.
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
And the basins, and the fire-pans, and the bowls, and the caldrons, and the candlesticks, and the censers, and the cups, and whatever was of gold or silver, did the captain of the guard take away.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
The two pillars, the sea, and the twelve brazen bulls that were under the bases, which King Solomon made in the house of Jehovah, the brass from all these was beyond weight.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
For as to the pillars, eighteen cubits in height was the one pillar, and a line of twelve cubits measured it round, and their thickness was four fingers, being hollow.
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
And a chapiter of brass was upon them; and the height of one chapiter was five cubits; and there was network with pomegranates upon the chapiter all round, the whole of brass. The second pillar also, and the pomegranates, were like unto these.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
And the pomegranates were ninety and six toward every wind; all the pomegranates were a hundred upon the network round about.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
And the captain of the guard took Seraiah, the chief priest, and Zephaniah, the second priest, and the three keepers of the door;
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
and out of the city he took a eunuch who had charge over the men of war, and seven men of those that were near the king's person, who were found in the city, and the principal scribe of the host, who mustered the people of the land, and threescore men of the people of the land, who were found in the midst of the city;
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
these, Nebuzaradan, captain of the guard, took, and brought to the king of Babylon at Riblah.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
And the king of Babylon smote them, and put them to death in Riblah in the land of Hamath. Thus was Judah carried away captive out of their own land.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
This is the people whom Nebuchadnezzar carried away captive: in the seventh year, three thousand and twenty-three Jews;
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
in the eighteenth year of Nebuchadnezzar, he carried away captive from Jerusalem eight hundred and thirty-two persons;
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
in the three and twentieth year of Nebuchadnezzar, Nebuzaradan, captain of the guard, carried away captive of the Jews seven hundred forty and five persons. All the persons were four thousand and six hundred.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
And it came to pass in the thirty and seventh year of the captivity of Jehoiachin, the king of Judah, in the twelfth month, on the twenty-fifth day of the month, that Evil-merodach, the king of Babylon, in the first year of his reign, lifted up the head of Jehoiachin, king of Judah, and brought him forth out of prison,
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
and spoke kindly to him, and set his seat above the seat of the kings that were with him in Babylon,
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
and changed his prison garments; and he ate bread before him all the days of his life.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
And a constant allowance was given him by the king of Babylon, a portion every day, until the day of his death, all the days of his life.