< Yeremiya 52 >
1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
One and twenty years was Zedekiah old when he became king, and eleven years did he reign in Jerusalem. And his mother's name was Chamutal the daughter of Jeremiah of Libnah.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
And he did what is evil in the eyes of the Lord, in accordance with all that Jehoyakim had done.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
For through the anger of the Lord it came to pass against Jerusalem and Judah, till he had cast them out of his presence, that Zedekiah rebelled against the king of Babylon.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
And it came to pass in the ninth year of his reign, in the tenth month, on the tenth day of the month, that Nebuchadrezzar the king of Babylon came, he and all his army, against Jerusalem, and they encamped against it, and built against it works of attack round about.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
So the city was placed in a state of siege until the eleventh year of king Zedekiah.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
And in the fourth month, on the ninth day of the month, when the famine was severe in the city, so that there was no bread for the people of the land:
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
The city was broken in, and all the men of war fled, and went forth out of the city by night by the way of the gate between the two walls, which was near the king's garden; [while the Chaldeans were round about the city; ] and they went by the way of the plain.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
But the army of the Chaldeans pursued after the king, and they overtook Zedekiah in the plains of Jericho: and all his army was scattered from him.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
And they caught the king, and they brought him up unto the king of Babylon to Riblah in the land of Chamath: and he called him to account.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
And the king of Babylon slaughtered the sons of Zedekiah before his eyes: and also all the princes of Judah did he slaughter in Riblah.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
And the eyes of Zedekiah did he blind; and the king of Babylon bound him with brazen fetters, and carried him to Babylon, and put him in the ward-house till the day of his death.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
And in the fifth month, on the tenth day of the month, which was the nineteenth year of king Nebuchadrezzar the king of Babylon, came Nebuzaradan, the captain of the guard, [who] served the king of Babylon, unto Jerusalem.
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
And he burnt the house of the Lord, and the king's house: and all the houses of Jerusalem, and all the houses of the great men, did he burn with fire:
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
And all the walls of Jerusalem round about did all the army of the Chaldeans, that were with the captain of the guard, pull down.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
And certain of the poorest of the people, and the residue of the people that had been left in the city, and the deserters, that had run away to the king of Babylon, and the rest of the multitude, did Nebuzaradan the captain of the guard carry away into exile.
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
But certain of the poorest of the land did Nebuzaradan the captain of the guard leave for vine-dressers and for husbandmen.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
Also the pillars of copper that were in the house of the Lord, and the bases, and the copper sea that was in the house of the Lord, did the Chaldeans break, and they carried off all their copper to Babylon.
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
And the pots, and the shovels, and the knives, and the bowls, and the spoons, and all the vessels of copper wherewith they used to perform the service, did they take away.
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
And the basins, and the censers, and the bowls, and the pots, and the candlesticks, and the spoons, and the purifying-tubes: of what was of gold the gold, and of what was of silver the silver, did the captain of the guard take away.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
The two pillars, the one sea, and the twelve copper oxen that served instead of the bases, which king Solomon had made for the house of the Lord: the copper of all these vessels could not be weighed.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
And as regardeth the pillars, eighteen cubits was the height of each one pillar; and a thread of twelve cubits would compass it; and its thickness was four fingers: it was hollow.
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
And a capital was upon it of copper; and the height of the one capital was five cubits, with network and pomegranates upon the capital round about, all of copper. And the like was the case with the second pillar and the pomegranates.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
And the pomegranates were ninety and six on every side: all the pomegranates upon the network were one hundred round about.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
And the captain of the guard took Serayah the chief priest, and Zephanyah the priest second in rank, and the three door-keepers;
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
And out of the city he took a certain court-officer, who had the supervision of the men of war: and seven men of those that had free access to the kings presence, who were found in the city; and the scribe of the chief of the army, who ordered to the army the people of the land; and sixty men of the people of the land, that were found in the midst of the city;
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
And Nebuzaradan the captain of the guard took them, and led them away unto the king of Babylon to Riblah.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
And the king of Babylon smote them, and put them to death in Riblah in the land of Chamath. Thus Judah was carried away into exile out of his own country.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
This is the people whom Nebuchadrezzar carried away into exile: in the seventh year, three thousand and twenty and three Jews;
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
In the eighteenth year of Nebuchadrezzar from Jerusalem, eight hundred thirty and two persons;
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
In the three and twentieth year of Nebuchadrezzar, did Nebuzaradan the captain of the guard carry away into exile of the Jews seven hundred forty and five persons; all the persons were four thousand and six hundred.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
And it came to pass in the seven and thirtieth year of the exile of Jehoyachin the king of Judah, in the twelfth month, on the five and twentieth day of the month that Evil-merodach the king of Babylon in the [first] year of his reign lifted up the head of Jehoyachin the king of Judah, and brought him forth out of the prison-house;
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
And he spoke kindly with him, and set his throne above the throne of the kings that were with him in Babylon,
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
And he changed his prison-garments: and he ate bread before him continually all the days of his life.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
And his allowance was a continual allowance given him by the king, the necessary ration for the day on its day, until the day of his death, all the days of his life.