< Yeremiya 52 >

1 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
V jedenmecítma letech byl Sedechiáš, když počal kralovati, a jedenácte let kraloval v Jeruzalémě. Jméno matky jeho bylo Chamutal, dcera Jeremiášova z Lebna.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
I činil to, což jest zlého před očima Hospodinovýma, všecko tak, jakž byl dělal Joakim.
3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
Nebo se to dálo pro rozhněvání Hospodinovo proti Jeruzalému a Judovi, až je i zavrhl od tváři své. V tom zprotivil se Sedechiáš králi Babylonskému.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
Stalo se pak léta devátého kralování jeho, měsíce desátého, v desátý den téhož měsíce, že přitáhl Nabuchodonozor král Babylonský se vším vojskem svým k Jeruzalému, a položili se u něho, a vzdělali proti němu hradbu vůkol.
5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
A bylo město obleženo až do jedenáctého léta krále Sedechiáše.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
V kterémžto, měsíce čtvrtého, devátého dne téhož měsíce, rozmohl se hlad v městě, a neměl chleba lid země.
7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
I prolomeny jsou zdi městské, a všickni muži bojovní utekli, a vyšli z města v noci skrze bránu mezi dvěma zdmi, u zahrady královské, (Kaldejští pak leželi okolo města), a ušli cestou pouště.
8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
I honilo vojsko Kaldejské krále, a postihli Sedechiáše na rovinách Jerišských, a všecko vojsko jeho rozprchlo se od něho.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
A tak javše krále, přivedli ho k králi Babylonskému do Ribla v zemi Emat, kdežto učinil o něm soud.
10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
I zmordoval král Babylonský syny Sedechiášovy před očima jeho, ano i všecka knížata Judská zmordoval v Ribla.
11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
Oči pak Sedechiášovy oslepil, a svázav ho řetězy ocelivými král Babylonský, dal jej dovésti do Babylona, a dal jej do vězení až do dne smrti jeho.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
Potom měsíce pátého, desátého dne téhož měsíce, léta devatenáctého kralování Nabuchodonozora krále Babylonského, přitáhl Nebuzardan, hejtman nad žoldnéři, kterýž sloužíval králi Babylonskému, do Jeruzaléma.
13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
A zapálil dům Hospodinův, i dům královský, i všecky domy v Jeruzalémě, a tak všecky domy veliké vypálil ohněm.
14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
Všecky také zdi Jeruzalémské vůkol pobořilo všecko vojsko Kaldejské, kteréž bylo s tím hejtmanem nad žoldnéři.
15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Přitom z chaterného lidu, totiž ostatek lidu, kterýž byl zůstal v městě, i poběhlce, kteříž byli ustoupili k králi Babylonskému, a jiný obecný lid zavedl Nebuzardan, hejtman nad žoldnéři.
16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
Toliko něco chaterného lidu země zanechal Nebuzardan, hejtman nad žoldnéři, aby byli vinaři a oráči.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
Nadto sloupy měděné, kteříž byli v domě Hospodinově, i podstavky i moře měděné, kteréž bylo v domě Hospodinově, ztloukli Kaldejští, a odvezli všecku měď z nich do Babylona.
18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
Též hrnce. lopaty a nástroje hudebné, a kotlíky a kadidlnice, i všecky nádoby měděné, jimiž sloužili, pobrali.
19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
I medenice a nádoby k oharkům, s kotlíky a hrnci, a svícny, a kadidlnice a koflíky, a cožkoli zlatého a stříbrného bylo, pobral hejtman nad žoldnéři;
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
Sloupy dva, moře jedno, a volů dvanáct měděných, kteříž byli pod podstavky, jichž byl nadělal král Šalomoun do domu Hospodinova. Nebylo váhy mědi všech těch nádob.
21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
Nebo sloupů těch, osmnácti loket byla výška sloupu jednoho, kterýž okolek měl dvanácti loktů, ztlouští pak čtyř prstů byl dutý.
22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
A makovice na něm měděná, a makovice jedné výška pěti loket, a mřežování i jablka zrnatá na té makovici vůkol; všecko bylo měděné. Takovýž byl i sloup druhý s zrnatými jablky.
23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
A bylo jablek zrnatých devadesát a šest po každé straně; všudy jablek zrnatých bylo po stu na mřežování vůkol.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
Vzal také hejtman nad žoldnéři Saraiáše kněze předního, a Sofoniáše kněze nižšího, a tři strážné prahu.
25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
A z města vzal komorníka jednoho, kterýž byl hejtmanem nad muži bojovnými, a sedm mužů, jenž bývali při králi, kteříž nalezeni byli v městě, a předního spisovatele vojska, kterýž popisoval vojsko z lidu země, a šedesáte mužů z lidu země, kteříž nalezeni byli v městě.
26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
Zjímav tedy je Nebuzardan, hejtman nad žoldnéři, přivedl je k králi Babylonskému do Ribla.
27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
I pobil je král Babylonský, a zmordoval je v Ribla v zemi Emat, a tak zaveden jest Juda z země své.
28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
Tenť jest lid, kterýž zavedl Nabuchodonozor léta sedmého, Judských tři tisíce a třimecítma.
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
Léta osmnáctého Nabuchodonozora zavedl z Jeruzaléma duší osm set třidceti a dvě.
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
Léta třimecítmého Nabuchodonozora zavedl Nebuzardan, hejtman nad žoldnéři, Judské, duší sedm set čtyřidceti a pět, všech duší čtyry tisíce a šest set.
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
Stalo se také třidcátého sedmého léta po zajetí Joachina krále Judského, dvanáctého měsíce, dvadcátého pátého dne téhož měsíce, povýšil Evilmerodach král Babylonský toho léta, když počal kralovati, Joachina krále Judského, pustiv ho z žaláře.
32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
A mluvil s ním dobrotivě, i stolici jeho postavil nad stolice králů, kteříž s ním byli v Babyloně.
33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
Změnil též roucho jeho, kteréž měl v žaláři, a jídal chléb před ním vždycky, po všecky dny života svého.
34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
Nebo vyměřený pokrm ustavičně dáván byl jemu od krále Babylonského, a to na každý den, až do dne smrti jeho, po všecky dny života jeho.

< Yeremiya 52 >