< Yeremiya 51 >

1 Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
Sɛɛ na Awurade se: “Monhwɛ, mɛkanyan ɔsɛefo bi honhom atia Babilonia ne nnipa a wɔwɔ Leb Kamai.
2 Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
Mɛsoma ananafo akɔ Babilonia sɛ wonkohuhuw ne so na wɔnsɛe nʼasase; wobetia no wɔ afanan nyinaa wɔ nʼamanehunu da no.
3 Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
Mma agyantowni pema nʼagyan, mma ɔnhyɛ ne nkatabo. Mma ne mmerante mfa wɔn ho nni; sɛe nʼasraafo no pasaa.
4 Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
Wɔbɛhwehwe ase a wɔatotɔ wɔ Babilonia, a wɔapirapira yiye wɔ ne mmɔnten so.
5 Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
Na Israel Nyankopɔn, Asafo Awurade no, nnyaw Israel ne Yuda hɔ ɛ, ɛwɔ mu, afɔdi ahyɛ wɔn asase no so ma wɔ Israel Ɔkronkronni no anim.
6 “Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
“Munguan mfi Babilonia! Muntu mmirika mpere mo nkwa! Mommma wɔnnsɛe mo esiane ne bɔne nti. Awurade aweretɔbere aso; ɔde nea ɛfata no betua no ka.
7 Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
Na Babilonia yɛ sikakɔkɔɔ kuruwa wɔ Awurade nsam; ɔmaa asase nyinaa bow nsa. Aman no nom ne nsa; ɛno nti, afei wɔabobɔ adam.
8 Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
Babilonia bɛhwe ase abubu mpofirim. Muntwa ne ho agyaadwo! Mompɛ ne yaw no ano aduru; ebia ne ho bɛtɔ no.
9 Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
“‘Anka yɛbɛsa Babilonia yare, nanso wontumi nsa no yare; momma yennyaw no hɔ na obiara nkɔ nʼankasa asase so, efisɛ nʼatemmu du sorosoro; ɛforo soro te sɛ omununkum.’
10 “‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
“‘Awurade abu yɛn bem. Mommra, momma yɛnka wɔ Sion, nea Awurade, yɛn Nyankopɔn ayɛ.’
11 “Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
“Monsew agyan no ano! Momfa nkatabo no! Awurade ahwanyan Mede ahemfo no, efisɛ ne botae ne sɛ ɔbɛsɛe Babilonia. Awurade bɛtɔ were, ɔbɛtɔ were ama nʼasɔrefi no.
12 Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
Mompagyaw frankaa bi ntia Babilonia afasu! Mummia bammɔ mu, momma awɛmfo no nnyinagyina. Munsiesie ahintawee! Awurade bɛma nʼatirimpɔw aba mu, nea wahyɛ atia Babilonia no.
13 Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
Mo a motete nsuwansuwa bebree ho na nnwetɛbona abu mo so, mo awiei aba, bere a ɛsɛ sɛ wotwa mo kyene no.
14 Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
Asafo Awurade, aka ne ho ntam sɛ: mede nnipa bɛhyɛ wo ma sɛ tɛwtɛw, na wɔabɔ ose wɔ wo so.
15 “Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
“Ɔde ne tumi bɔɔ asase; ɔtoo wiase fapem wɔ ne nyansa mu na ɔde ne nhumu trɛw ɔsorosoro mu.
16 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
Sɛ ɔbobɔ mu a, ɔsoro nsu woro so; ɔma omununkum ma ne ho so fi nsase ano. Ɔsoma anyinam ka osu ho na ɔma mframa bɔ fi ne koradan mu.
17 “Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
“Onipa biara nnim nyansa, na onni nimdeɛ; sikadwumfo biara anim gu ase, esiane nʼahoni nti. Ne nsɛsode yɛ atoro; wonni ɔhome biara wɔ wɔn mu.
18 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
Wɔn so nni mfaso, wɔn ho yɛ serew; sɛ wɔn atemmu du so a, wɔbɛyera.
19 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Nea ɔyɛ Yakob Kyɛfa no nte sɛ eyinom, efisɛ ɔno ne ade nyinaa Yɛfo a Israel, abusua a ɛyɛ nʼagyapade nso ka ho. Asafo Awurade ne ne din.
20 “Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
“Woyɛ me ko abaa, mʼakode a mede kɔ sa mede wo dwerɛw amanaman, mede wo sɛe ahenni bebree,
21 ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
mede wo bobɔ ɔpɔnkɔ ne ne sotefo, teaseɛnam ne ne kafo,
22 Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
mede wo dwerɛw ɔbarima ne ɔbea, mede wo dwerɛw akwakoraa ne ɔbabun, mede wo dwerɛw aberante ne ababaa,
23 Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
mede wo dwerɛw oguanhwɛfo ne nguankuw, mede wo dwerɛw okuafo ne anantwi, mede wo dwerɛw amradofo ne adwumayɛfo.
24 “Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
“Metua Babilonia ne wɔn a wɔtete Babilonia ka wɔ mfomso a, wɔayɛ wɔ Sion nyinaa, wɔ wʼanim,” Awurade na ose.
25 “Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
“Bepɔw sɛefo, me ne wo anya, wo a wosɛe asase nyinaa no,” Awurade na ose. “Mɛteɛ me nsa wɔ wo so mepia wo afi abotan no so, na mayɛ wo sɛ bepɔw a ɛnka hwee.
26 Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
Wɔremfa ɔbo biara mfi wo so nyɛ tweatibo anaasɛ fapem mpo, efisɛ wobɛda mpan afebɔɔ,” Awurade na ose.
27 “Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
“Momma frankaa so wɔ asase no so! Monhyɛn torobɛnto no wɔ amanaman no mu! Munsiesie amanaman no mma wontu no so sa; Momfrɛfrɛ saa ahenni ahorow yi mma wɔnko ntia no: Ararat, Mini ne Askenas. Munnyi ɔsahene ntia no; momfa apɔnkɔ manyamanya te sɛ tɛwtɛw mmra.
28 Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
Munsiesie amanaman no mma wontu no so sa, mo Mede ahemfo, wɔn amradofo ne wɔn adwumayɛfo nyinaa, ne aman a wodi so nyinaa.
29 Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
Asase no wosow, na onukunuku ne mu, efisɛ Awurade atirimpɔw a etia Babilonia sɛ ɔbɛsɛe Babilonia asase a obiara rentumi ntena so no nsakraa ɛ.
30 Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
Babilonia dɔmmarima agyae ko wɔhyehyɛ wɔn aban mu. Wɔn ahoɔden asa; wɔayɛ sɛ mmea. Wɔatoto nʼatenae ahorow no mu gya, na wɔabubu nʼapon akyi adaban.
31 Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
Abɔfo didi so na asomafo didi so a wɔrekɔbɔ Babiloniahene amanneɛ se, wɔafa ne kuropɔn no,
32 Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
wɔagye asutwabea ahorow a ɛdeda asubɔnten no ano no afa, na wɔde ogya ato ɔwora no mu, na asraafo no abɔ huboa.”
33 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
Sɛɛ na Asafo Awurade, Israel Nyankopɔn, se: “Babilonia Babea ayɛ sɛ, awiporowbea wɔ bere a wɔretiatia hɔ. Aka kakraa bi, na bere a ɛsɛ sɛ wotwa no sɛ nnɔbae no adu.”
34 A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
“Babiloniahene Nebukadnessar adwerɛw yɛn, ɔde yɛn ato ɔhaw mu, wayɛ yɛn sɛ ahina a hwee nni mu. Wamene yɛn sɛ ɔwɔ no na ɔde yɛn nneɛma a ɛyɛ dɛ ahyɛ ne yafunu ma, na wapuw yɛn afi nʼanom agu.
35 Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
Ma ayakayakade a wɔde dii yɛn honam no mmra Babilonia so,” nnipa a wɔtete Sion na wɔka. “Ma yɛn mogya ngu wɔn a wɔtete Babilonia so,” Yerusalem na ɔka.
36 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
Enti sɛɛ na Awurade se: “Hwɛ, medi mo asɛm ama mo na matɔ were ama mo; Mɛma po a ɛyɛ ne de no ayow na mama ne nsubɔnten ayoyow.
37 Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
Babilonia bɛyɛ mmubui siw, sakraman atu ahodwiriwde ne fɛwdi, baabi a obiara nte.
38 Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
Ne nkurɔfo nyinaa bobɔ mu sɛ gyata, wɔbobɔ mu te sɛ gyatamma.
39 Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
Nanso bere a wɔahwanyan wɔn ho no, mɛto pon ama wɔn na mama wɔabobow nsa, sɛnea wɔde nteɛteɛmu bedi ahurusi, na wɔadeda a wɔrennyan bio,” Awurade na ose.
40 “Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
“Mede wɔn bɛba te sɛ nguantenmma a wɔrekokum wɔn, te sɛ adwennini ne mpapo.
41 “Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
“Sɛnea wɔbɛfa Sesak, wɔbɛfa asase nyinaa so ahohoahoa! Babilonia bɛyɛ ahodwiriwde wɔ amanaman no mu!
42 Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
Po bebunkam afa Babilonia so; na nʼasorɔkye bɛkata ne so.
43 Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
Ne nkurow bɛda mpan, nweatam a so awo, asase a obiara nte so, na obiara ntu kwan mfa so.
44 Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
Mɛtwe Bel aso wɔ Babilonia na mama wapuw nea wamene agu. Amanaman no rento santen nkɔ ne nkyɛn bio. Na Babilonia fasu bebubu.
45 “Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
“Me nkurɔfo, mumfi ne mu! Muntu mmirika mpere mo nkwa! Munguan mfi Awurade abufuwhyew ano.
46 Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
Mommma mo koma ntu na munnsuro sɛ mote huhuhuhu wɔ asase no so a; huhuhuhu ba afe yi na foforo ba afe a ɛbɛba, basabasayɛ ho huhuhuhu wɔ asase no so ɛfa ɔhene a ɔsɔre tia ɔfoforo ho.
47 Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
Na ampa ara bere no bɛba a mɛtwe Babilonia ahoni aso; nʼasase no nyinaa anim begu ase na nʼatɔfo nyinaa bɛtotɔ ase wɔ ne so.
48 Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
Ɔsoro ne asase ne nea ɛwɔ mu nyinaa de ahosɛpɛw bɛteɛ mu agu Babilonia so, efisɛ ɔsɛefo befi atifi fam abɛtow ahyɛ ne so,” Awurade na ose.
49 “Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
“Ɛsɛ sɛ Babilonia hwe ase, esiane Israel atɔfo nti sɛnea atɔfo a wɔwɔ wiase nyinaa ahwehwe ase esiane Babilonia nti no.
50 Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
Mo a mo aguan afi afoa ano, monkɔ, na monntwentwɛn mo nan ase! Monkae Awurade wɔ akyirikyiri asase so, na munnwen Yerusalem ho.”
51 Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
“Wɔagu yɛn anim ase, efisɛ wayeyaw yɛn na fɛre akata yɛn anim, efisɛ ananafo ahyɛn Awurade fi kronkronbea ahorow hɔ.”
52 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
“Nanso nna bi reba,” Awurade na ose, “a mɛtwe nʼahoni aso, na nʼasase so nyinaa apirafo besi apini.
53 Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
Sɛ Babilonia kɔka soro mpo, na omiamia nʼaban tenten bammɔ mu a, mɛsoma ɔsɛefo ne no abedi asi,” Awurade na ose.
54 “Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
“Osu nnyigyei bi fi Babilonia, ɔsɛe kɛse bi nnyigyei fi Babiloniafo asase so.
55 Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
Awurade bɛsɛe Babilonia; ɔbɛma nʼasotuatua nnyigyei no agyae. Atamfo a wɔte sɛ ahum betu sɛ nsu akɛse; wɔn mmubomu bɛyɛ gyegyeegye.
56 Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
Ɔsɛefo bi bɛsɔre atia Babilonia; wɔbɛfa ne dɔmmarima nnommum na wobebubu wɔn tadua mu. Efisɛ Awurade yɛ Onyankopɔn a ɔhyɛ anan mu; obetua so ka pɛpɛɛpɛ.
57 Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Mɛma nʼadwumayɛfo ne nʼanyansafo abow nsa nʼamradonom, ne mpanyimfo ne dɔmmarima nso saa ara; wɔbɛdeda afebɔɔ a wɔrennyan,” sɛɛ na ɔhempɔn a ne din ne Asafo Awurade, no se.
58 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
Sɛɛ na Asafo Awurade, se: “Wobedwiriw Babilonia afasu a ɛtrɛw no agu fam na wɔbɛto nʼapon atenten no mu gya; nnipa no haw wɔn ho kwa, ɔman no adwumayɛ ma ogya no dɛw mmom.”
59 Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
Eyi ne asɛm a Yeremia ka kyerɛɛ Neria babarima Seraia a ɔyɛ adwumayɛfo panyin na ɔyɛ Maseia nena no, bere a ɔne Yudahene Sedekia kɔɔ Babilonia wɔ nʼadedi afe a ɛto so anan no mu.
60 Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
Na Yeremia akyerɛw amanehunu a ɛbɛba Babilonia so no nyinaa agu nhoma mmobɔwee so, nea wakyerɛw a ɛfa Babilonia ho nyinaa.
61 Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
Ɔka kyerɛɛ Seraia se, “Sɛ wudu Babilonia a, hwɛ sɛ wobɛkenkan saa nsɛm yi nyinaa sɛnea obiara bɛte.
62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
Afei ka se, ‘Awurade, woaka se wobɛsɛe beae yi sɛnea onipa anaa aboa biara rentumi ntena so; na ɛbɛda mpan afebɔɔ.’
63 Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
Sɛ wokenkan nhoma mmobɔwee yi wie a, kyekyere fam ɔbo ho, na tow kyene Asubɔnten Eufrate mu.
64 Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.
Afei ka se, ‘Sɛɛ na Babilonia ne ne nkurɔfo bɛmem a wɔrensɔre bio, esiane amanehunu a mede bɛba ne so no nti.’” Yeremia nsɛm no awiei ni.

< Yeremiya 51 >