< Yeremiya 51 >

1 Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
Yahvé dice: “He aquí que yo me levantaré contra Babilonia, y contra los que habitan en Lebkamai, un viento destructor.
2 Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
Enviaré a Babilonia extraños que la aventarán. Vaciarán su tierra; porque en el día de la angustia estarán contra ella todos.
3 Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
Contra el que se dobla, que el arquero doble su arco, también contra el que se levanta con su cota de malla. ¡No le perdonen los jóvenes! ¡Destruyan por completo a todo su ejército!
4 Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
Caerán muertos en la tierra de los caldeos, y se empuja a través de sus calles.
5 Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
Porque Israel no está abandonado, ni Judá, por su Dios, por Yahvé de los Ejércitos; aunque su tierra está llena de culpa contra el Santo de Israel.
6 “Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
“¡Huye de en medio de Babilonia! ¡Todo el mundo salva su propia vida! No seas cortado en su iniquidad, porque es el tiempo de la venganza de Yahvé. Él le dará una recompensa.
7 Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
Babilonia ha sido una copa de oro en la mano de Yahvé, que emborrachó a toda la tierra. Las naciones han bebido de su vino; por eso las naciones se han vuelto locas.
8 Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
¡Babilonia ha caído repentinamente y ha sido destruida! ¡Llora por ella! Toma un bálsamo para su dolor. Tal vez pueda curarse.
9 Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
“Habríamos curado a Babilonia, pero no está curada. Abandónala, y que cada uno se vaya a su país; pues su juicio llega hasta el cielo, y se eleva hasta los cielos.
10 “‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
‘Yahvé ha producido nuestra justicia. Venid y anunciemos en Sión la obra de Yahvé, nuestro Dios’.
11 “Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
“¡Que las flechas estén afiladas! ¡Sujeta los escudos con firmeza! Yahvé ha agitado el espíritu de los reyes de los medos, porque su propósito es contra Babilonia, para destruirla; porque es la venganza de Yahvé, la venganza de su templo.
12 Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
¡Levanten un estandarte contra los muros de Babilonia! ¡Haz que el reloj sea fuerte! Poner a los vigilantes, y preparar las emboscadas; porque Yahvé se ha propuesto y ha hecho lo que dijo sobre los habitantes de Babilonia.
13 Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
Tú que habitas sobre muchas aguas, abundante en tesoros, ha llegado tu fin, la medida de tu codicia.
14 Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
Yahvé de los Ejércitos ha jurado por sí mismo, diciendo, ‘Seguramente te llenaré de hombres, como con las langostas, y levantarán un grito contra ti’.
15 “Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
“Él ha hecho la tierra con su poder. Él ha establecido el mundo por su sabiduría. Con su entendimiento ha extendido los cielos.
16 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
Cuando él emite su voz, hay un rugido de aguas en los cielos, y hace que los vapores asciendan desde los confines de la tierra. Hace relámpagos para la lluvia, y saca el viento de sus arcas.
17 “Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
“Todo hombre se ha vuelto estúpido y sin conocimiento. Todo orfebre se siente decepcionado por su imagen, porque sus imágenes fundidas son falsas, y no hay aliento en ellos.
18 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
Son vanidad, una obra de ilusión. En el tiempo de su visita, perecerán.
19 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
La porción de Jacob no es como éstas, porque él formó todas las cosas, incluyendo la tribu de su herencia. Yahvé de los Ejércitos es su nombre.
20 “Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
“Vosotros sois mi hacha de combate y mis armas de guerra. Contigo romperé las naciones en pedazos. Con ustedes destruiré reinos.
21 ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
Contigo romperé en pedazos el caballo y su jinete.
22 Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
Contigo romperé en pedazos el carro y el que va en él. Contigo me romperé en pedazos hombre y mujer. Contigo me romperé en pedazos el viejo y el joven. Contigo me romperé en pedazos el joven y la virgen.
23 Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
Contigo romperé en pedazos el pastor y su rebaño. Contigo me romperé en pedazos el agricultor y su yugo. Contigo me romperé en pedazos gobernadores y diputados.
24 “Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
“Le devolveré a Babilonia y a todos los habitantes de Caldea todo el mal que han hecho en Sión a tus ojos”, dice el Señor.
25 “Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
“He aquí que estoy contra ti, montaña destructora”, dice Yahvé, “que destruye toda la tierra. Extiendo mi mano sobre ti, te bajan de las rocas, y te convertirá en una montaña quemada.
26 Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
No te quitarán una piedra angular, ni una piedra para los cimientos; pero tú estarás desolado para siempre”, dice Yahvé.
27 “Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
“¡Poned un estandarte en la tierra! ¡Toca la trompeta entre las naciones! ¡Preparen a las naciones contra ella! ¡Convoca contra ella a los reinos de Ararat, Minni y Ashkenaz! ¡Nombrar a un mariscal contra ella! ¡Haz que los caballos suban como las langostas enjambre!
28 Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
Prepara contra ella a las naciones, ¡los reyes de los medos, sus gobernadores, y todos sus diputados, y toda la tierra de su dominio!
29 Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
La tierra tiembla y sufre; para los propósitos de Yahvé contra Babilonia se mantienen, para convertir la tierra de Babilonia en una desolación, sin habitantes.
30 Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
Los poderosos de Babilonia han dejado de luchar, permanecen en sus fortalezas. Su poderío ha fracasado. Se han convertido en mujeres. Sus moradas son incendiadas. Sus barras están rotas.
31 Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
Un corredor correrá al encuentro de otro, y un mensajero para encontrarse con otro, para mostrar al rey de Babilonia que su ciudad está tomada por todos los lados.
32 Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
Así que los pasajes se apoderan. Han quemado las cañas con fuego. Los hombres de guerra están asustados”.
33 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
Porque Yahvé de los Ejércitos, el Dios de Israel dice: “La hija de Babilonia es como una era en el momento en que se pisa. Todavía un poco, y el tiempo de la cosecha viene para ella”.
34 A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
“Nabucodonosor, rey de Babilonia, me ha devorado. Me ha aplastado. Me ha convertido en un recipiente vacío. Él, como un monstruo, me ha tragado. Se ha llenado la boca con mis delicias. Me ha expulsado.
35 Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
¡Que la violencia hecha a mí y a mi carne sea sobre Babilonia!” el habitante de Sion dirá; y, “¡Que mi sangre sea sobre los habitantes de Caldea!” dirá Jerusalén.
36 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
Por eso dice Yahvé: “He aquí que yo defenderé tu causa, y me vengaré por ti. Secaré su mar, y hacer que su fuente se seque.
37 Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
Babilonia se convertirá en un montón, una morada para los chacales, un asombro, y un silbido, sin habitante.
38 Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
Rugirán juntos como leones jóvenes. Gruñirán como cachorros de león.
39 Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
Cuando se inflamen, haré su fiesta, y los emborracharé, para que se alegren, y dormir un sueño perpetuo, y no despertar”, dice Yahvé.
40 “Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
“Los haré caer como corderos al matadero, como los carneros con los machos cabríos.
41 “Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
“¡Cómo se lleva a Sheshach! ¡Cómo se apodera la alabanza de toda la tierra! ¡Cómo se ha convertido Babilonia en una desolación entre las naciones!
42 Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
El mar ha subido sobre Babilonia. Está cubierta por la multitud de sus olas.
43 Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
Sus ciudades se han convertido en una desolación, una tierra seca, y un desierto, una tierra en la que no habita ningún hombre. Ningún hijo de hombre pasa por ella.
44 Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
Ejecutaré el juicio sobre Bel en Babilonia, y sacaré de su boca lo que se ha tragado. Las naciones no fluirán más hacia él. Sí, el muro de Babilonia caerá.
45 “Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
“Pueblo mío, aléjate de en medio de ella, y cada uno de ustedes se salve de la feroz ira de Yahvé.
46 Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
No dejes que tu corazón desfallezca. No temas por las noticias que se escucharán en la tierra. Para las noticias vendrá un año, y después de eso en otro año vendrán las noticias, y la violencia en la tierra, gobernante contra gobernante.
47 Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
Por tanto, he aquí que vienen días en que ejecutaré el juicio sobre las imágenes grabadas de Babilonia; y toda su tierra será confundida. Todos sus muertos caerán en medio de ella.
48 Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
Entonces los cielos y la tierra, y todo lo que hay en ella, cantará de alegría sobre Babilonia; porque los destructores vendrán a ella desde el norte”, dice Yahvé.
49 “Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
“Como Babilonia ha hecho caer a los muertos de Israel, así que los muertos de toda la tierra caerán en Babilonia.
50 Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
Tú que has escapado de la espada, ¡ve! ¡No te quedes quieto! Recuerda a Yahvé desde lejos, y deja que Jerusalén entre en tu mente”.
51 Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
“Estamos confundidos porque hemos escuchado reproches. La confusión ha cubierto nuestros rostros, porque han entrado extraños en los santuarios de la casa de Yahvé”.
52 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
“Por lo tanto, he aquí que vienen los días”, dice Yahvé, “que ejecutaré el juicio sobre sus imágenes grabadas; y por toda su tierra gemirán los heridos.
53 Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
Aunque Babilonia se eleve hasta el cielo, y aunque deba fortificar la altura de su fuerza, pero vendrán a ella destructores de mi parte”, dice Yahvé.
54 “Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
“El sonido de un grito viene de Babilonia, ¡y de gran destrucción de la tierra de los caldeos!
55 Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
Porque Yahvé arrasa con Babilonia, ¡y destruye de ella la gran voz! Sus olas rugen como muchas aguas. El ruido de su voz es pronunciado.
56 Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
Porque el destructor ha venido sobre ella, incluso en Babilonia. Sus poderosos hombres han sido tomados. Sus arcos están rotos en pedazos, porque Yahvé es un Dios de retribución. Seguramente lo pagará.
57 Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Haré de ella príncipes y sabios, sus gobernantes, sus diputados y sus poderosos hombres borrachos. Dormirán un sueño perpetuo, y no despertar,” dice el Rey, cuyo nombre es Yahvé de los Ejércitos.
58 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
El Señor de los Ejércitos dice: “Los anchos muros de Babilonia serán completamente derribados. Sus altas puertas serán quemadas con fuego. Los pueblos trabajarán por la vanidad, y las naciones para el fuego; y se cansarán”.
59 Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
Palabra que el profeta Jeremías ordenó a Seraías, hijo de Nerías, hijo de Maseías, cuando fue con Sedequías, rey de Judá, a Babilonia, en el cuarto año de su reinado. Seraías era jefe de intendencia.
60 Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
Jeremías escribió en un libro todos los males que vendrían sobre Babilonia, y todas estas palabras que están escritas sobre Babilonia.
61 Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
Jeremías dijo a Seraías: “Cuando llegues a Babilonia, procura leer todas estas palabras,
62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
y di: ‘Señor, tú has hablado sobre este lugar, para cortarlo, para que nadie habite en él, ni hombre ni animal, sino que sea desolado para siempre’.
63 Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
Cuando termines de leer este libro, atarás una piedra y la arrojarás en medio del Éufrates.
64 Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.
Entonces dirás: ‘Así se hundirá Babilonia y no volverá a levantarse a causa del mal que le haré pasar; y se cansarán’.” Hasta aquí las palabras de Jeremías.

< Yeremiya 51 >