< Yeremiya 51 >
1 Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
LEUM GOD El fahk, “Nga ac oru sie eng upa in tuhyak ac kunausla acn Babylonia ac mwet we.
2 Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
Nga ac supwala mwetsac in kunausla acn Babylonia, oana ke eng uh okla kulun wheat uh. Ke len in ongoiya sac, un mwet mweun ac tuku yen nukewa me, ac usla koanon acn we.
3 Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
Nikmet sang pacl lun mwet mweun Babylonia in pisrik mwe pisr natulos, ku in nokomang nuknuk in mweun lalos. Sukela mwet mweun nukewa we — mwet fusr ac mwet matu!
4 Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
Elos ac fah kineta ac misa ke inkanek in siti selos.
5 Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
Oasr mwatan mwet Israel ac Judah ke elos nukewa tuh orekma koluk lainyu, Nga Su Mutallana lun Israel. Ne ouinge, nga LEUM GOD Kulana tiana som lukelos.
6 “Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
Kaingla liki Babylonia! Kaing tuh kowos in moul. Nimet oru kowos in misa ke sripen ma koluk lun mwet Babylonia, mweyen nga fah oru foloksak luk inge, ac kalyaelos fal nu ke orekma koluk lalos.
7 Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
Babylonia el tuh oana sie cup gold inpouk, ac oru tuh faclu nufon sruhila. Mutunfacl pus numla wain nimal ac wella.
8 Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
Acn Babylonia sa na ikori ac kunausyukla! Kowos in tung kacl, ac suk ono in unwela kinet kacl. Sahp el ac ku in kwela!
9 Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
Mwetsac su muta we elos fahk, ‘Kut tuh srike in kasru acn Babylonia, tusruktu arulana pahtlac. Tari kut folokla nu yen sesr. God El kalyei Babylonia ke ku lal nufon, ac sukela acn we.”’
10 “‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
LEUM GOD El fahk, “Mwet luk elos wowoyak ac fahk, ‘LEUM GOD El fahkak lah kut pa suwohs uh. Lela kut in som ac fahk nu sin mwet Jerusalem ma LEUM GOD lasr El orala!”’
11 “Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
LEUM GOD El purakak tokosra lun Media, mweyen El nunku Elan kunaus acn Babylonia. Pa ingan ma El ac oru in folokin musalla lun Tempul lal. Mwet kol lun un mwet mweun uh sapkin, “Kowos tamla mwe pisr nutuwos an! Akola mwe loang lowos!
12 Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
Kolak sie flag in akkalemye lah pacl in mweuni pot Babylon. Akpusyela mwet san! Oakiya kais sie u nu yen elos ac karingin. Supwala mwet in wikwik soano mwet lokoalok. LEUM GOD El orala ma El fahk mu El ac oru nu sin mwet Babylonia.
13 Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
Pukanten infacl ac mwe kasrup in facl sac, tusruktu sun pacl in safla lal. Moul lun Babylonia ac wutiyukla na pwaye.
14 Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
LEUM GOD Kulana El fulahk ke moul lal sifacna mu El fah use mwet puspis in mweuni acn Babylonia oana sie u in locust, ac elos fah sasa ke kutangla lalos.
15 “Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
LEUM GOD El orala faclu ke ku lal; El oakiya faclu ke lalmwetmet lal, Ac El asroelik kusrao ke etu lal.
16 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
Ke sap lal, kof lucng liki yen engyeng uh ngirngir; El orama pukunyeng uh liki saflaiyen faclu. El oru sarom in sarmelik in af uh Ac supwama eng uh liki nien filma lal.
17 “Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Ke mwet uh liye ma inge, elos akilen lupan lalfon ac nikin lalos sifacna. Elos su oru ma sruloala elos mwekinla, Mweyen god ma elos orala uh tia pwaye ac wangin moul la.
18 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
Elos ma lusrongten ac fal in pilesreyuk. Elos ac fah kunausyukla pacl se LEUM GOD El tuku in nununkalos.
19 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
God lal Jacob El tia oana ma inge. El pa orala ma nukewa, Ac El sulela mwet Israel elos in mwet lal. Inel pa LEUM GOD Kulana.
20 “Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
LEUM GOD El fahk, “Babylonia, kom hammer nutik, kufwen mwe mweun nutik. Nga orekmakin kom in tuktukya mutunfacl ac tokosrai.
21 ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
Keim nga kunausla horse ac mwet kasrusr fac, Nga kunausla chariot ac mwet kasrusr fac.
22 Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
Keim nga uniya mukul ac mutan, Nga akmuseya mwet matu ac mwet fusr, Nga uniya tulik mukul ac tulik mutan.
23 Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
Keim nga onela mwet shepherd ac un kosro natulos, Nga onela pac mwet ima ac ox natulos. Keim nga tuktukya mwet kol fulat ac mwet pwapa fulat.”
24 “Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
LEUM GOD El fahk, “Kowos fah liye ke nga ac oru foloksak nu sin Babylonia ac mwet we ke orekma koluk nukewa elos oru nu sin Jerusalem.
25 “Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
Babylonia, kom oana soko fineol ma kunausla faclu nufon, tusruktu nga, LEUM GOD, lain kom. Nga fah sruokkomi, aktupasrpasryekomla, ac filikomla in oan apatla.
26 Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
Wangin eot ke mahnum sum fah sifil orekmakinyuk nu ke musa lohm. Kom ac fah oana sie acn mwesis nwe tok. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.
27 “Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
“Kolak sie mwe akul ac ukya mwe ukuk tuh mutunfacl uh in lohng lah pacl in mweun! Akoela mutunfacl uh in mweun lain Babylonia! Pangoneni tokosrai lun Ararat, Minni, ac Ashkenaz elos in sroang wi mweun. Srisrngia sie mwet fulat in kol mweun an. Use horse uh in pukanten oana un locust.
28 Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
Akola mutunfaclu in mweun lain Babylonia. Sapla nu sin tokosra lun acn Media, wi mwet kol ac mwet fulat lalos, ac un mwet mweun lun facl nukewa elos leumi.
29 Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
Faclu kusrusr ac rarrar mweyen LEUM GOD El akfahsrye pwapa lal in oru Babylonia in sie acn mwesisla, yen wangin mwet fah muta we.
30 Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
Mwet mweun watwen lun acn Babylonia elos tia illa in mweun, a elos mutana in pot ku lalos. Wanginla pulaik lalos ac elos sangeng oana mutan uh. Mwet lokoalok elos fukulya mutunpot lun siti uh ac furreak lohm we.
31 Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
Mwet utuk kas uh kasrusr atutafi ke pweng nu sin tokosra lun Babylonia, lah acn nukewa ke siti sel uh musalsalu.
32 Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
Mwet lokoalok elos sruokya acn in tupalla infacl uh, ac esukak pot ku nukewa lun acn we. Mwet mweun lun Babylonia elos arulana tuninfongla.
33 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
Ac tia paht mwet lokoalok lalos fah pakelosi ac fotongolosi oana wheat ke acn in kulkul wheat. Nga, LEUM GOD Kulana, God lun Israel, pa fahk ma inge.”
34 A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
Tokosra lun Babylonia el sipsipikya Jerusalem Ac kangla. El okoala koanon siti sac oana sufa soko; El okomla acn we oana soko kosro lulap sulallal. El kangla ma el lungse kac Ac filakunla ma ngia.
35 Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
Lela mwet Zion uh in fahk, “Mwatan orekma sulallal ma tuh orek nu sesr In oan fin Babylonia!” Lela mwet Jerusalem in fahk, “Mwatan mwe keok nukewa ma orek nu sesr In oan fin Babylonia!”
36 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
Na LEUM GOD El fahk nu sin mwet Jerusalem, “Nga fah aol kowos in kwafe keiwos, ac orek foloksak nu sin mwet lokoalok lowos ke ma elos tuh oru nu suwos. Nga fah oru in wanginla kof in acn Babylonia, ac infacl nukewa we in mihnla.
37 Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
Facl sac fah ekla sie yol in kutkut, yen kosro lemnak mukena muta we. Wangin mwet ac fah muta we, ac mwet nukewa su liye facl sac ac fah fwefela ac arulana sangeng.
38 Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
Mwet Babylonia nukewa ngutngut oana lion, ac kou oana lion fusr.
39 Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
Ya elos kainmongo? Nga fah akoo sie kufwa nu selos ac oru elos in sruhila ac engan. Na elos ac motulla ac fah tia sifil ngutalik.
40 “Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Nga fah usalosla in anwuki, oana sheep fusr, nani, ac sheep mukul. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.”
41 “Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
LEUM GOD El fahk ke acn Babylon: “Siti se ma faclu nufon tuh kaksakin, inge kutangyukla, ac ekla sie acn arulana mwe aksangeng nu sin mutunfaclu in liye.
42 Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
Noa ngirngir meoa uh toki nu fin Babylon ac afunla.
43 Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
Inkul ma apkuran nu we sikiyukla acn mwesisla, yen wangin mwet muta we ku forfor we.
44 Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
Nga fah kael Bel, god lun Babylonia, ac eisla liki inwalul ma nukewa ma el ukumya. Mutunfacl uh ac fah tia sifilpa alu nu sel. “Pot lun acn Babylon mokukla.
45 “Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
Mwet Israel, kaing liki acn ingan! Kaing tuh kowos in moulla liki kasrkusrak lulap luk.
46 Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
Nimet fuhleak finsrak lowos ku sangeng ke sramsram lusrongten kowos lohng. Yac nukewa oasr sramsram lusrongten ac fwackelik, ke mwet sulallal in facl suwos, ac ke sie tokosra lain sie pac tokosra.
47 Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
Ke ma inge pacl se ac fah tuku ke nga ac oru ma nga akoo in oru nu ke ma sruloala lun Babylonia. Mutunfacl sac nufon ac fah akmwekinyeyuk, ac mwet we nukewa ac fah anwuki.
48 Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
Ma nukewa fin faclu ac yen engyeng uh fah sasa ke engan pacl se Babylonia putatyang nu inpoun mwet su tuku epang me in kunausulla.
49 “Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
Acn Babylonia ac fah ikori mweyen el uniya mwet puspis fin faclu, ac oayapa uniya mwet puspis sin mwet Israel. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.”
50 Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
LEUM GOD El fahk nu sin mwet lal in acn Babylonia: “Kowos su kaingla liki misa, kowos som! Nimet soano! Kowos finne muta loesla liki acn suwos, nunku keik, LEUM GOD lowos, ac esam acn Jerusalem.
51 Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
Kowos fahk mu, ‘Kut mwekinla ac tonongla, ac pula mu wangin ma kut ku in oru, mweyen mwet in mutunfacl saya elos utyak ac aktaekyela acn mutal in Tempul.’
52 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
Ke ma inge, nga fahk mu oasr pacl se ac tuku ke nga ac oru ma nga akoo in oru nu ke ma sruloala lun Babylonia, ac mwet kinet uh ac sasao yen nukewa fin facl sac.
53 Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
Babylon finne ku in fanyak nu yen engyeng uh ac musai sie pot ku we, nga ac nuna supwala mwet in kunausla. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.”
54 “Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
Na LEUM GOD El fahk, “Lohng pusren tung in Babylon, Pusren mwemelil ke sripen sikiyukla facl sac.
55 Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
Inge nga kunausla acn Babylon Ac oru in wanginla pusracl. Fwilin mwet mweun uh sasak nu we oana fwilin noa. Elos sasa ke elos mweuni acn we.
56 Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
Elos tuku in kunausla Babylon. Mwet mweun we sruoh, Ac mwe pisr natulos kotkot uh. Nga sie God su kai mwet su orekma koluk, Ac nga fah folokin nu sin Babylon fal nu ke ma el orala.
57 Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Nga fah oru mwet fulat we in sruhila — Mwet lalmwetmet, mwet kol, ac mwet mweun. Elos ac motulla ac tia sifil ngutalik. Nga, tokosra, pa fahk ma inge. Nga LEUM GOD Kulana.
58 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
Pot sralap lun Babylon ac fah rakinyuki nu infohk uh, Ac mutunpot fulat we isisyak. Kemkatu lun mutunfacl puspis wangin sripa; Orekma upa lalos firiryak. Nga, LEUM GOD Kulana, pa fahk ma inge.”
59 Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
Seraiah, mwet tutaf lal Tokosra Zedekiah, el wen natul Neriah ac nutin natul Mahseiah. In yac se akakosr ma Zedekiah el tokosra lun Judah, Seraiah el tuh welul som nu Babylonia, ac nga tuh sapkin ma elan oru.
60 Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
Nga simusla in book se ma nukewa ma ac sikyak ke ac kunanula acn Babylonia, oayapa mwe fahkak puspis saya ke acn we.
61 Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
Nga fahk nu sel Seraiah, “Pacl se kom ac sun acn Babylon, aklohya riti ma nukewa simla in book se inge mwet uh in lohng.
62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
Toko kom pre ac fahk, ‘LEUM GOD, kom fahk mu kom ac kunausla acn se inge tuh in wangin kutena ma moul muta fac, tia mwet ku ma orakrak, a ac fah oana sie acn mwesis nwe tok.’
63 Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
Seraiah, kom fin riti book se inge nu sin mwet uh nwe safla, na kom kapriya nu ke sie eot an, ac sisla nu Infacl Euphrates,
64 Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.
ac fahk, ‘Pa inge ma ac sikyak nu sin Babylonia — el ac tili ac tia sifil otyak ke sripen kunausten lulap su LEUM GOD El ac oru nu sin acn we.”’ Kas lal Jeremiah safla inse.